< Mlaliki 7 >

1 Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino, ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
A good name is better than fine perfume; and the day of death better than the day of one's birth.
2 Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero: Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense; anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
It is better to go to the house of mourning than to go to the house of feasting: for that is the end of all men, and the living should take this to heart.
3 Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
Sorrow is better than laughter; for by the sadness of the face the heart is made good.
4 Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa, koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
The heart of the wise is in the house of mourning; but the heart of fools is in the house of mirth.
5 Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
It is better to hear the rebuke of the wise, than for a man to hear the song of fools.
6 Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika, izinso ndi zopandapake.
For as the crackling of thorns under a pot, so is the laughter of the fool. This also is vanity.
7 Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru, ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
Surely extortion makes the wise man foolish; and a bribe destroys the understanding.
8 Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake, ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
Better is the end of a thing than its beginning. The patient in spirit is better than the proud in spirit.
9 Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako, pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
Do not be hasty in your spirit to be angry, for anger rests in the bosom of fools.
10 Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
Do not say, "Why were the former days better than these?" For you do not ask wisely about this.
11 Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
Wisdom is as good as an inheritance. Yes, it is more excellent for those who see the sun.
12 Nzeru ndi chitetezo, monganso ndalama zili chitetezo, koma phindu la chidziwitso ndi ili: kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
For wisdom is a defense, even as money is a defense; but the excellency of knowledge is that wisdom preserves the life of him who has it.
13 Taganizirani zimene Mulungu wazichita: ndani angathe kuwongola chinthu chimene Iye anachipanga chokhota?
Consider the work of God, for who can make that straight, which he has made crooked?
14 Pamene zinthu zili bwino, sangalala; koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino: Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo, ndiponso nthawi imene si yabwinoyo. Choncho munthu sangathe kuzindikira chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
In the day of prosperity be joyful, and in the day of adversity consider; yes, God has made the one side by side with the other, to the end that man should not find out anything after him.
15 Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi: munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake, ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
All this have I seen in my days of vanity: there is a righteous man who perishes in his righteousness, and there is a wicked man who lives long in his evildoing.
16 Usakhale wolungama kwambiri kapena wanzeru kwambiri, udziwonongerenji wekha?
Do not be overly righteous, neither make yourself overly wise. Why should you destroy yourself?
17 Usakhale woyipa kwambiri, ndipo usakhale chitsiru, uferenji nthawi yako isanakwane?
Do not be too wicked, neither be foolish. Why should you die before your time?
18 Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi, ndipo usataye njira inayo. Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
It is good that you should take hold of this. Yes, also from that do not withdraw your hand; for he who fears God will come forth from them all.
19 Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
Wisdom is a strength to the wise man more than ten rulers who are in a city.
20 Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
Surely there is not a righteous man on earth, who does good and doesn't sin.
21 Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula, mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
Also do not take heed to all words that are spoken, lest you hear your servant curse you;
22 pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
for often your own heart knows that you yourself have likewise cursed others.
23 Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati, “Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,” koma nzeruyo inanditalikira.
All this have I proved in wisdom. I said, "I will be wise;" but it was far from me.
24 Nzeru zimene zilipo, zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri, ndani angathe kuzidziwa?
That which is, is far off and exceedingly deep. Who can find it out?
25 Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe, ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru ndiponso kupusa kwake kwa misala.
I turned around, and my heart sought to know and to search out, and to seek wisdom and the scheme of things, and to know that wickedness is stupidity, and that foolishness is madness.
26 Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa, mkazi amene ali ngati khoka, amene mtima wake uli ngati khwekhwe, ndipo manja ake ali ngati maunyolo. Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo, koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
I find more bitter than death the woman whose heart is snares and traps, whose hands are chains. Whoever pleases God shall escape from her; but the sinner will be ensnared by her.
27 Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi: “Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
Look, this have I found, says the Preacher, one to another, to find out the scheme;
28 pamene ine ndinali kufufuzabe koma osapeza kanthu, ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000, koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
which my soul still seeks; but I have not found: one man among a thousand have I found; but a woman among all those have I not found.
29 Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi: Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama, koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”
Look, this only have I found, that God made humankind upright, but they search for many schemes.

< Mlaliki 7 >