< Mlaliki 5 >

1 Uzisamala mayendedwe ako pamene ukupita ku nyumba ya Mulungu. Upite pafupi kuti ukamvetsere mʼmalo mopereka nsembe ya zitsiru zimene sizizindikira kuti zikuchita zolakwa.
Qaphela izinyathelo zakho nxa usiya endlini kaNkulunkulu. Sondela ulalele kulokuthi wenze imihlatshelo yeziwula ezingaziyo ukuthi ziyona.
2 Usamafulumire kuyankhula, usafulumire mu mtima mwako kunena chilichonse pamaso pa Mulungu. Mulungu ali kumwamba ndipo iwe uli pa dziko lapansi, choncho mawu ako akhale ochepa.
Ungawalazeli ngomlomo wakho, ungabi lephaphu uphange uthembise kuNkulunkulu. UNkulunkulu usezulwini ikanti wena usemhlabeni, ngakho kawabe malutshwana amazwi akho.
3 Kuchuluka kwa mavuto mu mtima kumabweretsa maloto oyipa, ndipo kuchuluka kwa mawu kumadzetsa uchitsiru.
Njengephupho elifika nxa kulezinkathazo ezinengi, injalo inkulumo yesiwula nxa ilamazwi amanengi.
4 Pamene ulumbira kwa Mulungu usachedwe kukwaniritsa chimene walumbiracho. Iye sakondweretsedwa ndi chitsiru; kwaniritsa lumbiro lako.
Nxa usenza isifungo kuNkulunkulu, ungaphuzi ukusigcwalisa. Kathokozi ngeziwula; gcwalisa isifungo sakho.
5 Kuli bwino kusalumbira kusiyana ndi kulumbira koma osakwaniritsa lumbirolo.
Kungcono ukungafungi kulokwenza isifungo ungabe usasigcwalisa.
6 Pakamwa pako pasakuchimwitse. Ndipo usanene kwa mthenga wa mʼNyumba ya Mulungu kuti, “Ndinalakwitsa polumbira.” Chifukwa chiyani ukufuna Mulungu akwiye ndi mawu ako ndiponso ntchito ya manja ako?
Ungavumeli umlomo wakho ukungenise esonweni. Njalo ungatshingeli isithunywa sethempelini usithi, “Isifungo sami besiyisiphosiso.” UNkulunkulu angakuthukuthelelani lokho okutshoyo abesebhidliza umsebenzi wezandla zakho na?
7 Maloto ochuluka ndi mawu ochuluka ndi zinthu zopandapake. Kotero lemekeza Mulungu.
Ukuphupha kanengi lamazwi amanengi kuyize. Ngakho mesabe uNkulunkulu.
8 Ngati uwona anthu osauka akuzunzika mʼdziko, ndiponso anthu ena akupsinja anzawo ndi kuwalanda ufulu wawo, usadabwe ndi zinthu zimenezi; pakuti woyangʼanira ali naye wina womuyangʼanira wamkulu, ndipo pamwamba pa awiriwa pali ena akuluakulu owaposa.
Nxa ubona abayanga esiqintini bencindezelwa, bencitshwa ukwahlulelwa okuhle kanye lamalungelo, ungamangaliswa yilezozinto; ngoba phela induna nganye ikhangelwe ngomunye ongaphezu kwayo, kuthi ngaphezu kwabo bonke kube labanye njalo abangaphezulu.
9 Anthu onse amatengako zokolola za mʼminda: koma ndi mfumu yokha imene imapeza phindu la mindayi.
Inala elizweni ngeyomuntu wonke; inkosi ngokwayo ithola inzuzo ngalokho okuvela emasimini.
10 Aliyense amene amakonda ndalama sakhutitsidwa ndi ndalamazo; aliyense amene amakonda chuma sakhutitsidwa ndi zimene amapeza. Izinso ndi zopandapake.
Lowo othanda imali akaneliswa yiloba yimalini; lowo othanda inotho akasuthiswa yilokho akuzuzayo. Lokhu lakho kuyize.
