< Mlaliki 8 >
1 Ndani angafanane ndi munthu wanzeru? Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu? Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.
Кой е като мъдрия? И кой знае изяснението на нещата? Мъдростта на човека осветлява лицето му, И коравината на лицето му се променя.
2 Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu.
Аз те съветвам да пазиш царевата заповед, А най-вече заради клетвата пред Бога.
3 Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho.
Не бързай да излезеш от присъствието му; Не постоянствай в лоша работа; Защото върши всичко, каквото иска,
4 Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
Тъй като думата на царя има власт, И кой ще му рече: Що правиш?
5 Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse, ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.
Който пази заповедта няма да види нещо зло; И сърцето на мъдрия познава, че има и време и съдба за непокорството.
6 Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse, ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.
Понеже за всяко нещо има време и съдба; Защото окаянството на човека е голямо върху него,
7 Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?
Понеже не знае какво има да стане; Защото кой може да му яви как ще бъде?
8 Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.
Няма човек, който да има власт над духа, та да задържи духа, Нито да има власт над деня на смъртта; И в тая война няма уволнение, Нито ще избави нечестието ония, които са предадени на него.
9 Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza.
Всичко това видях, като занимах сърцето си С всяко дело, което става под слънцето, Че има време, когато човек властва над човека за негова повреда.
10 Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.
При това, видях нечестивите погребани, Които бяха дохождали и отивали в святото място; И те бидоха забравени в града дето бяха така сторили. И това е суета.
11 Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa.
Понеже присъдата против нечестиво дело не се изпълнява скоро, За това сърцето на човешките чада е всецяло вдадено да струва зло.
12 Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu.
Ако и грешникът да струва зло сто пъти и да дългоденства, Пак аз това зная, че ще бъде добре На ония, които се боят от Бога, които се боят пред Него;
13 Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.
А на нечестивия не ще бъде добре, Нито ще се продължат дните му, които ще бъдат като сянка, Защото той не се бои пред Бога.
14 Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino.
Има една суета, която става на земята: Че има праведни, на които се случва според делата на нечестивите, А пък има нечестиви, на които се случва според делата на праведните. Рекох, че и това е суета.
15 Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.
За това, аз похвалих веселбата, Защото на човека няма по-добро под слънцето Освен да яде и да пие и да се весели, И това да му остава от труда му През всичките дни на живота му, които Бог му е дал под слънцето.
16 Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku,
Когато предадох сърцето си да позная мъдростта, И да видя труденето, което ставаше по земята, Как очите на някои не виждат сън ни деня ни нощя,
17 pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.
Тогава видях всичкото Божие дело, Че човек не може да издири делото, което става под слънцето; Понеже колкото и да се труди човек да го търси, Пак няма да го намери; Па дори ако и мъдрият да рече да го познае, Не ще може да го намери;