< Mlaliki 11 >

1 Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.
Баци хлеб свој поврх воде; јер ћеш га наћи после много времена.
2 Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu, pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.
Раздели седморици и осморици; јер не знаш какво ће зло бити на земљи.
3 Ngati mitambo yadzaza ndi madzi, imagwetsa mvula pa dziko lapansi. Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto, ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.
Кад се напуне облаци, просипају дажд на земљу, и ако падне дрво на југ или на север, где падне дрво онде ће остати.
4 Amene amayangʼana mphepo sadzadzala; amene amayangʼana mitambo sadzakolola.
Ко пази на ветар, неће сејати, и ко гледа на облаке, неће жети.
5 Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo, kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi, momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu, Mlengi wa zinthu zonse.
Како не знаш који је пут ветру ни како постају кости у утроби трудне жене, тако не знаш дела Божијег и како твори све.
6 Dzala mbewu zako mmawa ndipo madzulo usamangoti manja lobodo, pakuti sudziwa chimene chidzapindula, mwina ichi kapena icho, kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.
Из јутра сеј семе своје и увече немој да ти почивају руке, јер не знаш шта ће бити боље, ово или оно, или ће обоје бити једнако добро.
7 Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.
Слатка је светлост, и добро је очима гледати сунце;
8 Munthu akakhala wa zaka zambiri, mulekeni akondwerere zaka zonsezo, koma iye azikumbukira masiku a mdima, pakuti adzakhala ochuluka. Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.
Али да човек живи много година и свагда се весели, па се опомене дана тамних како ће их бити много, све што је било биће таштина.
9 Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono, ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako. Tsatira zimene mtima wako ukufuna, ndiponso zimene maso ako akuona, koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo Mulungu adzakuweruza.
Радуј се, младићу, за младости своје, и нека се весели срце твоје док си млад, и ходи куда те срце твоје води и куда очи твоје гледају; али знај да ће те за све то Бог извести на суд.
10 Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako, upewe zokupweteka mʼthupi mwako, pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.
Уклони дакле жалост од срца свог, и одрини зло од тела свог, јер је детињство и младост таштина.

< Mlaliki 11 >