< Mlaliki 11 >

1 Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.
Kast dit Brød paa Vandet; thi du skal finde det længe derefter.
2 Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu, pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.
Del ud til syv, ja, og til otte; thi du kan ikke vide, hvad for Ulykke der skal ske paa Jorden.
3 Ngati mitambo yadzaza ndi madzi, imagwetsa mvula pa dziko lapansi. Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto, ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.
Naar Skyerne ere fulde af Regn, udgyde de den paa Jorden; og naar et Træ falder imod Sønden eller og imod Norden, paa hvilket Sted Træet vil falde, der falder det.
4 Amene amayangʼana mphepo sadzadzala; amene amayangʼana mitambo sadzakolola.
Hvo som agter paa Vejr, saar ikke, og hvo som ser paa Skyerne, høster ikke.
5 Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo, kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi, momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu, Mlengi wa zinthu zonse.
Ligesom du ikke ved, hvilken Vindens Vej er, saa lidet som du ved, hvorledes Benene dannes i den frugtsommeliges Liv, saaledes kan du heller ikke vide Guds Gerning, hvorledes han gør det alt sammen.
6 Dzala mbewu zako mmawa ndipo madzulo usamangoti manja lobodo, pakuti sudziwa chimene chidzapindula, mwina ichi kapena icho, kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.
Saa din Sæd om Morgenen, og lad din Haand ikke hvile om Aftenen; thi du ved ikke, enten dette eller hint skal lykkes, eller om de begge skulle blive lige gode.
7 Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.
Og sødt er Lyset, og lysteligt er det for Øjnene at se Solen.
8 Munthu akakhala wa zaka zambiri, mulekeni akondwerere zaka zonsezo, koma iye azikumbukira masiku a mdima, pakuti adzakhala ochuluka. Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.
Thi lever Mennesket endog mange Aar, skal han glæde sig i dem alle og komme de mørke Dage i Hu; thi de ville blive mange; alt det, der kommer, er Forfængelighed.
9 Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono, ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako. Tsatira zimene mtima wako ukufuna, ndiponso zimene maso ako akuona, koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo Mulungu adzakuweruza.
Glæd dig, du unge! i din Ungdom, og lad dit Hjerte være vel til Mode i din Ungdoms Dage, og vandre efter dit Hjertes Veje og efter dine Øjnes Syn; men vid, at for alt dette skal Gud føre dig for Dommen.
10 Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako, upewe zokupweteka mʼthupi mwako, pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.
Og bortfjern Græmmelse fra dit Hjerte, og lad Lidelser gaa bort fra dit Kød; thi Ungdom og Livets Morgenrøde ere Forfængelighed.

< Mlaliki 11 >