< Mlaliki 9 >
1 Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani.
Doista sve ovo složih u srce svoje da bih rasvijetlio sve to, kako su pravedni i mudri i djela njihova u ruci Božijoj, a èovjek ne zna ni ljubavi ni mržnje od svega što je pred njim.
2 Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe. Zomwe zimachitikira munthu wabwino, zimachitikiranso munthu wochimwa, zomwe zimachitikira amene amalumbira, zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.
Sve biva svjema jednako: pravedniku biva kao bezbožniku, dobromu i èistomu kao neèistomu, onome koji prinosi žrtvu kao onome koji ne prinosi, kako dobromu tako grješniku, onome koji se kune kao onome koji se boji zakletve.
3 Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa.
A to je najgore od svega što biva pod suncem što svjema jednako biva, te je i srce ljudsko puno zla, i ludost im je u srcu dok su živi, a potom umiru.
4 Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!
Jer ko æe biti izabran? U živijeh svijeh ima nadanja; i psu živu bolje je nego mrtvu lavu.
5 Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa kanthu; alibe mphotho ina yowonjezera, ndipo palibe amene amawakumbukira.
Jer živi znaju da æe umrijeti, a mrtvi ne znaju ništa niti im ima plate, jer im se spomen zaboravio.
6 Chikondi chawo, chidani chawo ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale; sadzakhalanso ndi gawo pa zonse zochitika pansi pano.
I ljubavi njihove i mržnje njihove i zavisti njihove nestalo je, i više nemaju dijela nigda ni u èemu što biva pod suncem.
7 Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako.
Hajde, jedi hljeb svoj s radošæu, i vesela srca pij vino svoje, jer su mila Bogu djela tvoja.
8 Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse.
Svagda neka su ti haljine bijele, i ulja na glavi tvojoj da se ne premièe.
9 Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano.
Uživaj život sa ženom koju ljubiš svega vijeka svojega taštega, koji ti je dat pod suncem za sve vrijeme taštine tvoje, jer ti je to dio u životu i od truda tvojega kojim se trudiš pod suncem.
10 Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol )
Sve što ti doðe na ruku da èiniš, èini po moguænosti svojoj, jer nema rada ni mišljenja ni znanja ni mudrosti u grobu u koji ideš. (Sheol )
11 Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano: opambana pa kuthamanga si aliwiro, kapena opambana pa nkhondo si amphamvu, ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru, kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri, kapena okomeredwa mtima si ophunzira; koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.
Opet vidjeh pod suncem da nije do brzijeh trka, ni rat do hrabrijeh, ni hljeb do mudrijeh, ni bogatstvo do razumnijeh, ni dobra volja do vještijeh, nego da sve stoji do vremena i zgode.
12 Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti: monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde, kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha, chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa, pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.
Jer èovjek ne zna vremena svojega, nego kao što se ribe hvataju mrežom nesreænom i kao što se ptice hvataju pruglom, tako se hvataju sinovi èovjeèiji u zao èas, kad navali na njih iznenada.
13 Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri:
Vidjeh i ovu mudrost pod suncem, koja mi se uèini velika:
14 Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo.
Bijaše malen grad i u njemu malo ljudi; i doðe na nj velik car, i opkoli ga i naèini oko njega velike opkope.
15 Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo.
A naðe se u njemu siromah èovjek mudar, koji izbavi grad mudrošæu svojom, a niko se ne sjeæaše toga siromaha èovjeka.
16 Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.
Tada ja rekoh: bolja je mudrost nego snaga, ako se i ne maraše za mudrost onoga siromaha i rijeèi se njegove ne slušahu.
17 Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.
Rijeèi mudrijeh ljudi valja s mirom slušati više nego viku onoga koji zapovijeda meðu ludima.
18 Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.
Bolja je mudrost nego oružje ubojito; ali jedan grješnik kvari mnogo dobra.