< Mlaliki 10 >
1 Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira, choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
Les mouches mortes font que l'huile du parfumeur produit une mauvaise odeur; ainsi un peu de folie l'emporte sur la sagesse et l'honneur.
2 Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino, koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
Le cœur du sage est à sa droite, mais le cœur d'un insensé à sa gauche.
3 Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu, zochita zake ndi zopanda nzeru ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
Oui, même quand l'insensé marche sur le chemin, son intelligence lui fait défaut, et il dit à tout le monde qu'il est un insensé.
4 Ngati wolamulira akukwiyira, usachoke pa ntchito yako; kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.
Si l'esprit du chef s'élève contre toi, ne quitte pas ta place, car la douceur met en repos les grandes offenses.
5 Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano, kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
Il y a un mal que j'ai vu sous le soleil, c'est le genre d'erreur qui vient du chef.
6 Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba, pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
La folie est placée dans une grande dignité, et les riches sont assis dans un lieu bas.
7 Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.
J'ai vu des serviteurs sur des chevaux, et des princes marchant comme des serviteurs sur la terre.
8 Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha; amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
Celui qui creuse une fosse peut y tomber, et celui qui perce un mur peut être mordu par un serpent.
9 Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo; amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.
Celui qui taille des pierres peut être blessé par elles. Celui qui fend du bois peut être mis en danger par celui-ci.
10 Ngati nkhwangwa ili yobuntha yosanoledwa, pamafunika mphamvu zambiri potema, koma luso limabweretsa chipambano.
Si la hache est émoussée, et qu'on n'en aiguise pas le tranchant, il faut employer plus de force; mais l'habileté fait réussir.
11 Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka ngati njokayo yakuluma kale.
Si le serpent mord avant d'être charmé, la langue du charmeur n'y gagne rien.
12 Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa, koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
Les paroles de la bouche du sage sont agréables, mais l'insensé est avalé par ses propres lèvres.
13 Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa; potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
Le commencement des paroles de sa bouche est folie, et la fin de son discours est folie malicieuse.
14 ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu. Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?
L'insensé multiplie aussi les paroles. L'homme ne sait pas ce qui sera; et ce qui sera après lui, qui peut le dire?
15 Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa; ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.
Le travail des insensés fatigue chacun d'eux, car il ne sait pas comment aller à la ville.
16 Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana, ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
Malheur à toi, pays, quand ton roi est un enfant, et tes princes mangent le matin!
17 Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake, kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.
Heureux es-tu, pays, quand ton roi est le fils de nobles, et vos princes mangent en temps voulu, pour la force, et non pour l'ivresse!
18 Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka; ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.
Par la paresse, le toit s'enfonce; et par l'oisiveté des mains, la maison fuit.
19 Phwando ndi lokondweretsa anthu, ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo, koma ndalama ndi yankho la chilichonse.
On fait un festin pour rire, et le vin rend la vie heureuse; et l'argent est la réponse à tout.
20 Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako, kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako, pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako nʼkukafotokoza zomwe wanena.
Ne maudissez pas le roi, non, pas dans vos pensées; et ne maudissez pas les riches dans votre chambre, car un oiseau du ciel peut porter votre voix, et ce qui a des ailes peut en parler.