< Mlaliki 11 >

1 Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.
Fa wʼawi twa po; na daakye bi wubenya so mfaso.
2 Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu, pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.
Fa hyɛ aguadi ason mu, yiw, nea ɛto so awotwe mu, wunnim atoyerɛnkyɛm a ɛbɛba asase no so.
3 Ngati mitambo yadzaza ndi madzi, imagwetsa mvula pa dziko lapansi. Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto, ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.
Sɛ nsu ayɛ omununkum mu ma a, ɛtɔ osu gu asase so. Sɛ dua bi bu hwe anafo fam anaa atifi fam a, nea ɛhwee no, ɛhɔ ara na ɛbɛda.
4 Amene amayangʼana mphepo sadzadzala; amene amayangʼana mitambo sadzakolola.
Obiara a ɔtwɛn wim nsakrae no rennua, na nea ɔhwɛ omununkum no nso rentwa.
5 Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo, kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi, momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu, Mlengi wa zinthu zonse.
Sɛnea wunnim ɔkwan a mframa nam so, anaa sɛnea wɔnwen nipadua wɔ ɔyafunu mu no, saa ara na worentumi nte Onyankopɔn nnwuma ase, ade nyinaa Yɛfo no.
6 Dzala mbewu zako mmawa ndipo madzulo usamangoti manja lobodo, pakuti sudziwa chimene chidzapindula, mwina ichi kapena icho, kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.
Dua wʼaba anɔpa, na anwummere nso ma wo nsa nna ho, na wunnim nea ɛbɛyɛ yiye, sɛ eyi anaa eyi, anaasɛ ebia abien no nyinaa bɛyɛ yie.
7 Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.
Hann yɛ fɛ; na ɛyɛ aniwa dɛ sɛ ohu owia.
8 Munthu akakhala wa zaka zambiri, mulekeni akondwerere zaka zonsezo, koma iye azikumbukira masiku a mdima, pakuti adzakhala ochuluka. Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.
Mfe dodow a onipa bɛtena nkwa yi mu nyinaa ɛsɛ sɛ onya ahotɔ. Nanso ɛsɛ sɛ ɔkae nnabɔne na ɛbɛdɔɔso. Biribiara a ɛbɛba no yɛ ahuhude.
9 Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono, ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako. Tsatira zimene mtima wako ukufuna, ndiponso zimene maso ako akuona, koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo Mulungu adzakuweruza.
Ma wʼani nnye, aberante, bere a woyɛ ɔbabun, ma wo koma mma wo anigye wɔ wo mmerantebere mu. Di nea wo koma pɛ ne nea wʼaniwa hu akyi, nanso hu sɛ eyinom nyinaa ho Onyankopɔn de wo bɛba atemmu mu.
10 Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako, upewe zokupweteka mʼthupi mwako, pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.
Enti yi adwennwen biara fi wo koma mu na tow ɔhaw biara a ɛwɔ wo mu no gu, efisɛ mmeranteyɛ ne ahoɔden yɛ ahuhude.

< Mlaliki 11 >