< Mlaliki 12 >

1 Uzikumbukira mlengi wako masiku a unyamata wako, masiku oyipa asanafike, nthawi isanafike pamene udzanena kuti, “Izi sizikundikondweretsa.”
Piemini savu Radītāju savā jaunībā, pirms tās ļaunās dienas nāk un tie gadi tuvojās, kur tu sacīsi: tie man nepatīk.
2 Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala, mwezi ndi nyenyezi zidzada. Mitambo idzabweranso mvula itagwa.
Pirms saule un gaišums un mēnesis un zvaigznes aptumšojās, un padebeši nāk atkal pēc lietus,
3 Nthawi imene manja ako adzanjenjemera, miyendo yako idzafowoka, pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka, ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.
Tai laikā, kad tie nama sargi trīcēs, un tie stiprie vīri locīsies, un tie malēji stāvēs klusu, tāpēc ka viņu palicis maz, un tie, kas pa logiem skatās, paliks tumši,
4 Makutu ako adzatsekeka, ndipo sudzamva phokoso lakunja; sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo kapena kulira kwa mbalame mmawa.
Un tās divas durvis pret ielu taps aizslēgtas, tā ka malšanas skaņa paliks lēnāka, un viņš uzmostas, kad putniņa balsi dzird, un kad klusu skan visas dziesmas,
5 Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera, amaopa kuyenda mʼmisewu; Mutu umatuwa kuti mbuu, amayenda modzikoka ngati ziwala ndipo chilakolako chimatheratu. Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.
Kad arī kalnus bīsies un baiļosies, pa ceļu ejot, un kad tas mandeļu koks ziedēs, un sisenis būs par nastu, un līksmība zudīs; jo cilvēks iet uz savu mūža namu, un tie žēlotāji ies apkārt pa ielām;
6 Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke, kapena mbale yagolide isanasweke; mtsuko usanasweke ku kasupe, kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.
Pirms tā sudraba virve trūks, un tas zelta trauks saplīst un tas smeļamais pie avota izkalst, un tas skritulis pie akas salūst;
7 Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera, mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.
Jo pīšļiem būs atkal zemē griezties, kā tie ir bijuši, un garam atkal pie Dieva, kas to ir devis.
8 “Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki. “Zonse ndi zopandapake!”
Niecība vien! saka tas mācītājs, viss ir niecība!
9 Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri.
Nu vēl atliek: šis mācītājs bija gudrs, un viņš ļaudīm mācīja atzīšanu, un sadomāja un izmeklēja un sastādīja daudz sakāmus vārdus.
10 Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.
Tas mācītājs meklēja, skaistus vārdus atrast un taisnības vārdus pareizi sarakstīt.
11 Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi.
Gudru vīru vārdi ir kā dzenuļi, un kā iesistas naglas viņu (atziņas) krājumi, no viena Gana doti.
12 Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi. Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.
Un beidzot: sargies, mans dēls! Grāmatu rakstīšanai nav gala un daudz lasīšanas nopūlē miesu.
13 Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa: uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake, pakuti umenewu ndiwo udindo wa anthu onse.
Visas mācības gala vārds ir šis: bīsties Dievu un turi Viņa baušļus, jo tas pienākas visiem cilvēkiem.
14 Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse, kuphatikizanso zinthu zonse zobisika, kaya zabwino kapena zoyipa.
Jo Dievs ikkatru darbu vedīs tiesā līdz ar visu, kas ir apslēpts, vai tas labs vai ļauns.

< Mlaliki 12 >