< Deuteronomo 9 >

1 Mvera Israeli. Watsala pangʼono kuwoloka Yorodani ndi kukathamangitsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa iweyo, imene mizinda yake ndi ikuluikulu yokhala ndi makoma ofika mpaka kumwamba.
to hear: hear Israel you(m. s.) to pass [the] day [obj] [the] Jordan to/for to come (in): come to/for to possess: take nation great: large and mighty from you city great: large and to gather/restrain/fortify in/on/with heaven
2 Anthuwo ndi ataliatali, Aanaki! Ukudziwa za iwo ndipo unamvapo zikunenedwa kuti, “Ndani amene angalimbane ndi Aanaki?”
people great: large and to exalt son: child Anakite which you(m. s.) to know and you(m. s.) to hear: hear who? to stand to/for face: before son: child Anak
3 Koma khulupirira lero kuti Yehova Mulungu wako amene ali patsogolo pako ali ngati moto wonyeketsa. Adzawononga iwowo ndipo adzawagonjetsa iweyo ukuona. Pamenepo udzawathamangitsa ndi kuwakantha mwamsanga, monga momwe Yehova wakulonjezera.
and to know [the] day for LORD God your he/she/it [the] to pass to/for face: before your fire to eat he/she/it to destroy them and he/she/it be humble them to/for face: before your and to possess: take them and to perish them quickly like/as as which to speak: promise LORD to/for you
4 Yehova Mulungu wako akadzawapirikitsa pamaso pako, usadzanene mu mtima mwako kuti, “Yehova wandibweretsa kuno kudzalanda dziko lino chifukwa cha kulungama kwanga.” Ayi, koma ndi chifukwa cha kuyipa kwa anthu amene Yehova ati awapirikitse pamaso pako.
not to say in/on/with heart your in/on/with to thrust LORD God your [obj] them from to/for face: before your to/for to say in/on/with righteousness my to come (in): bring me LORD to/for to possess: take [obj] [the] land: country/planet [the] this and in/on/with wickedness [the] nation [the] these LORD to possess: take them from face: before your
5 Sukalowa ndi kutenga dziko lawolo chifukwa cha kulungama kwako kapena kukhulupirika kwako koma chifukwa cha kuyipa kwa anthuwo. Yehova Mulungu wako awapirikitsa pamaso pako kuti akwaniritse zimene analumbira kwa makolo ako Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
not in/on/with righteousness your and in/on/with uprightness heart your you(m. s.) to come (in): come to/for to possess: take [obj] land: country/planet their for in/on/with wickedness [the] nation [the] these LORD God your to possess: take them from face: before your and because to arise: establish [obj] [the] word which to swear LORD to/for father your to/for Abraham to/for Isaac and to/for Jacob
6 Tsono zindikira kuti si chifukwa cha kulungama kwako kuti Yehova Mulungu wako akukupatsa dziko labwinoli kuti ulitenge popeza ndiwe wokanika.
and to know for not in/on/with righteousness your LORD God your to give: give to/for you [obj] [the] land: country/planet [the] pleasant [the] this to/for to possess: take her for people severe neck you(m. s.)
7 Kumbukirani izi ndipo musayiwale mmene munaputira mkwiyo wa Yehova Mulungu mʼchipululu muja. Kuyambira tsiku limene munatuluka mu Igupto mpaka pamene munafika kuno, mwakhala owukira Yehova.
to remember not to forget [obj] which be angry [obj] LORD God your in/on/with wilderness to/for from [the] day which to come out: come from land: country/planet Egypt till to come (in): come you till [the] place [the] this to rebel to be with LORD
8 Ku Horebu munaputa mkwiyo wa Yehova, kotero kuti anakwiya kwambiri nafuna kukuwonongani.
and in/on/with Horeb be angry [obj] LORD and be angry LORD in/on/with you to/for to destroy [obj] you
9 Nditakwera ku phiri kuti ndikalandire miyala iwiri ya malamulo, ya pangano limene Yehova anachita ndi inu, ndinakhala ku phiriko kwa masiku makumi anayi usiku ndi usana, sindinadye buledi kapena kumwa madzi.
in/on/with to ascend: rise I [the] mountain: mount [to] to/for to take: recieve tablet [the] stone tablet [the] covenant which to cut: make(covenant) LORD with you and to dwell in/on/with mountain: mount forty day and forty night food: bread not to eat and water not to drink
10 Yehova anandipatsa miyala iwiri yolembedwa ndi chala chake. Pa miyalapo panali malamulo onse amene Yehova analengeza kwa inu pa phiri kuchokera mʼmoto pa tsiku la msonkhano.
and to give: give LORD to(wards) me [obj] two tablet [the] stone to write in/on/with finger God and upon them like/as all [the] word which to speak: speak LORD with you in/on/with mountain: mount from midst [the] fire in/on/with day [the] assembly
11 Pakutha pa masiku makumi anayi usiku ndi usana, Yehova anandipatsa miyala iwiri, miyala ya pangano.
and to be from end forty day and forty night to give: give LORD to(wards) me [obj] two tablet [the] stone tablet [the] covenant
12 Tsono Yehova anandiwuza, “Tsikako kuno msanga, chifukwa anthu ako aja unawatulutsa ku Iguptowa adziyipitsa. Iwo apatukapo mofulumira pa zimene ndinawalamulira ndipo adzipangira fano lachitsulo.”
