< Mlaliki 10 >

1 Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira, choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
Dead flies cause the ointment of the perfumer to send forth a stinking savour: [so] doth a little folly outweigh wisdom and honour.
2 Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino, koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
A wise man’s heart is at his right hand; but a fool’s heart at his left.
3 Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu, zochita zake ndi zopanda nzeru ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
Yea also, when the fool walketh by the way, his understanding faileth him, and he saith to every one [that] he is a fool.
4 Ngati wolamulira akukwiyira, usachoke pa ntchito yako; kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.
If the spirit of the ruler rise up against thee, leave not thy place; for yielding allayeth great offences.
5 Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano, kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
There is an evil which I have seen under the sun, as it were an error which proceedeth from the ruler:
6 Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba, pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
folly is set in great dignity, and the rich sit in low place.
7 Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.
I have seen servants upon horses, and princes walking as servants upon the earth.
8 Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha; amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
He that diggeth a pit shall fall into it; and whoso breaketh through a fence, a serpent shall bite him.
9 Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo; amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.
Whoso heweth out stones shall be hurt therewith; [and] he that cleaveth wood is endangered thereby.
10 Ngati nkhwangwa ili yobuntha yosanoledwa, pamafunika mphamvu zambiri potema, koma luso limabweretsa chipambano.
If the iron be blunt, and one do not whet the edge, then must he put to more strength: but wisdom is profitable to direct.
11 Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka ngati njokayo yakuluma kale.
If the serpent bite before it be charmed, then is there no advantage in the charmer.
12 Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa, koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
The words of a wise man’s mouth are gracious; but the lips of a fool will swallow up himself.
13 Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa; potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
The beginning of the words of his mouth is foolishness: and the end of his talk is mischievous madness.
14 ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu. Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?
A fool also multiplieth words: [yet] man knoweth not what shall be; and that which shall be after him, who can tell him?
15 Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa; ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.
The labour of fools wearieth every one of them, for he knoweth not how to go to the city.
16 Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana, ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
Woe to thee, O land, when thy king is a child, and thy princes eat in the morning!
17 Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake, kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.
Happy art thou, O land, when thy king is the son of nobles, and thy princes eat in due season, for strength, and not for drunkenness!
18 Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka; ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.
By slothfulness the roof sinketh in; and through idleness of the hands the house leaketh.
19 Phwando ndi lokondweretsa anthu, ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo, koma ndalama ndi yankho la chilichonse.
A feast is made for laughter, and wine maketh glad the life: and money answereth all things.
20 Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako, kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako, pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako nʼkukafotokoza zomwe wanena.
Curse not the king, no, not in thy thought; and curse not the rich in thy bedchamber: for a bird of the air shall carry the voice, and that which hath wings shall tell the matter.

< Mlaliki 10 >