< Mlaliki 7 >
1 Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino, ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
Nasaysayaat ti napintas a nagan ngem ti nangina a pabanglo, ken ti aldaw ti pannakatay ket nasaysayaat ngem ti aldaw ti pannakaiyanak.
2 Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero: Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense; anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
Nasaysayaat iti mapan iti balay iti ladladingit ngem iti balay iti ramrambak, ta umay ti panagladangit kadagiti amin a tattao iti pagpatinggaan ti biag, isu a masapul nga ipapuso dagiti sibibiag a tattao daytoy.
3 Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
Nasaysayaat ti ladingit ngem ti katawa, ta kalpasan ti kinaliday ti rupa ket dumteng ti kinaragsak ti puso.
4 Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa, koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
Ti puso ti masirib ket adda iti balay iti ladladingit, ngem adda ti puso dagiti maag iti balay iti ramrambak.
5 Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
Nasaysayaat ti dumngeg iti panangtubngar iti masirib ngem ti dumngeg iti kanta dagiti maag.
6 Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika, izinso ndi zopandapake.
Ta kasla iti panagrissat dagiti mapupuoran a sisiit iti sirok ti banga, kasta met ti katawa dagiti maag. Maiyarig met laeng daytoy iti alingasaw.
7 Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru, ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
Awan duadua a ti panagkusit ket pagbalinenna a maag ti maysa a masirib a tao, ken dadaelen ti pasuksok ti pusona.
8 Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake, ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
Nasaysayaat ti panagleppas ti maysa a banag ngem ti rugrugi; ken nasaysayaat dagiti tattao a naanus ti espirituda ngem dagiti natangsit ti espirituda.
9 Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako, pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
Saankayo a dagus a makapungtot iti espirituyo, ta agnanaed ti pungtot kadagiti puso dagiti maag.
10 Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
Saanyo a kunaen, “Apay a nasaysayaat dagiti naglabas nga aldaw ngem kadagitoy? Ta saan a gapu iti kinasirib a dinamagyo daytoy.
11 Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
Ti kinasirib ket nasayaat a kas kadagiti napapateg a banbanag a tinawidtayo manipud kadagiti kapuonantayo. Mangipapaay daytoy iti pagimbagan para kadagiti makakita iti init.
12 Nzeru ndi chitetezo, monganso ndalama zili chitetezo, koma phindu la chidziwitso ndi ili: kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
Ta mangipapaay iti salaknib ti kinasirib kas iti kuarta a makaipaay iti salaknib, ngem ti pagimbagan iti pannakaammo ket mangmangted ti kinasirib iti biag iti siasinoman nga addaan iti daytoy.
13 Taganizirani zimene Mulungu wazichita: ndani angathe kuwongola chinthu chimene Iye anachipanga chokhota?
Utobem dagiti aramid ti Dios: Siasino ti makalinteg ti aniaman a banag nga inaramidna a killo?
14 Pamene zinthu zili bwino, sangalala; koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino: Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo, ndiponso nthawi imene si yabwinoyo. Choncho munthu sangathe kuzindikira chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
No nasayaat dagiti tiempo, agbiagka a siraragsak iti dayta a kinasayaat, ngem no saan a nasayaat dagiti tiempo, utobem daytoy: impalubos ti Dios nga umadda iti agpada a tiempo. Iti daytoy a rason, awanto ti makaammo ti aniaman a banag a dumteng kalpasanna.
15 Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi: munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake, ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
Nakitak dagiti adu a banbanag kabayatan dagiti awan kaipapananna nga al-aldawko. Adda dagiti mapukaw a nalinteg a tattao iti laksid dagiti kinalintegda ken adda dagiti nadangkes a tattao nga agbibiag iti atiddug iti laksid kadagiti kinadakesda.
16 Usakhale wolungama kwambiri kapena wanzeru kwambiri, udziwonongerenji wekha?
Saanka nga aginsisingpet, a masirib iti bukodmo a panagkita. Apay koma a dadaelem ti bagim?
17 Usakhale woyipa kwambiri, ndipo usakhale chitsiru, uferenji nthawi yako isanakwane?
Saanka unay nga agbalin a nadangkes wenno maag. Apay koma a matayka sakbay ti naituding a tiempom?
18 Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi, ndipo usataye njira inayo. Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
Nasayaat a salimetmetam koma daytoy a kinasirib, ken saanmo koma nga ikkaten dagiti imam manipud iti kinalinteg. Ta ti tao nga agbutbuteng iti Dios ket maaramidnanto dagiti amin a pagrebbenganna.
19 Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
Nabilbileg ti kinasirib iti masirib a tao, ngem ti sangapulo a mangiturturay iti siudad.
20 Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
Awan ti nalinteg a tao ditoy rabaw ti daga nga agar-aramid iti nasayaat ken saanen pulos nga agbasbasol.
21 Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula, mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
Saanka a dumngeg kadagiti amin a sasao a maibalbalikas, gapu ta amangan no mangngegmo ti adipenmo a mangilunod kenka.
22 pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
Kasta met, ammom iti bagim nga iti bukodmo a puso ket masansan nga inlunodmo dagiti dadduma.
23 Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati, “Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,” koma nzeruyo inanditalikira.
Napaneknekak amin dagitoy babaen iti kinasirib. Kinunak, “Agbalinak a masirib,” ngem nakarkaro daytoy ngem ti kabaelak.
24 Nzeru zimene zilipo, zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri, ndani angathe kuzidziwa?
Adayo ti kinasirib ken kasta unay ti kinaunegna. Siasino ti makasarak iti daytoy?
25 Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe, ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru ndiponso kupusa kwake kwa misala.
Intalyawko ti pusok nga agadal ken agsukimat ken agbiruk iti kinasirib ken kadagiti pannakaipalawag ti kinapudno ken tapno maawatan a ti dakes ket kinakuneng ken ti kinamaag ket kinamauyong.
26 Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa, mkazi amene ali ngati khoka, amene mtima wake uli ngati khwekhwe, ndipo manja ake ali ngati maunyolo. Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo, koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
Naduktalak a ti napapait ngem iti patay ket ti siasinoman a babai a ti pusona ket napno kadagiti silo ken iket, ken dagiti imana ket kawar. Makalibas kenkuana ti siasinoman a makaay-ayo iti Dios, ngem maalananto dagiti managbasol.
27 Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi: “Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
“Panunotenyo ti naduktalak,” kinuna ti Manursuro. Naynayunak ti mangdukduktal iti sabali pay tapno makabirukak iti pannakaipalawag iti kinapudno.
28 pamene ine ndinali kufufuzabe koma osapeza kanthu, ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000, koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
Daytoy ti birbirukek pay laeng, ngem saanko a nasarakan daytoy. Nakasakarak iti maysa a nalinteg a lalaki kadagiti rinibo, ngem awan ti nabirukak kadakuada a babai.
29 Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi: Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama, koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”
Naduktalak laeng daytoy: a pinarsua ti Dios a nalinteg ti sangkataoan, ngem pimmanawda nga agbirbiruk kadagiti adu a kinarigat.