< Mlaliki 9 >

1 Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani.
زیرا که جمیع این مطالب را در دل خود نهادم و این همه را غور نمودم که عادلان وحکیمان و اعمال ایشان در دست خداست. خواه محبت و خواه نفرت، انسان آن را نمی فهمد. همه‌چیز پیش روی ایشان است.۱
2 Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe. Zomwe zimachitikira munthu wabwino, zimachitikiranso munthu wochimwa, zomwe zimachitikira amene amalumbira, zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.
همه‌چیز برای همه کس مساوی است. برای عادلان و شریران یک واقعه است؛ برای خوبان و طاهران و نجسان؛ برای آنکه ذبح می‌کند و برای آنکه ذبح نمی کندواقعه یکی است. چنانکه نیکانند همچنان گناهکارانند؛ و آنکه قسم می‌خورد و آنکه از قسم خوردن می‌ترسد مساوی‌اند.۲
3 Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa.
در تمامی اعمالی که زیر آفتاب کرده می‌شود، از همه بدتر این است که یک واقعه برهمه می‌شود و اینکه دل بنی آدم از شرارت پراست و مادامی که زنده هستند، دیوانگی در دل ایشان است و بعد از آن به مردگان می‌پیوندند.۳
4 Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!
زیرا برای آنکه با تمامی زندگان می‌پیوندد، امیدهست چونکه سگ زنده از شیر مرده بهتر است.۴
5 Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa kanthu; alibe mphotho ina yowonjezera, ndipo palibe amene amawakumbukira.
زانرو که زندگان می‌دانند که باید بمیرند، امامردگان هیچ نمی دانند و برای ایشان دیگر اجرت نیست چونکه ذکر ایشان فراموش می‌شود.۵
6 Chikondi chawo, chidani chawo ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale; sadzakhalanso ndi gawo pa zonse zochitika pansi pano.
هم محبت و هم نفرت و حسد ایشان، حال نابود شده است و دیگر تا به ابد برای ایشان از هر‌آنچه زیرآفتاب کرده می‌شود، نصیبی نخواهد بود.۶
7 Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako.
پس رفته، نان خود را به شادی بخور وشراب خود را به خوشدلی بنوش چونکه خدااعمال تو را قبل از این قبول فرموده است.۷
8 Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse.
لباس تو همیشه سفید باشد و بر سر تو روغن کم نشود.۸
9 Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano.
جمیع روزهای عمر باطل خود را که او تو را درزیر آفتاب بدهد با زنی که دوست می‌داری درجمیع روزهای بطالت خود خوش بگذران. زیراکه از حیات خود و از زحمتی که زیر آفتاب می‌کشی نصیب تو همین است.۹
10 Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol h7585)
هر‌چه دستت به جهت عمل نمودن بیابد، همان را با توانایی خود به عمل آور چونکه در عالم اموات که به آن می‌روی نه کار و نه تدبیر و نه علم و نه حکمت است. (Sheol h7585)۱۰
11 Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano: opambana pa kuthamanga si aliwiro, kapena opambana pa nkhondo si amphamvu, ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru, kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri, kapena okomeredwa mtima si ophunzira; koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.
برگشتم و زیر آفتاب دیدم که مسابقت برای تیزروان و جنگ برای شجاعان و نان نیز برای حکیمان و دولت برای فهیمان و نعمت برای عالمان نیست، زیرا که برای جمیع ایشان وقتی واتفاقی واقع می‌شود.۱۱
12 Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti: monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde, kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha, chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa, pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.
و چونکه انسان نیز وقت خود را نمی داند، پس مثل ماهیانی که در تورسخت گرفتار و گنجشکانی که در دام گرفته می‌شوند، همچنان بنی آدم به وقت نامساعد هرگاه آن بر ایشان ناگهان بیفتد گرفتار می‌گردند.۱۲
13 Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri:
و نیز این حکم را در زیر آفتاب دیدم و آن نزد من عظیم بود:۱۳
14 Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo.
شهری کوچک بود که مردان در آن قلیل العدد بودند و پادشاهی بزرگ بر آن آمده، آن را محاصره نمود و سنگرهای عظیم برپاکرد.۱۴
15 Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo.
و در آن شهر مردی فقیر حکیم یافت شد، که شهر را به حکمت خود رهانید، اما کسی آن مرد فقیر را بیاد نیاورد.۱۵
16 Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.
آنگاه من گفتم حکمت از شجاعت بهتر است، هر‌چند حکمت این فقیررا خوار شمردند و سخنانش را نشنیدند.۱۶
17 Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.
سخنان حکیمان که به آرامی گفته شود، ازفریاد حاکمی که در میان احمقان باشد زیاده مسموع می‌گردد.۱۷
18 Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.
حکمت از اسلحه جنگ بهتر است. اما یک خطاکار نیکویی بسیار را فاسدتواند نمود.۱۸

< Mlaliki 9 >