< Mlaliki 5 >

1 Uzisamala mayendedwe ako pamene ukupita ku nyumba ya Mulungu. Upite pafupi kuti ukamvetsere mʼmalo mopereka nsembe ya zitsiru zimene sizizindikira kuti zikuchita zolakwa.
Őrizd lábadat, midőn Isten házába mész; a odalépni, hogy figyelj, jobb mint mikor a balgák áldozatot adnak, mert nincs tudásuk, úgy hogy rosszat cselekesznek.
2 Usamafulumire kuyankhula, usafulumire mu mtima mwako kunena chilichonse pamaso pa Mulungu. Mulungu ali kumwamba ndipo iwe uli pa dziko lapansi, choncho mawu ako akhale ochepa.
Ne hírtelenkedjél szájaddal, és szíved ne siessen szót kiejteni Isten előtt, mert Isten az égben van, te pedig a földön vagy, azért legyenek a te szavaid kevesek.
3 Kuchuluka kwa mavuto mu mtima kumabweretsa maloto oyipa, ndipo kuchuluka kwa mawu kumadzetsa uchitsiru.
Mert jön az álom sok bajlódással és a balgának hangja sok beszéddel.
4 Pamene ulumbira kwa Mulungu usachedwe kukwaniritsa chimene walumbiracho. Iye sakondweretsedwa ndi chitsiru; kwaniritsa lumbiro lako.
Midőn fogadást teszel Istennek, ne késsél azt megfizetni, mert nem telik kedve a balgákban; a mit fogadtál, fizesd meg!
5 Kuli bwino kusalumbira kusiyana ndi kulumbira koma osakwaniritsa lumbirolo.
Jobb, ha nem fogadsz, mintsem hogy fogadsz és nem fizeted meg.
6 Pakamwa pako pasakuchimwitse. Ndipo usanene kwa mthenga wa mʼNyumba ya Mulungu kuti, “Ndinalakwitsa polumbira.” Chifukwa chiyani ukufuna Mulungu akwiye ndi mawu ako ndiponso ntchito ya manja ako?
Ne engedd szádnak, hogy vétekbe ejtse a te testedet, s ne mondd a küldött előtt, hogy tévedés volt; mért haragudjék Isten haragod miatt és rontsa meg kezed munkáját?
7 Maloto ochuluka ndi mawu ochuluka ndi zinthu zopandapake. Kotero lemekeza Mulungu.
Mert sok álom és sok hiúság mellett sok beszéd is van; hanem az Istent féljed.
8 Ngati uwona anthu osauka akuzunzika mʼdziko, ndiponso anthu ena akupsinja anzawo ndi kuwalanda ufulu wawo, usadabwe ndi zinthu zimenezi; pakuti woyangʼanira ali naye wina womuyangʼanira wamkulu, ndipo pamwamba pa awiriwa pali ena akuluakulu owaposa.
Ha szegénynek elnyomását és jognak és igazságnak megrablását látod a tartományban, ne csodálkozzál a dolgon; mert magas őrködik magas fölött, és legmagasabb van fölöttük.
9 Anthu onse amatengako zokolola za mʼminda: koma ndi mfumu yokha imene imapeza phindu la mindayi.
S az országnak nyeresége mindenképen az: király, ki szolgája lett a szántóföldnek.
10 Aliyense amene amakonda ndalama sakhutitsidwa ndi ndalamazo; aliyense amene amakonda chuma sakhutitsidwa ndi zimene amapeza. Izinso ndi zopandapake.
A ki szereti az ezüstöt, nem lakik jó1 ezüsttel, s a ki szereti a gazdagságot, annak nincs termése. Ez is hiúság.
11 Chuma chikachuluka akudya nawo chumacho amachulukanso. Nanga mwini wake amapindulapo chiyani kuposa kumangochiyangʼana ndi maso ake?
Megsokasodván a jószág, megsokasodtak annak emésztői, s mi haszna van a gazdájának abban, hacsak nem szemeinek látása?
12 Wantchito amagona tulo tabwino ngakhale adye pangʼono kapena kudya kwambiri, koma munthu wolemera, chuma sichimulola kuti agone.
Édes a munkásnak alvása, akár keveset, akár sokat eszik; s a gazdagnak jóllakottsága nem engedi őt aludni.
13 Ine ndinaona choyipa chomvetsa chisoni pansi pano: chuma chokundikidwa chikupweteka mwini wake yemwe,
Van egy fájó baj, melyet láttam a nap alatt: gazdagság megőrizve gazdájának a saját bajára.
14 kapena chuma chowonongedwa pa nthawi yatsoka, kotero kuti pamene wabereka mwana alibe kanthu koti amusiyire.
S elvész ama gazdagság gonosz bajlódás mellett; fiat nemzett, de nincs kezében semmi.
15 Munthu anabadwa wamaliseche kuchokera mʼmimba mwa amayi ake, ndipo monga iye anabadwira, adzapitanso choncho. Pa zonse zimene iye anakhetsera thukuta palibe nʼchimodzi chomwe chimene adzatenge mʼmanja mwake.
A mint kijött anyja méhéből, mezítelen megy megint oda, úgy a mint jött; és mit sem visz el fáradságáért, hogy elvigye kezében.
16 Izinso ndi zoyipa kwambiri: munthu adzapita monga momwe anabwerera, ndipo iye amapindula chiyani, pakuti amagwira ntchito yolemetsa yopanda phindu?
És ez is fájó baj: megfelelően annak, a hogy jött, úgy fog elmenni; mi nyeresége van tehát neki, hogy a szélnek fáradozik.
17 Masiku ake onse ndi odzaza ndi mdima, kukhumudwa kwakukulu, masautso ndi nkhawa.
Sőt mind az ő napjaiban sötétségben élvez és boszankodik sokat, betegsége is van meg harag.
18 Tsono ndinazindikira kuti nʼchabwino ndi choyenera kuti munthu azidya ndi kumwa, ndi kukhutitsidwa ndi ntchito yake yolemetsa imene amayigwira pansi pano pa nthawi yake yochepa imene Mulungu amamupatsa, poti ichi ndiye chake.
Íme a mit én jónak, a mit szépnek láttam: hogy egyék és igyék és élvezze a jót minden fáradságáért, melylyel fáradozik a nap alatt élete napjainak tartamára, melyet Isten adott neki; mert az az ő osztályrésze.
19 Komatu pamene Mulungu apereka chuma kwa munthu aliyense ndi zinthu zina, ndi kulola kuti akondwere ndi chumacho, munthuyo alandire chumacho ndi kusangalala ndi ntchito yake, imene ndi mphatso yochokera kwa Mulungu.
Az is bármely ember, kinek adott az Isten gazdagságot éa javakat és urává tette annak, bogy élvezzen belőle és hogy kivegye az osztályrészét és hogy örűljön fáradságában – az Istennek az adománya.
20 Munthu wotereyu saganizirapo za masiku a moyo wake, chifukwa Mulungu amamutanganidwitsa ndi chisangalalo cha mu mtima mwake.
Mert nem sokat fog emlékezni élete napjairól, mivel Isten megengedi szívének örömét.

< Mlaliki 5 >