< Mlaliki 11 >
1 Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.
Send bread your on [the] surface of the waters for in [the] abundance of days you will find it.
2 Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu, pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.
Give a portion to seven and also to eight for not you know what? will it be calamity on the earth.
3 Ngati mitambo yadzaza ndi madzi, imagwetsa mvula pa dziko lapansi. Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto, ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.
If they will be filled the clouds rain on the earth they will pour [it] out and whether it falls a tree at the south and or at the north [the] place where it falls the tree there it will be.
4 Amene amayangʼana mphepo sadzadzala; amene amayangʼana mitambo sadzakolola.
[one who] watches for A wind not he will sow and [one who] looks on the clouds not he will reap.
5 Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo, kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi, momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu, Mlengi wa zinthu zonse.
Just as not you [are] knowing what? [is] [the] way of the wind like bones in [the] womb of the full [woman] thus not you know [the] work of God who he makes everything.
6 Dzala mbewu zako mmawa ndipo madzulo usamangoti manja lobodo, pakuti sudziwa chimene chidzapindula, mwina ichi kapena icho, kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.
In the morning sow seed your and to the evening may not you give rest to hand your for not you [are] knowing where? this will it succeed ¿ this or? this and or? [will] both of them as one [be] good.
7 Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.
And [is] sweet the light and [is] good for the eyes to see the sun.
8 Munthu akakhala wa zaka zambiri, mulekeni akondwerere zaka zonsezo, koma iye azikumbukira masiku a mdima, pakuti adzakhala ochuluka. Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.
That except years [surely] a multitude will live person in all of them let him be take pleasure and he may remember [the] days of darkness for [surely] many will be all that has come [is] futility.
9 Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono, ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako. Tsatira zimene mtima wako ukufuna, ndiponso zimene maso ako akuona, koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo Mulungu adzakuweruza.
Rejoice O young man in youth your and let it make good you heart your in [the] days of youth your and walk in [the] ways of heart your and in [the] sight of eyes your and know that on all these [things] he will bring you God in judgment.
10 Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako, upewe zokupweteka mʼthupi mwako, pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.
And remove vexation from heart your and put away evil from flesh your for youth and the black hair [are] futility.