< Mlaliki 7 >

1 Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino, ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
Краще добре ім'я́ від оливи хорошої, а день смерти люди́ни — від дня її вро́дження!
2 Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero: Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense; anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
Краще ходити до дому жало́би, ніж ходити до дому бенке́ту, бо то — кінець кожній люди́ні, і живий те до серця свого бере!
3 Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
Кращий смуток від смі́ху, бо при обличчі сумні́м добре серце!
4 Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa, koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
Серце мудрих — у домі жало́би, а серце безглу́здих — у домі весе́лощів.
5 Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
Краще слухати до́кір розумного, аніж слу́хати пісні безумних,
6 Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika, izinso ndi zopandapake.
бо як трі́скот терни́ни під горщиком, такий сміх нерозу́много. Теж марно́та й оце!
7 Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru, ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
Коли мудрий кого утискає, то й сам нерозумним стає, а хаба́р губить серце.
8 Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake, ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
Кінець ді́ла ліпший від поча́тку його; ліпший терпеливий від чванькува́того!
9 Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako, pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
Не спіши в своїм дусі, щоб гні́ватися, бо гнів спочиває у на́драх глупці́в.
10 Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
Не кажи: „Що́ це сталось, що перші дні були кращі за ці?“, бо не з мудрости ти запитався про це.
11 Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
Добра мудрість з багатством, а прибу́ток для тих, хто ще сонечко бачить,
12 Nzeru ndi chitetezo, monganso ndalama zili chitetezo, koma phindu la chidziwitso ndi ili: kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
бо в тіні мудрости — як у тіні срі́бла, та ко́ристь пізна́ння у то́му, що мудрість життя зберігає тому́, хто має її.
13 Taganizirani zimene Mulungu wazichita: ndani angathe kuwongola chinthu chimene Iye anachipanga chokhota?
Розваж Божий учинок, — бо хто́ може те ви́простати, що Він покриви́в?
14 Pamene zinthu zili bwino, sangalala; koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino: Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo, ndiponso nthawi imene si yabwinoyo. Choncho munthu sangathe kuzindikira chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
За доброго дня користай із добра́, за злого ж — розважуй: Одне й друге вчинив Бог на те, щоб люди́на нічо́го по собі не знайшла́!
15 Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi: munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake, ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
В днях марно́ти своєї я всьо́го набачивсь: буває справедливий, що гине в своїй справедливості, буває й безбожний, що довго живе в своїм злі.
16 Usakhale wolungama kwambiri kapena wanzeru kwambiri, udziwonongerenji wekha?
Не будь справедливим занадто, і не роби себе мудрим над міру: пощо нищити маєш себе?
17 Usakhale woyipa kwambiri, ndipo usakhale chitsiru, uferenji nthawi yako isanakwane?
Не будь несправедливим занадто, і немудрим не будь: пощо маєш померти в неча́сі своїм?
18 Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi, ndipo usataye njira inayo. Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
Добре, щоб ти ухопи́вся за це, але й з того своєї руки не спускай, бо богобоя́зний втече від усього того.
19 Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
Мудрість робить мудрого сильнішим за десятьох володарів, що в місті.
20 Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
Немає люди́ни праведної на землі, що робила б добро́ й не грішила,
21 Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula, mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
тому́ не клади свого серця на всякі слова́, що гово́рять, щоб не чути свого раба, коли він лихосло́вить тебе,
22 pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
знає бо серце твоє, що багато разі́в також ти лихосло́вив на інших!
23 Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati, “Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,” koma nzeruyo inanditalikira.
Усе́ це я в мудрості ви́пробував, і сказав: „Стану мудрим!“Та дале́ка від мене вона!
24 Nzeru zimene zilipo, zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri, ndani angathe kuzidziwa?
Дале́ке оте, що було́, і глибо́ке, глибо́ке, — хто зна́йде його?
25 Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe, ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru ndiponso kupusa kwake kwa misala.
Звернувся я серцем своїм, щоб пізна́ти й розві́дати, та шукати премудрість і розум, та щоб пізнати, що безбожність — глупо́та, а нерозум — безу́мство!
26 Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa, mkazi amene ali ngati khoka, amene mtima wake uli ngati khwekhwe, ndipo manja ake ali ngati maunyolo. Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo, koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
І знайшов я річ гіршу від смерти — то жінку, бо па́стка вона, її ж серце — тене́та, а руки її — то кайда́ни! Хто добрий у Бога — врято́ваний буде від неї, а грішного схо́пить вона!
27 Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi: “Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
Подивися, оце я знайшов, сказав Пропові́дник: рівняймо одне до одно́го, щоб знайти зрозумі́ння!
28 pamene ine ndinali kufufuzabe koma osapeza kanthu, ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000, koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
Чого ще шукала душа моя, та не знайшла: я люди́ну знайшов одну з тисячі, але жінки між ними всіма́ не знайшов!
29 Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi: Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama, koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”
Крім то́го, поглянь, що знайшов я: що праведною вчинив Бог люди́ну, та ви́гадок усяких шукають вони!

< Mlaliki 7 >