< Mlaliki 6 >

1 Ine ndinaona choyipa china pansi pano, ndipo chimasautsa anthu kwambiri:
I have seen something [else here] on this earth that troubles people.
2 Mulungu amapereka chuma, zinthu ndi ulemu kwa munthu, kotero kuti munthuyo sasowa kanthu kalikonse kamene akukalakalaka, koma Mulungu samulola kuti adyerere zinthuzo, ndipo mʼmalo mwake amadyerera ndi mlendo. Izi ndi zopandapake, ndi zoyipa kwambiri.
God enables some people to get a lot of money and possessions and to be honored; they have everything [LIT] that they want. But God [sometimes] does not allow them to continue to enjoy those things. Someone else gets them and enjoys them. That seems senseless and unfair.
3 Ngakhale munthu atabereka ana 100 ndi kukhala ndi moyo zaka zambiri; komatu ngakhale atakhala zaka zambiri chotani, ngati iye sangadyerere chuma chake ndi kuyikidwa mʼmanda mwaulemu, ine ndikuti mtayo umamuposa iyeyo.
Someone might have 100 children and live for many years. But if he is not able to enjoy the things that he has acquired, and if he is not buried [properly after he dies], [I say that] a child that is dead when it is born is more fortunate.
4 Mtayo umangopita pachabe ndipo umapita mu mdima, ndipo mu mdimamo dzina lake limayiwalika.
That dead baby’s birth is meaningless; it does not even have a name. It goes directly to the place where there is only darkness.
5 Ngakhale kuti mtayowo sunaone dzuwa kapena kudziwa kanthu kalikonse, koma umapumula kuposa munthu uja,
It does not [live to] see the sun or know anything. But it finds more rest than rich people do [who are alive].
6 ngakhale munthuyo atakhala ndi moyo zaka 2,000, koma ndi kulephera kudyerera chuma chake. Kodi onsewa sapita malo amodzi?
Even if people could live for 2,000 years, if they do not enjoy the things that God gives to them, [it would have been better for them never to have been born]. [All people who live a long time] certainly [RHQ] all go to the same place— [to the grave].
7 Ntchito yonse ya munthu imathera pakamwa pake, komatu iye sakhutitsidwa ndi pangʼono pomwe.
People work hard to [earn enough money to buy] food to eat [MTY], but [often] they never get enough to eat.
8 Kodi munthu wanzeru amaposa motani chitsiru? Kodi munthu wosauka amapindula chiyani podziwa kukhala bwino pamaso pa anthu ena?
So it seems that [RHQ] wise people do not receive more lasting benefits than foolish people do. And it seems that [RHQ] poor people do not benefit from knowing how to conduct their lives.
9 Kuli bwino kumangoona zinthu ndi maso kusiyana ndi kumangozilakalaka mu mtima. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
It is better to enjoy the things that we already have [MTY] than to constantly want more things; continually wanting more things is [senseless], [like] the wind.
10 Chilichonse chimene chilipo anachitchula kale dzina, za mmene munthu alili nʼzodziwika; sangathe kutsutsana ndi munthu amene ali wamphamvu kupambana iyeyo.
All the things that exist [on the earth] have been given names. And everyone knows what people are like, [so] it is useless to argue with someone (OR, with God) who is stronger than we are.
11 Mawu akachuluka zopandapake zimachulukanso, nanga munthu zimamupindulira chiyani?
The more [that we] talk, the more [often we say things that are] senseless, so it certainly does not [RHQ] benefit us to talk a lot.
12 Pakuti ndani amene amadziwa chomwe ndi chabwino pa moyo wa munthu, pakuti moyo wake ndi wa masiku ochepa ndi opandapake, umangopitira ngati mthunzi. Ndani amene angamufotokozere zimene zidzachitika pansi pano iye atapita?
We live for only a short time; we disappear like [SIM] a shadow disappears [in the sunlight]. No one [RHQ] knows what is best for us while we are alive, and no one [RHQ] knows what will happen to us after we die [EUP].

< Mlaliki 6 >