11 Chuma chikachuluka akudya nawo chumacho amachulukanso. Nanga mwini wake amapindulapo chiyani kuposa kumangochiyangʼana ndi maso ake?
Nxa inotho isanda, bayanda lalabo abayisebenzisayo. Imsiza ngani umniniyo ngaphandle kokuyithapha ngamehlo nje kuphela?
12 Wantchito amagona tulo tabwino ngakhale adye pangʼono kapena kudya kwambiri, koma munthu wolemera, chuma sichimulola kuti agone.
Bumnandi ubuthongo besisebenzi, loba sisidla okuncane loba okunengi, kodwa isinothi asilali ngenxa yenotho yaso.
13 Ine ndinaona choyipa chomvetsa chisoni pansi pano: chuma chokundikidwa chikupweteka mwini wake yemwe,
Sengibone ububi obudanisayo ngaphansi kwelanga: ubuhaga ngenotho okulimaza umnikazi,
14 kapena chuma chowonongedwa pa nthawi yatsoka, kotero kuti pamene wabereka mwana alibe kanthu koti amusiyire.
loba inotho esuke yachitheka ngomnyama othile, okuthi nxa umuntu elendodana ayisayikuthola lutho.
15 Munthu anabadwa wamaliseche kuchokera mʼmimba mwa amayi ake, ndipo monga iye anabadwira, adzapitanso choncho. Pa zonse zimene iye anakhetsera thukuta palibe nʼchimodzi chomwe chimene adzatenge mʼmanja mwake.
Umuntu uphuma esiswini sikanina engelalutho, njengokufika kwakhe ubuyela enjalo. Kazuzi lutho olusuka emsebenzini wakhe angaluphatha ezandleni zakhe.
16 Izinso ndi zoyipa kwambiri: munthu adzapita monga momwe anabwerera, ndipo iye amapindula chiyani, pakuti amagwira ntchito yolemetsa yopanda phindu?
Lobu labo yibubi obudanisayo: Njengokufika kwakhe, umuntu uzabuyela enjalo, ngakho uzuzani, njengoba esebenza esadalalela umoya?
17 Masiku ake onse ndi odzaza ndi mdima, kukhumudwa kwakukulu, masautso ndi nkhawa.
Zonke insuku zakhe udlela emnyameni, ekhathazekile, ehluphekile, ezondile.
18 Tsono ndinazindikira kuti nʼchabwino ndi choyenera kuti munthu azidya ndi kumwa, ndi kukhutitsidwa ndi ntchito yake yolemetsa imene amayigwira pansi pano pa nthawi yake yochepa imene Mulungu amamupatsa, poti ichi ndiye chake.
Ngasengibona ukuthi kuhle kuqondile ukuthi umuntu adle njalo anathe, njalo azuze ukusuthiseka ekutshikatshikeni kwakhe ngomsebenzi ngaphansi kwelanga ngalezonsuku ezilutshwane ezokuphila uNkulunkulu asamuphe zona ngoba lesi yisabelo sakhe.
19 Komatu pamene Mulungu apereka chuma kwa munthu aliyense ndi zinthu zina, ndi kulola kuti akondwere ndi chumacho, munthuyo alandire chumacho ndi kusangalala ndi ntchito yake, imene ndi mphatso yochokera kwa Mulungu.
Kunjalo futhi ukuthi nxa uNkulunkulu esipha umuntu inotho lempahla, amvumele ukuthi akholise ngazo, emukele isabelo sakhe athokoze emsebenzini wakhe, lesi yisipho sikaNkulunkulu.
20 Munthu wotereyu saganizirapo za masiku a moyo wake, chifukwa Mulungu amamutanganidwitsa ndi chisangalalo cha mu mtima mwake.
Kahlali ekhumbula ngezinsuku zempilo yakhe ngoba uNkulunkulu umenza ahlale ngenjabulo enhliziyweni.

< Mlaliki 5 >