< Mlaliki 1 >

1 Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
The words of Ecclesiastes, the son of David, the king of Jerusalem.
2 “Zopandapake! Zopandapake!” atero Mlaliki. “Zopandapake kotheratu! Zopandapake.”
Ecclesiastes said: Vanity of vanities! Vanity of vanities, and all is vanity!
3 Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
What more does a man have from all his labor, as he labors under the sun?
4 Mibado imabwera ndipo mibado imapita, koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
A generation passes away, and a generation arrives. But the earth stands forever.
5 Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
The sun rises and sets; it returns to its place, and from there, being born again,
6 Mphepo imawombera cha kummwera ndi kukhotera cha kumpoto; imawomba mozungulirazungulira, kumangobwererabwerera komwe yachokera.
it circles through the south, and arcs toward the north. The spirit continues on, illuminating everything in its circuit, and turning again in its cycle.
7 Mitsinje yonse imakathira ku nyanja, koma nyanjayo sidzaza; kumene madziwo amachokera, amabwereranso komweko.
All rivers enter into the sea, and the sea does not overflow. To the place from which the rivers go out, they return, so that they may flow again.
8 Zinthu zonse ndi zotopetsa, kutopetsa kwake ndi kosaneneka. Maso satopa ndi kuona kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
Such things are difficult; man is not able to explain them with words. The eye is not satisfied by seeing, nor is the ear fulfilled by hearing.
9 Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso, zomwe zinachitika kale zidzachitikanso. Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
What is it that has existed? The same shall exist in the future. What is it that has been done? The same shall continue to be done.
10 Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti, “Taona! Ichi ndiye chatsopano?” Chinalipo kale, kalekale; chinalipo ife kulibe.
There is nothing new under the sun. Neither is anyone able to say: “Behold, this is new!” For it has already been brought forth in the ages that were before us.
11 Anthu akale sakumbukiridwa, ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu sadzakumbukiridwa ndi iwo amene adzabwere pambuyo pawo.
There is no remembrance of the former things. Indeed, neither shall there be any record of past things in the future, for those who will exist at the very end.
12 Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.
I, Ecclesiastes, was king of Israel at Jerusalem.
13 Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!
And I was determined in my mind to seek and to investigate wisely, concerning all that is done under the sun. God has given this very difficult task to the sons of men, so that they may be occupied by it.
14 Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
I have seen all that is done under the sun, and behold: all is emptiness and an affliction of the spirit.
15 Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa; chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
The perverse are unwilling to be corrected, and the number of the foolish is boundless.
16 Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”
I have spoken in my heart, saying: “Behold, I have achieved greatness, and I have surpassed all the wise who were before me in Jerusalem.” And my mind has contemplated many things wisely, and I have learned.
17 Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
And I have dedicated my heart, so that I may know prudence and doctrine, and also error and foolishness. Yet I recognize that, in these things also, there is hardship, and affliction of the spirit.
18 Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso: chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.
Because of this, with much wisdom there is also much anger. And whoever adds knowledge, also adds hardship.

< Mlaliki 1 >