< Mlaliki 8 >

1 Ndani angafanane ndi munthu wanzeru? Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu? Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.
Ngubani onjengohlakaniphileyo? Ngubani-ke owazi ukuchasiswa kolutho? Inhlakanipho yomuntu iyakhanyisa ubuso bakhe, lobulukhuni bobuso bakhe buyaguqulwa.
2 Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu.
Ngithi: Gcina umlayo wenkosi, lanjengokwesifungo sikaNkulunkulu.
3 Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho.
Ungaphangisi ukusuka phambi kwayo, ungemi edabeni olubi, ngoba yenza konke ekuthandayo.
4 Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
Lapho okulelizwi lenkosi khona kulamandla; njalo ngubani ongathi kuyo: Wenzani?
5 Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse, ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.
Lowo ogcina umlayo kayikwazi into embi, lenhliziyo yohlakaniphileyo iyasazi isikhathi lokwahlulela.
6 Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse, ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.
Ngoba kulo lonke udaba kulesikhathi lokwahlulela, ngoba ububi bomuntu bukhulu phezu kwakhe.
7 Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?
Ngoba kakwazi ukuthi kuzakuba yini, ngoba ngubani ongamtshela ukuthi kuzakuba nini?
8 Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.
Kakulamuntu olamandla phezu komoya ukubamba umoya, njalo kalamandla osukwini lokufa; njalo kakukho ukukhululwa kuleyompi, lobubi kabuyikukhulula abaninibo.
9 Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza.
Konke lokhu ngikubonile, nganikela inhliziyo yami emsebenzini wonke owenziwa ngaphansi kwelanga; kulesikhathi lapho umuntu abusa khona umuntu kube yikulimala kwakhe.
10 Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.
Ngokunjalo-ke ngabona ababi bengcwatshwa, ababevela njalo baye endaweni engcwele, abasebekhohlakele emzini lapho ababenze khona okunjalo. Lokhu lakho kuyize.
11 Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa.
Ngoba isigwebo ngesenzo esibi singenziwa masinyane, ngenxa yalokho inhliziyo yabantwana babantu igcwele ngaphakathi kwabo ukwenza okubi.
12 Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu.
Lanxa isoni sisenza okubi izikhathi ezilikhulu, lensuku zaso zelulwe, kube kanti sibili ngiyazi ukuthi kuzabalungela labo abamesabayo uNkulunkulu, abesabayo phambi kwakhe.
13 Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.
Kodwa omubi kakuyikumlungela; futhi kayikwelula insuku zakhe; unjengesithunzi ngoba kesabi phambi kukaNkulunkulu.
14 Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino.
Kukhona okuyize okwenziwayo emhlabeni, ukuthi bakhona abalungileyo abehlelwa njengokomsebenzi wababi, bakhona lababi abehlelwa njengokomsebenzi wabalungileyo. Ngathi: Lokhu lakho kuyize.
15 Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.
Ngakho mina ngababaza intokozo; ngoba umuntu kalalutho oluhle ngaphansi kwelanga, ngaphandle kokudla lokunatha lokuthokoza, ngoba lokhu kuzahlala laye ekutshikatshikeni kwakhe ensukwini zempilo yakhe uNkulunkulu amnike zona ngaphansi kwelanga.
16 Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku,
Lapho nganikela inhliziyo ukwazi inhlakanipho lokubona umsebenzi owenziwa emhlabeni, (ngoba futhi ukhona ongaboni ubuthongo ngamehlo akhe emini lebusuku)
17 pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.
ngasengibona wonke umsebenzi kaNkulunkulu ukuthi umuntu kalakho ukufumana umsebenzi owenziwayo ngaphansi kwelanga; ngoba lanxa umuntu etshikatshika ukukudinga, kube kanti kayikukufumana; yebo futhi, lanxa ohlakaniphileyo angathi uyazi, kayikuba lakho ukukuthola.

< Mlaliki 8 >