< Mlaliki 7 >

1 Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino, ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
Une bonne réputation vaut mieux que le bon parfum; et le jour de la mort, que le jour de la naissance.
2 Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero: Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense; anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
Mieux vaut aller dans une maison de deuil, que d'aller dans une maison de festin; car là est la fin de tout homme, et celui qui vit met cela dans son cœur.
3 Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
Mieux vaut la tristesse que le rire; car, par la tristesse du visage, le cœur devient joyeux.
4 Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa, koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
Le cœur des sages est dans la maison de deuil; mais le cœur des insensés est dans la maison de joie.
5 Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
Mieux vaux entendre la répréhension du sage, que d'entendre la chanson des insensés.
6 Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika, izinso ndi zopandapake.
Car tel qu'est le bruit des épines sous la chaudière, tel est le rire de l'insensé. Cela aussi est une vanité.
7 Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru, ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
Certainement l'oppression peut faire perdre le sens au sage; et le présent corrompt le cœur.
8 Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake, ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
Mieux vaut la fin d'une chose que son commencement; mieux vaut un esprit patient qu'un esprit hautain.
9 Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako, pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
Ne te hâte point dans ton esprit de t'irriter; car l'irritation repose dans le sein des insensés.
10 Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
Ne dis point: D'où vient que les jours passés étaient meilleurs que ceux-ci? Car ce n'est point par sagesse que tu t'enquiers de cela.
11 Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
La sagesse est aussi bonne qu'un héritage; elle est un avantage pour ceux qui voient le soleil.
12 Nzeru ndi chitetezo, monganso ndalama zili chitetezo, koma phindu la chidziwitso ndi ili: kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
Car on est à couvert à l'ombre de la sagesse et à l'ombre de l'argent; mais la science a cet avantage, que la sagesse fait vivre celui qui la possède.
13 Taganizirani zimene Mulungu wazichita: ndani angathe kuwongola chinthu chimene Iye anachipanga chokhota?
Regarde l'œuvre de Dieu; car qui peut redresser ce qu'il aura courbé?
14 Pamene zinthu zili bwino, sangalala; koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino: Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo, ndiponso nthawi imene si yabwinoyo. Choncho munthu sangathe kuzindikira chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
Au jour de la prospérité, sois joyeux; et au jour de l'adversité, prends-y garde; aussi Dieu a fait l'un comme l'autre, afin que l'homme ne trouve rien de ce qui sera après lui.
15 Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi: munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake, ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
J'ai vu tout ceci pendant les jours de ma vanité. Il y a tel juste qui périt dans sa justice, et il y a tel méchant qui prolonge ses jours dans sa méchanceté.
16 Usakhale wolungama kwambiri kapena wanzeru kwambiri, udziwonongerenji wekha?
Ne sois pas juste à l'excès, et ne te fais pas trop sage; pourquoi te perdrais-tu?
17 Usakhale woyipa kwambiri, ndipo usakhale chitsiru, uferenji nthawi yako isanakwane?
Ne sois pas méchant à l'excès, et ne sois point insensé; pourquoi mourrais-tu avant ton temps?
18 Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi, ndipo usataye njira inayo. Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
Il est bon que tu retiennes ceci, et que tu ne négliges pas cela; car celui qui craint Dieu, sort de toutes ces choses.
19 Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
La sagesse donne plus de force au sage que dix gouverneurs qui seraient dans une ville.
20 Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
Certainement il n'y a point d'homme juste sur la terre, qui fasse le bien et qui ne pèche point.
21 Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula, mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
Aussi ne fais point attention à toutes les paroles qu'on dira, de peur que tu n'entendes ton serviteur parler mal de toi.
22 pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
Car ton cœur a reconnu bien des fois que toi aussi tu as mal parlé des autres.
23 Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati, “Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,” koma nzeruyo inanditalikira.
J'ai éprouvé tout cela par la sagesse; et j'ai dit: J'acquerrai de la sagesse; mais elle s'est éloignée de moi.
24 Nzeru zimene zilipo, zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri, ndani angathe kuzidziwa?
Ce qui est loin, ce qui est profond, profond, qui peut l'atteindre?
25 Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe, ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru ndiponso kupusa kwake kwa misala.
J'ai appliqué mon cœur à connaître, à sonder et à chercher la sagesse et la raison de tout, et à connaître la méchanceté de la folie, et la sottise de la déraison.
26 Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa, mkazi amene ali ngati khoka, amene mtima wake uli ngati khwekhwe, ndipo manja ake ali ngati maunyolo. Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo, koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
Et j'ai trouvé plus amère que la mort, la femme dont le cœur est un piège et un filet, et dont les mains sont des liens; celui qui est agréable à Dieu lui échappera; mais le pécheur sera pris par elle.
27 Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi: “Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
Voici, dit l'Ecclésiaste, ce que j'ai trouvé, en examinant les choses une à une pour en trouver la raison.
28 pamene ine ndinali kufufuzabe koma osapeza kanthu, ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000, koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
Voici ce que mon âme cherche encore, mais que je n'ai point trouvé. J'ai trouvé un homme entre mille; mais je n'ai pas trouvé une femme entre elles toutes.
29 Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi: Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama, koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”
Seulement voici ce que j'ai trouvé: c'est que Dieu a fait l'homme droit; mais ils ont cherché beaucoup de discours.

< Mlaliki 7 >