< Mlaliki 8 >

1 Ndani angafanane ndi munthu wanzeru? Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu? Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.
O WAI ka mea i like me ka mea naauao? Owai ka mea i ike i ka hoakaka ana i ka olelo? Ka naanao o ke kanaka, oia ka mea e oluolu ai kona maka, a ua hala kona maka haaheo.
2 Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu.
Ke ao aku nei au ia oe, e malama i ke kanawai o ke alii, no ka hoohiki ana i ke Akua.
3 Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho.
Mai wikiwiki oe i kou hele ana mai kona alo aku: mai kupaa oe ma ka mea ino; no ka mea, ke hana la ia i na mea a pau loa ana i makemake ai.
4 Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
Ma ka olelo a ke alii, aia no ka mana; a owai la ka mea e hiki ke olelo aku ia ia, Heaha kau i hana'i?
5 Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse, ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.
O ka mea malama i ke kanawai, aole ia e ike i ka mea ino; a o ka naau o ka mea akamai, ua ike ia i ka manawa a me ka hoopono.
6 Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse, ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.
No ka mea, aia no i na mea a pau he wa no, a me ka hoopono; a ua nui ke kaumaha maluna o ke kanaka.
7 Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?
No ka mea. aole ia i ike i ka mea e hiki mai ana; a o ka wa e hiki mai ai, owai la ka mea e hiki ke hai aku ia ia?
8 Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.
Aohe kanaka e hiki ke malama i ka hanu a paa ia, aohe mea ikaika i ka la e make ai; aole hoi i hookuuia kekahi mai keia kaua aku; aole nae e hoopakele ka hewa i ka poe hewa.
9 Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza.
Ua ike au i keia mau mea a pau, a halalo kuu naau i na hana a pau i hanaia malalo iho o ka la, aia i kekahi wa no e alii ai kekahi kanaka maluna o kekahi i mea e poino ai oia iho.
10 Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.
A pela no, ua ike au i ke kanuia o ka poe hewa, ua hele lakou iloko o kahi hemolele, a hoi mai, a ua poina lakou ma ke kulanakauhale, kahi a lakou i hana'i pela. He mea lapuwale keia.
11 Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa.
No ka hooko koke ole ia mai o ka olelo hoahewa i ka hana ino; no ia mea, ua paa loa ka naau o na keiki a kanaka e hana hewa.
12 Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu.
Ina e hana ino ka mea hewa, pahaneri ka hana ana, a ua hooloihiia kona mau la, ua ike no au, ua pomaikai ka poe makau i ke Akua, ka poe makau imua ona.
13 Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.
Aole e pomaikai ka mea hewa, aole nae ia e hooloihi i kona mau la, no ka mea, me he aka la ka mea i makau ole imua i ke alo o ke Akua.
14 Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino.
Eia kekahi mea lapuwale i hanaia ma ka honua; aia no kekahi poe pono, a ua ili wale ia lakou e like me ka hana a ka poe hewa, a aia hoi ka poe hewa, ua ili wale ia lakou e like me ka hana a ka poe pono. I iho la au, he mea lapuwale keia.
15 Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.
Alaila, mahalo iho la au i ka olioli, no ka mea, aohe mea maikai i ke kanaka malalo iho o ka la i oi aku i ka ai ana, i ka inu, a me ka olioli; he mea mau keia ia ia no kana haua, i na la o kona ola ana a ke Akua i haawi mai ai ia ia malalo iho o ka la.
16 Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku,
Alaila, haawi ae la au i ko'u naau e ike i ka naauao, a e ike hoi i ka mea i hanaia ma ka honua; no ka mea, aia no kekahi mea i pili ole ai kona mau maka i ka hiamoe i ka po a me ke ao:
17 pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.
A ike iho la au i na hana a pau a ke Akua, no ka mea, aole hiki i ke kanaka ke hoomaopopo i na hana i hanaia malalo iho o ka la; oiaio hoi, ina e hooikaika ke kanaka e imi, aole nae i maopopo, ina e olelo ka mea naauao e ike ia, aole nae e hiki ia ia ke hoomaopopo aku.

< Mlaliki 8 >