< Mlaliki 8 >

1 Ndani angafanane ndi munthu wanzeru? Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu? Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.
Mądrość człowieka oświeca oblicze jego, a hardość twarzy jego odmienia.
2 Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu.
Jać radzę, abyś wyroku królewskiego przestrzegał a wszakże według przysięgi Bożej.
3 Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho.
Nie skwapiaj się odejść od oblicza jego, ani trwaj w uporze; albowiem cobykolwiek chciał, uczyniłciby.
4 Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
Bo gdzie słowo królewskie, tam i moc jego: a któż mu rzecze: Co czynisz?
5 Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse, ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.
Kto strzeże przykazania, nie uzna nic złego; i czas i przyczyny zna serce mądrego.
6 Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse, ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.
Albowiem wszelki zamysł ma czas i przyczyny; aleć wielka bieda trzyma się człowieka,
7 Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?
Że nie wie, co ma być; bo kiedy się co stanie, któż mu oznajmi?
8 Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.
Niemasz człowieka, coby miał moc nad żywotem, żeby zahamował duszę, ani ma mocy nade dniem śmierci; ani ma, czemby się bronił w tym boju, ani wyswobodzi niezbożnego niepobożność.
9 Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza.
Tom wszystko widział, gdym przyłożył serce swoje do tego wszystkiego, co się pod słońcem dzieje; widziałem ten czas, którego panuje człowiek nad człowiekiem na jego złe.
10 Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.
Tedym widział niezbożnych pogrzebionych, że się zaś nawrócili; ale którzy z miejsca świętego odeszli, przyszli w zapamiętanie w onem mieście, w którem dobrze czynili. I toć jest marność.
11 Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa.
Bo iż nie zaraz wychodzi dekret na złe sprawy, przetoż na tem jest wszystko serce synów ludzkich, aby czynili złe rzeczy.
12 Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu.
A chociaż grzesznik sto kroć źle czyni, i odwłacza mu się, wszakże ja wiem, że dobrze będzie bojącym się Boga, którzy się boją oblicza jego.
13 Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.
Ale niezbożnemu nie dobrze będzie, ani się przedłużą dni jego, owszem pomija jako cień, przeto, iż się nie boi oblicza Bożego.
14 Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino.
Jest też marność, która się dzieje na ziemi, że bywają sprawiedliwi, którym się tak powodzi, jakoby czynili uczynki niepobożnych; zasię bywają niepobożni, którym się tak powodzi, jakoby czynili uczynki sprawiedliwych. Przetożem rzekł: I toć jest marność.
15 Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.
A tak chwaliłem wesele, przeto, iż niemasz nic lepszego człowiekowi pod słońcem, jedno jeść, i pić, i weselić się, a iż mu jedno to zostaje z pracy jego po wszystkie dni żywota jego, które mu Bóg dał pod słońcem.
16 Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku,
A chociażem udał serce swe na to, abym doszedł mądrości, i zrozumiał kłopoty, które się dzieją na ziemi, dla których człowiek ani we dnie ani w nocy nie śpi;
17 pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.
A wszakże widziałem przy każdym uczynku Bożym, że nie może człowiek doścignąć sprawy, która się dzieje pod słońcem. Starać się człowiek chcąc tego dojść, ale nie dochodzi; owszem choćby rzekł mądry, że się chce dowiedzieć, nie będzie mógł znaleść.

< Mlaliki 8 >