< Mlaliki 11 >
1 Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.
Lança teu pão sobre as águas, porque depois de muitos dias tu o encontrarás.
2 Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu, pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.
Dá uma parte a sete, e até a oito; porque não sabes que mal haverá sobre a terra.
3 Ngati mitambo yadzaza ndi madzi, imagwetsa mvula pa dziko lapansi. Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto, ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.
Se as nuvens estiverem cheias, há chuva sobre a terra; e se a árvore cair, seja para ou sul ou seja para o norte, no lugar em que a árvore cair, ali ela ficará.
4 Amene amayangʼana mphepo sadzadzala; amene amayangʼana mitambo sadzakolola.
Quem ficar dando atenção ao vento, nunca semeará; e o que olhar para as nuvens nunca ceifará.
5 Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo, kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi, momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu, Mlengi wa zinthu zonse.
Assim como tu não sabes qual é o caminho do vento, [nem] como se formam os ossos [do feto] no ventre da grávida, assim também tu não sabes a obra de Deus, que faz todas as coisas.
6 Dzala mbewu zako mmawa ndipo madzulo usamangoti manja lobodo, pakuti sudziwa chimene chidzapindula, mwina ichi kapena icho, kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.
Pela manhã semeia tua semente, e à tarde não retires tua mão; pois tu não sabes qual [tentativa] dará certo, se uma, se outra, ou se ambas [as tentativas] serão boas.
7 Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.
Certamente a luz é agradável, e ver o sol é bom para os olhos.
8 Munthu akakhala wa zaka zambiri, mulekeni akondwerere zaka zonsezo, koma iye azikumbukira masiku a mdima, pakuti adzakhala ochuluka. Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.
Mesmo se o homem viver muitos anos, [e] em todos eles se alegrar, ele também deve se lembrar dos dias de trevas, porque serão muitos. Tudo o que acontece é futilidade.
9 Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono, ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako. Tsatira zimene mtima wako ukufuna, ndiponso zimene maso ako akuona, koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo Mulungu adzakuweruza.
Alegra-te, rapaz, em tua juventude; e agrada o teu coração nos dias de tua juventude; e anda pelos caminhos do teu coração, e na vista de teus olhos; sabe, porém, que por todas estas coisas, Deus te trará a julgamento.
10 Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako, upewe zokupweteka mʼthupi mwako, pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.
[Portanto] afasta o desagrado de teu coração, e tira de tua carne o mal; pois a adolescência e a juventude são futilidade.