< Mlaliki 9 >

1 Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani.
Thi alt dette har jeg lagt mig paa Hjerte, og det for at udgrunde det alt sammen, at de retfærdige og de vise og deres Gerninger ere i Guds Haand; om det er Kærlighed eller Had, ved intet Menneske; alt ligger for deres Ansigt.
2 Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe. Zomwe zimachitikira munthu wabwino, zimachitikiranso munthu wochimwa, zomwe zimachitikira amene amalumbira, zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.
Alt er ens for alle; det samme hændes den retfærdige og den ugudelige, den gode og den rene og den urene, og den, som ofrer, og den, der ikke ofrer; som den gode, saa gaar det Synderen, den, som sværger, gaar det som den, der frygter for Ed.
3 Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa.
Ondt iblandt alt det, som sker under Solen, er dette: At det samme hændes alle; og tillige er Menneskens Børns Hjerte fuldt af Ondskab, og der er Daarskaber i deres Hjerte, saa længe de leve, og derefter fare de til de døde.
4 Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!
Thi hvo er den, som kan undtages? om alle dem, som leve, er der Haab; thi en levende Hund er bedre end en Løve, som er død;
5 Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa kanthu; alibe mphotho ina yowonjezera, ndipo palibe amene amawakumbukira.
thi de levende vide, at de skulle dø; men de døde vide ikke noget, og de have ingen Løn ydermere; men deres Ihukommelse er glemt.
6 Chikondi chawo, chidani chawo ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale; sadzakhalanso ndi gawo pa zonse zochitika pansi pano.
Baade deres Kærlighed og deres Had og deres Avind er forlængst forsvunden, og de have i al Evighed ingen Del ydermere i alt det, som sker under Solen.
7 Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako.
Gak hen, æd dit Brød med Glæde og drik din Vin med et godt Mod; thi Gud har forlængst Behag i dine Gerninger.
8 Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse.
Lad dine Klæder altid være hvide, og lad Olie ikke fattes paa dit Hoved!
9 Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano.
Nyd Livet med en Hustru, som du elsker, alle dine Forfængeligheds Levedage, som Gud har givet dig under Solen, alle dine Forfængeligheds Dage; thi det er din Del af Livet og af dit Arbejde, som du arbejder med under Solen.
10 Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol h7585)
Alt hvad din Haand formaar at gøre med din Kraft, gør det; thi der er hverken Gerning eller Tanke eller Kundskab eller Visdom i Dødsriget, hvor du farer hen. (Sheol h7585)
11 Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano: opambana pa kuthamanga si aliwiro, kapena opambana pa nkhondo si amphamvu, ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru, kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri, kapena okomeredwa mtima si ophunzira; koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.
Jeg vendte tilbage og saa under Solen, at Løbet ikke er i de lettes Magt, og Krigen ikke i de vældiges, og ej heller Brødet i de vises, og ej heller Rigdommen i de forstandiges, og ej heller Gunst i de kløgtiges; thi Tid og Hændelse ramme dem alle.
12 Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti: monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde, kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha, chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa, pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.
Thi Mennesket ved heller ikke sin Tid, saa lidt som Fiskene, der fanges i det slemme Garn, og saa lidt som Fuglene, der fanges i Snaren; som disse, saa blive Menneskens Børn besnærede til Ulykkens Tid, eftersom den falder hastelig over dem.
13 Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri:
Ogsaa dette saa jeg som Visdom under Solen, og den syntes mig stor:
14 Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo.
Der var en liden Stad og faa Folk i den; og der kom en mægtig Konge imod den og omringede den og byggede store Belejringsværker om den;
15 Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo.
og han fandt derudi en fattig, viis Mand, og denne reddede Staden ved sin Visdom; men intet Menneske kom denne fattige Mand i Hu.
16 Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.
Da sagde jeg: Visdom er bedre end Styrke; men den fattiges Visdom er foragtet, og hans Ord blive ikke hørte.
17 Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.
De vises Ord, hørte i Ro, ere bedre end Herskerens Skrig iblandt Daarer.
18 Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.
Bedre er Visdom end Stridsvaaben; og een Synder kan fordærve meget godt.

< Mlaliki 9 >