< Mlaliki 11 >

1 Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.
Give generously to others [some of] the money [MET] that you have; if you do that, later you will get back an equal amount.
2 Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu, pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.
Share some of what you have with (seven or eight/several) [others], because you do not know when you will experience a disaster, [and if you give some of what you have to others], [when you experience that disaster, they will kindly help you].
3 Ngati mitambo yadzaza ndi madzi, imagwetsa mvula pa dziko lapansi. Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto, ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.
[It is always true that] when clouds are full of water, they pour rain on the earth. [Similarly], wherever a tree falls on the ground, that is where it will remain.
4 Amene amayangʼana mphepo sadzadzala; amene amayangʼana mitambo sadzakolola.
If farmers see in what direction the wind is blowing, they will know whether it is wise at that time to plant things or not. [It is also true that] if farmers look at the clouds [and see that they are blowing from the west, which means that it will probably rain, ] they will not [try to] harvest their crops on that day.
5 Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo, kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi, momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu, Mlengi wa zinthu zonse.
We do not know where the wind comes from or where it goes, and we do not know how bodies are formed in women’s wombs. Similarly [SIM], God is the one who made everything, and we cannot [fully] understand what God does.
6 Dzala mbewu zako mmawa ndipo madzulo usamangoti manja lobodo, pakuti sudziwa chimene chidzapindula, mwina ichi kapena icho, kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.
[Start] planting your seeds in the morning, and do not stop planting them until the evening, because you do not know which ones will grow better, the ones you plant in the morning or the ones you plant later in the day, or whether both will grow well.
7 Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.
It is very delightful to be alive and see [MTY] the sun [rise every morning].
8 Munthu akakhala wa zaka zambiri, mulekeni akondwerere zaka zonsezo, koma iye azikumbukira masiku a mdima, pakuti adzakhala ochuluka. Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.
[Even] if people live for many years, they should enjoy all of them. But they should not forget that [some day they will die] and then they will never be able to see any light again, and we do not know what will happen to us after we die.
9 Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono, ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako. Tsatira zimene mtima wako ukufuna, ndiponso zimene maso ako akuona, koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo Mulungu adzakuweruza.
You young people, be happy while you are still young. Enjoy [IDM] doing the things that you want to do. But do not forget that [some day] God will judge you concerning all the things that you do.
10 Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako, upewe zokupweteka mʼthupi mwako, pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.
[So when you are young] [MTY], do not worry about anything, and do not pay attention to the pains that you have in your body, because we will not remain young and strong forever.

< Mlaliki 11 >