< Mlaliki 10 >

1 Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira, choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
Las moscas muertas hacen que el aceite del perfumista produzca un mal olor; así que un poco de locura supera la sabiduría y el honor.
2 Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino, koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
El corazón del hombre sabio está a su derecha, sino el corazón de un necio a su izquierda.
3 Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu, zochita zake ndi zopanda nzeru ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
También cuando el necio va por el camino, le falla el entendimiento y dice a todos que es un necio.
4 Ngati wolamulira akukwiyira, usachoke pa ntchito yako; kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.
Si el espíritu del gobernante se levanta contra ti, no dejes tu lugar; porque la mansedumbre hace descansar las grandes ofensas.
5 Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano, kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
Hay un mal que he visto bajo el sol, la clase de error que procede del gobernante.
6 Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba, pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
La insensatez está puesta en gran dignidad, y los ricos se sientan en un lugar bajo.
7 Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.
He visto siervos sobre caballos, y príncipes que caminan como siervos sobre la tierra.
8 Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha; amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
El que cava una fosa puede caer en ella; y el que rompe un muro puede ser mordido por una serpiente.
9 Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo; amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.
El que talla piedras puede ser herido por ellas. El que parte la madera puede peligrar con ella.
10 Ngati nkhwangwa ili yobuntha yosanoledwa, pamafunika mphamvu zambiri potema, koma luso limabweretsa chipambano.
Si el hacha está desafilada y uno no afila el filo, debe usar más fuerza; pero la habilidad trae el éxito.
11 Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka ngati njokayo yakuluma kale.
Si la serpiente muerde antes de ser encantada, entonces no hay beneficio para la lengua del encantador.
12 Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa, koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
Las palabras de la boca del sabio son graciosas; pero al necio se lo tragan sus propios labios.
13 Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa; potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
El principio de las palabras de su boca es necedad; y el fin de su charla, locura maligna.
14 ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu. Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?
El necio también multiplica las palabras. El hombre no sabe lo que va a ser; y lo que va a ser después de él, ¿quién se lo puede decir?
15 Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa; ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.
El trabajo de los necios cansa a cada uno de ellos, pues no sabe cómo ir a la ciudad.
16 Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana, ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
Ay de ti, tierra, cuando tu rey es un niño, ¡y tus príncipes comen por la mañana!
17 Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake, kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.
Feliz eres, tierra, cuando tu rey es hijo de nobles, y tus príncipes comen a su debido tiempo, ¡para la fuerza, y no para la embriaguez!
18 Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka; ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.
Por pereza se hunde el techo; y por la ociosidad de las manos la casa gotea.
19 Phwando ndi lokondweretsa anthu, ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo, koma ndalama ndi yankho la chilichonse.
Se hace una fiesta para reír, y el vino alegra la vida; y el dinero es la respuesta para todas las cosas.
20 Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako, kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako, pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako nʼkukafotokoza zomwe wanena.
No maldigas al rey, no, no en tus pensamientos; y no maldigas a los ricos en tu habitación, porque un pájaro del cielo puede llevar tu voz, y lo que tiene alas puede contar el asunto.

< Mlaliki 10 >