< Mlaliki 9 >

1 Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani.
J’ai agité toutes ces choses dans mon cœur, afin de tâcher de les comprendre. Il y a des justes et des sages, et leurs œuvres sont dans la main de Dieu: et cependant l’homme ne sait s’il est digne d’amour ou de haine;
2 Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe. Zomwe zimachitikira munthu wabwino, zimachitikiranso munthu wochimwa, zomwe zimachitikira amene amalumbira, zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.
Mais toutes choses sont réservées pour l’avenir, étant incertaines dans le présent, parce que tout arrive également au juste et à l’impie, au bon et au méchant, au pur et à l’impur, à celui qui immole des victimes et à celui qui méprise les sacrifices; comme est le bon, ainsi est le pécheur; comme est le parjure, ainsi est celui-là même qui jure la vérité.
3 Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa.
Ce qu’il y a de plus fâcheux parmi toutes les choses qui se passent sous le soleil, c’est que les mêmes choses arrivent à tous: de là aussi les cœurs des fils des hommes sont remplis de malice et de mépris durant leur vie, et après cela ils seront conduits aux enfers.
4 Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!
Il n’est personne qui vive toujours et qui en ait même l’espérance; mieux vaut un chien vivant qu’un lion mort.
5 Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa kanthu; alibe mphotho ina yowonjezera, ndipo palibe amene amawakumbukira.
Car les vivants savent qu’ils doivent mourir; mais les morts ne connaissent plus rien, et ils n’ont plus de récompense, parce qu’à l’oubli a été livrée leur mémoire.
6 Chikondi chawo, chidani chawo ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale; sadzakhalanso ndi gawo pa zonse zochitika pansi pano.
L’amour aussi et la haine et l’envie ont péri avec eux, et ils n’ont point de part en ce siècle, ni dans l’œuvre qui se fait sous le soleil.
7 Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako.
Va donc et mange ton pain dans l’allégresse, et bois ton vin dans la joie; parce qu’à Dieu plaisent tes œuvres.
8 Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse.
Qu’en tout temps tes vêtements soient blancs, et que l’huile ne cesse pas de parfumer ta tête.
9 Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano.
Jouis complètement de la vie avec l’épouse que tu aimes tous les jours de ta vie fugitive, jours qui t’ont été donnés sous le ciel, durant tout le temps de ta vanité: car c’est là ta part dans la vie et dans ton travail auquel tu travailles sous le soleil.
10 Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol h7585)
Tout ce que peut faire ta main, fais-le promptement, parce que ni œuvre, ni raison, ni sagesse, ni science ne seront aux enfers, où tu cours. (Sheol h7585)
11 Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano: opambana pa kuthamanga si aliwiro, kapena opambana pa nkhondo si amphamvu, ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru, kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri, kapena okomeredwa mtima si ophunzira; koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.
Je me suis tourné vers une autre chose, et j’ai vu sous le soleil que la course n’est pas pour les prompts, ni la guerre pour les vaillants, ni le pain pour les sages, ni les richesses pour les savants, ni la faveur pour les ouvriers habiles, mais le temps et le hasard font toutes choses.
12 Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti: monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde, kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha, chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa, pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.
L’homme ne connaît pas sa fin: et comme les poissons sont pris à l’hameçon, et comme les oiseaux sont retenus par le lacs, ainsi sont pris les hommes par un temps mauvais, lorsque tout d’un coup il leur survient.
13 Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri:
J’ai aussi vu sous le soleil cette sagesse, et je l’ai estimée très grande:
14 Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo.
Une petite cité, et peu d’hommes en elle: il vint contre elle un grand roi, il l’investit, bâtit des forts autour, et le siège fut complet.
15 Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo.
Or, il s’y trouva un homme pauvre et sage, et il délivra la ville par sa sagesse; et nul dans la suite ne se ressouvint de cet homme pauvre.
16 Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.
Et je disais, moi, que la sagesse vaut mieux que la force. Comment donc la sagesse du pauvre a-t-elle été méprisée, et ses paroles n’ont-elles pas été écoutées?
17 Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.
Les paroles des sages sont écoutées en silence, plus que les cris du prince parmi les insensés.
18 Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.
Vaut mieux la sagesse que les armes guerrières: et celui qui pèche en un seul point perdra de grands biens.

< Mlaliki 9 >