< Mlaliki 10 >
1 Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira, choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
Des mouches mortes font exhaler une odeur fétide à l'huile du parfumeur; un peu de folie a la prépondérance sur la sagesse et l'honneur.
2 Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino, koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
La raison du sage est à sa droite; la raison du fou est à sa gauche.
3 Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu, zochita zake ndi zopanda nzeru ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
Quelle que soit la voie que suive le fou, il manque de sens, et il dit à chacun qu'il est un fou.
4 Ngati wolamulira akukwiyira, usachoke pa ntchito yako; kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.
Si la colère du souverain s'élève contre toi, ne cède pas la place, car le calme fait céder de grands péchés.
5 Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano, kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
Il est un mal que j'ai vu sous le soleil, par l'effet d'une méprise qui procède du prince:
6 Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba, pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
la folie est placée en très haut lieu, et des riches sont assis en lieu bas.
7 Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.
J'ai vu des esclaves montés sur des chevaux, et des princes marchant à pied comme des esclaves. –
8 Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha; amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
Celui qui creuse une fosse, y tombera; et celui qui fait une brèche à un mur, sera mordu par un serpent.
9 Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo; amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.
Celui qui remue des pierres, s'y fera mal, et celui qui fend du bois, se risque;
10 Ngati nkhwangwa ili yobuntha yosanoledwa, pamafunika mphamvu zambiri potema, koma luso limabweretsa chipambano.
si le fer est émoussé, et qu'il n'en affile pas le tranchant, il lui faudra un effort plus grand; mais la sagesse a l'avantage de donner l'adresse.
11 Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka ngati njokayo yakuluma kale.
Si le serpent mord quand il n'est pas enchanté, l'enchanteur ne sert à rien. –
12 Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa, koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
Les discours de la bouche du sage ont la grâce; mais le fou est la victime de ses propres lèvres;
13 Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa; potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
le début des paroles de sa bouche est folie, et la fin de son discours est un délire malfaisant.
14 ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu. Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?
Et le fou prodigue les paroles; [cependant] l'homme ignore l'avenir, et qui lui découvre ce qui aura lieu après lui?
15 Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa; ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.
Le travail du fou le fatigue, car il ne sait pas trouver le chemin de la ville. –
16 Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana, ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
Malheur à toi, pays, qui as pour roi un enfant, et dont les princes se mettent à table dès le matin!
17 Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake, kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.
Bonheur à toi, pays, qui as pour roi un fils de noble race, et dont les princes se mettent à table en temps convenable, pour se restaurer, et non pour boire!
18 Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka; ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.
Quand il y a paresse, la charpente se disloque; et, quand les mains sont lâches, le logis a des voies d'eau. –
19 Phwando ndi lokondweretsa anthu, ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo, koma ndalama ndi yankho la chilichonse.
On apprête un festin pour se réjouir, et le vin égaie les vivants; et l'argent répond à tout. –
20 Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako, kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako, pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako nʼkukafotokoza zomwe wanena.
Même dans ta pensée ne maudis pas le roi; et au fond de la chambre où tu couches, ne maudis pas le riche! Car l'oiseau du ciel emportera tes propos, et le volatile ailé publiera tes discours.