< Mlaliki 12 >

1 Uzikumbukira mlengi wako masiku a unyamata wako, masiku oyipa asanafike, nthawi isanafike pamene udzanena kuti, “Izi sizikundikondweretsa.”
While you are still young, keep thinking about [God], who created you. Do that before [you are old] and you experience many troubles, during the years when you say “I no [longer] enjoy being alive.”
2 Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala, mwezi ndi nyenyezi zidzada. Mitambo idzabweranso mvula itagwa.
[When you become old], the light from the sun and moon and stars will [seem] dim [to you], and [it will seem that the rain] clouds [always] return [quickly] after it rains.
3 Nthawi imene manja ako adzanjenjemera, miyendo yako idzafowoka, pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka, ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.
Then your [arms that you use to protect] [MET] your bodies will shake/tremble, and your [legs that support] [MET] your bodies will become weak. Many of your [teeth that you use to] grind/chew [your food] will fall out, and your [eyes that you use to] look out of windows will not see clearly.
4 Makutu ako adzatsekeka, ndipo sudzamva phokoso lakunja; sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo kapena kulira kwa mbalame mmawa.
Your [ears] [MET] will not hear the noise in the streets, and you will not be able to hear clearly the sound of people grinding grain with millstones. You will be awakened in the morning by hearing the birds singing/chirping, [but] you will not be able to hear well the songs that (the birds/people) sing.
5 Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera, amaopa kuyenda mʼmisewu; Mutu umatuwa kuti mbuu, amayenda modzikoka ngati ziwala ndipo chilakolako chimatheratu. Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.
You will be afraid to be in high places and afraid of dangers on the roads that you walk on. [Your hair] will become [white like] [MET] the flowers of almond trees. [When you try to walk], you will drag yourself along like [MET] grasshoppers, and you will no longer desire [to have sex]. Then you will [die and] go to your eternal home, and people who will mourn for you will be in the streets.
6 Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke, kapena mbale yagolide isanasweke; mtsuko usanasweke ku kasupe, kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.
[Think much about God now, because] soon our lives will end, [like] [MET] silver chains or golden bowls that break easily, or like pitchers/jugs that are broken at the water fountain, or like broken pulleys at a well.
7 Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera, mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.
Then our corpses will [decay and] become dirt again, and our spirits will return to God, the one who gave us our spirits.
8 “Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki. “Zonse ndi zopandapake!”
[So] I say [again] that it is difficult to understand why everything happens; everything is mysterious.
9 Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri.
I was considered to be a very wise man, and I taught the people many things. I assembled/collected and wrote down many proverbs, and I carefully thought about and studied them.
10 Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.
I searched for the right words, and what I have written is reliable and true.
11 Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi.
The things that [I and other] wise people say [teach people what they should do]; they are like [SIM] (goads/sharp sticks that people use to strike animals to direct where they should go). They are like [SIM] nails that stick out of pieces of wood. They are given to us by [God, who is like] [MET] our shepherd.
12 Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi. Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.
[So], my son, pay careful attention to what I have written, and choose carefully what you read that others have written, [because] writing proverbs/books is endless, and [trying to] study them all will cause you to become exhausted.
13 Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa: uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake, pakuti umenewu ndiwo udindo wa anthu onse.
[Now] you have heard all [that I have told you], and here is the conclusion: Revere God, and obey his commandments, because those commandments summarize everything that people should do.
14 Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse, kuphatikizanso zinthu zonse zobisika, kaya zabwino kapena zoyipa.
And do not forget that God will judge everything that we do, good things and bad things, [even] things that we do secretly.

< Mlaliki 12 >