< Mlaliki 10 >

1 Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira, choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
Pestilent flies will corrupt a preparation of sweet ointment: [and] a little wisdom is more precious than great glory of folly.
2 Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino, koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
A wise man's heart is at his right hand; but a fool's heart at his left.
3 Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu, zochita zake ndi zopanda nzeru ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
Yes, and whenever a fool walks by the way, his heart will fail him, and all that he thinks of is folly.
4 Ngati wolamulira akukwiyira, usachoke pa ntchito yako; kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.
If the spirit of the ruler rise up against you, leave not your place; for soothing will put an end to great offenses.
5 Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano, kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
There is an evil which I have seen under the sun, wherein an error has proceeded from the ruler.
6 Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba, pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
The fool has been set in very high places, while rich men would sit in a low one.
7 Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.
I have seen servants upon horses, and princes walking as servants on the earth.
8 Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha; amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
He that digs a pit shall fall into it; and him that breaks down a hedge a serpent shall bite.
9 Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo; amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.
He that removes stones shall be troubled thereby; he that cleaves wood shall be endangered thereby.
10 Ngati nkhwangwa ili yobuntha yosanoledwa, pamafunika mphamvu zambiri potema, koma luso limabweretsa chipambano.
If the axe-head should fall off, then the man troubles his countenance, and he must put forth more strength: and [in that case] skill is of no advantage to a man.
11 Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka ngati njokayo yakuluma kale.
If a serpent bite when there is no [charmer's] whisper, then there is no advantage to the charmer.
12 Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa, koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
The words of a wise mouth are gracious: but the lips of a fool will swallow him up.
13 Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa; potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
The beginning of the words of his mouth is folly: and the end of his talk mischievous madness.
14 ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu. Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?
A fool moreover multiplies words: man knows not what has been, nor what will be: who shall tell him what will come after him?
15 Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa; ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.
The labor of fools will afflict them, [as that of one] who knows not to go to the city.
16 Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana, ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
Woe to you, O city, whose king is young, and your princes eat in the morning!
17 Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake, kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.
Blessed are you, O land, whose king is a son of nobles, and whose princes shall eat seasonably, for strength, and shall not be ashamed.
18 Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka; ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.
By slothful neglect a building will be brought low: and by idleness of the hands the house will fall to pieces.
19 Phwando ndi lokondweretsa anthu, ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo, koma ndalama ndi yankho la chilichonse.
Men prepare bread for laughter, and wine and oil that the living should rejoice: but to money all things will humbly yield obedience.
20 Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako, kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako, pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako nʼkukafotokoza zomwe wanena.
Even in your conscience, curse not the king; and curse not the rich in your bedchamber: for a bird of the air shall carry your voice, and that which has wings shall report your speech.

< Mlaliki 10 >