< Mlaliki 12 >
1 Uzikumbukira mlengi wako masiku a unyamata wako, masiku oyipa asanafike, nthawi isanafike pamene udzanena kuti, “Izi sizikundikondweretsa.”
And remember creator your in [the] days of youth your until that not they will come [the] days of evil and they will arrive years which you will say not [belongs] to me in them pleasure.
2 Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala, mwezi ndi nyenyezi zidzada. Mitambo idzabweranso mvula itagwa.
Until that not it will become dark the sun and the light and the moon and the stars and they will return the clouds after the rain.
3 Nthawi imene manja ako adzanjenjemera, miyendo yako idzafowoka, pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka, ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.
In the day when they will tremble [the] keepers of the house and they will bend themselves [the] people of strength and they will cease the [female] grinders for they have become few and they will grow dim the [women who] look in the windows.
4 Makutu ako adzatsekeka, ndipo sudzamva phokoso lakunja; sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo kapena kulira kwa mbalame mmawa.
And they will be shut up [the] doors on the street when becomes low [the] sound of the grinding mill for someone may arise to [the] sound of bird and they may be reduced all [the] daughters of song.
5 Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera, amaopa kuyenda mʼmisewu; Mutu umatuwa kuti mbuu, amayenda modzikoka ngati ziwala ndipo chilakolako chimatheratu. Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.
Also from a high [place] people will be afraid and terrors [are] in the way and it may blossom the almond tree so it may drag itself along the grasshopper and it may fail the caper-berry for [is] going humankind to [the] house of perpetuity its and they will go about (in the street *L(abh)*) the mourners.
6 Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke, kapena mbale yagolide isanasweke; mtsuko usanasweke ku kasupe, kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.
Until that not (it will be snapped *Q(K)*) [the] cord of silver so it may be crushed [the] bowl of gold so it may be broken [the] jar at the water spring and it will be crushed the [water] wheel to the well.
7 Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera, mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.
And it will return the dust to the earth like which it was and the spirit it will return to God who he gave it.
8 “Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki. “Zonse ndi zopandapake!”
Futility of futilities he said the Teacher everything [is] futility.
9 Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri.
And besides that he was Teacher wise again he taught knowledge the people and he weighed and he searched out he arranged in order proverbs [surely] a multitude.
10 Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.
sought Teacher to find words of delight and [what] was written uprightness [was] words of truth.
11 Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi.
[the] words of Wise [people] [are] like goads and [are] like nails firmly fixed masters of collections they are given from a shepherd one.
12 Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi. Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.
And excess more than them O child my be warned to make books many there not [is] an end and study much [is] weariness of flesh.
13 Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa: uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake, pakuti umenewu ndiwo udindo wa anthu onse.
[the] end of [the] matter Everything it has been heard God fear and commandments his keep for this [is] all humankind.
14 Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse, kuphatikizanso zinthu zonse zobisika, kaya zabwino kapena zoyipa.
For every deed God he will bring in judgment with every hidden thing whether good and or evil.