< Aefeso 1 >

1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu. Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:
O PAULO, he lunaolelo a Iesu Kristo ma ka makemake o ke Akua, na ka poe haipule e noho ana ma Epeso, a me ka poe manaoio iloko o Iesu Kristo:
2 Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
E alohaia oukou, e maluhia hoi i ke Akua ko kakou Makua, a me ka Haku Iesu Kristo.
3 Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu.
E hoomaikaiia ku ke Akua, ka Makua o ko kakou Haku o Iesu Kristo, nana kakou i hoomaikai mai ma na mea maikai a pau o ka Uhane i na wahi lani ma o Kristo la.
4 Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake,
E like me ia i wae mai ai ia kakou ma ona la mamua aku o ka hookumuia mai o ke ao nei i hemolele ai kakou a me ka hala ole imua ona ma ke aloha:
5 Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake.
I koho e mai oia ia kakou mamua no ka hookamaia nana ma o Iesu Kristo la, e like me ka lokomaikai o kona makemake,
6 Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda.
I hoomaikaiia'i ka nani o kona aloha, ana i maliu mai ai ia kakou no ka Mea aloha;
7 Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu
Nona mai ke ola ia kakou ma kona koko, ke kala ana o na hala, e like me ka lako o kona lokomaikai;
8 chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso,
Ka mea ana i hoomahuahua mai ai ia kakou me ke akamai nui, a me ka naauao.
9 Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake.
Ua hoike mai la oia ia kakou i ka mea ikea ole o koua makemake, e like me kona manao aloha ana i manao ai iloko iho ona;
10 Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.
I ke aupuni o keia manawa hope, e houluulu i na mea a pau ma kahi hookahi iloko o Kristo, i na mea o ka lani e me na mea o ka honua, iloko ona.
11 Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake,
Ma ona la ua loaa mai ia ma kou ka noho ana, i koho mua ia mai makou o like me ka manao o ka mea nana e hana mai i na mea a pau ma ka manao ku paa o kona makemake;
12 nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake.
I hoomaikai aku ai makou i kona nani, ka poe i manao lana e mamua i ka Mesia.
13 Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza.
O oukou hoi kekahi i manao ia ia, i ko oukou hoolohe ana i ka olelo o ka oiaio, i ka euanelio e ola'i oukou; a i ko oukou manaoio ana ia ia, ua hoailonaia oukou e ka Uhane Hemolele i olelo e ia mai;
14 Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.
Oia ka hooiaio o ko kakou noho ana, a hiki aku i ke ola i kuaiia mai, i hoomaikaiia'i kona nani.
15 Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse,
Nolaila hoi, i kuu lohe ana'ku i ko oukou manaoio i ka Haku ia Iesu, a me ke aloha i na haipule a pau.
16 ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga.
Aole au e hooki i ka hoomaikai ana aku no oukou, e hoohiki ana ia oukou ma ka'u pule;
17 Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni.
I haawi mai ai ke Akua o ko kakou Haku o Iesu Kristo, ka Makua nona ka nani, ia oukou i ka Uhane hoonaauao a me ka hoike, i ike ai oukou ia ia;
18 Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima.
A hoomalamalamaia na maka o ko oukou naau, i ike ai oukou i ka manaolana ma kona hea ana mai, a me ka nani nui o kona mea e ili mai ana no ka poe haipule,
19 Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija
A me ka nui loa o kona mana no kakou ka poe manaoio, ma ka hooikaika ana o kona mana ikaika,
20 imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba.
Ana i hana iho ai iloko o Kristo i ka hoala'ua ia ia mai ka make mai, a hoonoho iho la ia ia ma kona lima akau i kahi lani,
21 Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. (aiōn g165)
Maluna ae o na alii a pau, o na mea ikaika, o na mea mana, na haku, a me na inoa a pau i kapaia, aole ma keia ao wale no, ma kela ao e hiki mai ana kekahi. (aiōn g165)
22 Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo,
A ua hoolilo iho la oia i na mea a pau malalo iho o kona mau wawae, ua hoonoho hoi ia ia i poo maluna o na mea a pau no ka ekalesia,
23 umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.
Oia kona kino, o ka lako o ka mea nana e hoolako mai i na mea a pau ma na mea a pau.

< Aefeso 1 >