< Mlaliki 11 >

1 Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.
Jette ton pain sur la face des eaux, car après beaucoup de jours tu le retrouveras;
2 Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu, pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.
donnes-en une part à sept, et même à huit: car tu ne sais pas quel malheur peut arriver sur la terre.
3 Ngati mitambo yadzaza ndi madzi, imagwetsa mvula pa dziko lapansi. Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto, ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.
Quand les nuées sont remplies de pluie, elles se vident sur la terre; et si un arbre tombe au midi ou au nord, il reste à la place où il est tombé.
4 Amene amayangʼana mphepo sadzadzala; amene amayangʼana mitambo sadzakolola.
Celui qui observe le vent ne sèmera point, et celui qui interroge les nuages ne moissonnera point.
5 Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo, kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi, momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu, Mlengi wa zinthu zonse.
Comme tu ne sais pas quel est le chemin du vent et comment se forment les os dans le sein de la mère, ainsi tu ne connais pas l’œuvre de Dieu, qui fait toutes choses.
6 Dzala mbewu zako mmawa ndipo madzulo usamangoti manja lobodo, pakuti sudziwa chimene chidzapindula, mwina ichi kapena icho, kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.
Dès le matin sème ta semence, et le soir ne laisse pas reposer ta main, car tu ne sais pas ce qui réussira, ceci ou cela, ou si l’un et l’autre ne sont pas également bons.
7 Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.
La lumière est douce, et c’est un plaisir pour l’œil de voir le soleil.
8 Munthu akakhala wa zaka zambiri, mulekeni akondwerere zaka zonsezo, koma iye azikumbukira masiku a mdima, pakuti adzakhala ochuluka. Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.
Même si l’homme vit de nombreuses années, qu’il se réjouisse pendant toutes ces années, et qu’il pense aux jours de ténèbres, car ils seront nombreux: tout ce qui arrive est vanité.
9 Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono, ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako. Tsatira zimene mtima wako ukufuna, ndiponso zimene maso ako akuona, koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo Mulungu adzakuweruza.
Jeune homme, réjouis-toi dans ta jeunesse; que ton cœur te donne de la joie dans les jours de ta jeunesse! Marche dans les voies de ton cœur, et selon les regards de tes yeux; mais sache que pour tout cela Dieu te fera venir en jugement.
10 Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako, upewe zokupweteka mʼthupi mwako, pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.
Bannis de ton cœur le chagrin, et éloigne le mal de ta chair; la jeunesse et l’adolescence sont vanité.

< Mlaliki 11 >