and to say LORD to(wards) me to arise: rise to go down quickly from this for to ruin people your which to come out: send from Egypt to turn aside: turn aside quickly from [the] way: conduct which to command them to make to/for them liquid
13 Ndipo Yehova anati kwa ine, “Anthu awa ndawaona ndipo ndi anthu okanikadi!
and to say LORD to(wards) me to/for to say to see: see [obj] [the] people [the] this and behold people severe neck he/she/it
14 Ndilekeni ndiwawononge ndi kufafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Ndipo ndidzakuyesa iwe mtundu wa anthu wamphamvu ndi wochuluka kuposa iwo.”
to slacken from me and to destroy them and to wipe [obj] name their from underneath: under [the] heaven and to make [obj] you to/for nation mighty and many from him
15 Choncho ndinatembenuka ndi kutsika phiri moto ukanayakabe. Ndipo miyala iwiri ya pangano inali mʼmanja mwanga.
and to turn and to go down from [the] mountain: mount and [the] mountain: mount to burn: burn in/on/with fire and two tablet [the] covenant upon two hand my
16 Ine poyangʼana ndinaona kuti inu munachimwira Yehova Mulungu wanu. Munadzipangira fano lowumbidwa ngati mwana wangʼombe. Inuyo munapatuka msanga kuchoka pa njira imene Yehova anakulamulirani.
and to see: see and behold to sin to/for LORD God your to make to/for you calf liquid to turn aside: turn aside quickly from [the] way: conduct which to command LORD [obj] you
17 Motero ine ndinaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwanga, ndi kuyiphwanya inu mukuona.
and to capture in/on/with two [the] tablet and to throw them from upon two hand my and to break them to/for eye: before(the eyes) your
18 Tsono nthawi yomweyo ndinagwa chafufumimba pamaso pa Yehova kwa masiku makumi anayi usiku ndi usana. Sindinadye buledi kapena kumwa madzi chifukwa cha machimo onse amene munawachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kumukwiyitsa kwambiri.
and to fall: fall to/for face: before LORD like/as first: previous forty day and forty night food: bread not to eat and water not to drink upon all sin your which to sin to/for to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD to/for to provoke him
19 Ine ndinachita mantha ndi mkwiyo ndi ukali wa Yehova chifukwa anakwiya nanu kokwanira kukuwonongani. Koma Yehova anandimveranso.
for to fear from face of [the] face: anger and [the] rage which be angry LORD upon you to/for to destroy [obj] you and to hear: hear LORD to(wards) me also in/on/with beat [the] he/she/it
20 Ndipo Yehova anakwiya ndi Aaroni ndipo akanamuwononga, koma ine ndinamupemphereranso Aaroniyo.
and in/on/with Aaron be angry LORD much to/for to destroy him and to pray also about/through/for Aaron in/on/with time ([the] he/she/it *L(abh)*)
21 Ndiponso ndinatenga chinthu chanu choyipacho, mwana wangʼombe amene munapangayo, ndi kumuwotcha pa moto. Kenaka ndinamuphwanya ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi ndipo ndinawaza fumbilo mu mtsinje umene unkayenda kuchokera mʼphiri.
and [obj] sin your which to make [obj] [the] calf to take: take and to burn [obj] him in/on/with fire and to crush [obj] him to grind be good till which to crush to/for dust and to throw [obj] dust his to(wards) [the] torrent: river [the] to go down from [the] mountain: mount
22 Inu munamukwiyitsanso Yehova ku Tabera, ku Masa ndi ku Kibiroti Hatava.
and in/on/with Taberah and in/on/with Massah and in/on/with Kibroth-hattaavah Kibroth-hattaavah be angry to be [obj] LORD
23 Ndipo Yehova atakutulutsani ku Kadesi Barinea anati, “Pitani mukatenge dziko limene ndakupatsani.” Koma munawukira ulamuliro wa Yehova Mulungu wanu. Inu simunamukhulupirire kapena kumumvera.
and in/on/with to send: depart LORD [obj] you from Kadesh-barnea Kadesh-barnea to/for to say to ascend: rise and to possess: take [obj] [the] land: country/planet which to give: give to/for you and to rebel [obj] lip: word LORD God your and not be faithful to/for him and not to hear: obey in/on/with voice his
24 Kuyambira pamene ndinakudziwani, mwakhala owukira Yehova.
to rebel to be with LORD from day to know I [obj] you
25 Ine ndinagwa chafufumimba pamaso pa Yehova kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku chifukwa Yehova ananena kuti akuwonongani.
and to fall: fall to/for face: before LORD [obj] forty [the] day and [obj] forty [the] night which to fall: fall for to say LORD to/for to destroy [obj] you
26 Ndinapemphera kwa Ambuye ndi kuti, “Haa Yehova Wamkulukulu, musawawononge anthu anu, chuma chanuchanu chimene munachipulumutsa ndi mphamvu yanu yayikulu ku Igupto ndi dzanja lanu la mphamvu.
and to pray to(wards) LORD and to say Lord YHWH/God not to ruin people your and inheritance your which to ransom in/on/with greatness your which to come out: send from Egypt in/on/with hand: power strong
27 Kumbukirani atumiki anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Musatengere kupulupudza, kuyipa ndi kuchimwa kwawo anthuwa.
to remember to/for servant/slave your to/for Abraham to/for Isaac and to/for Jacob not to turn to(wards) stubbornness [the] people [the] this and to(wards) wickedness his and to(wards) sin his
28 Kupanda kutero, ndiye kuti anthu a ku dziko lija munatitulutsaku adzati, ‘Yehova anawatulutsa kuti akawaphe mʼchipululu popeza sanathe kukawalowetsa mʼdziko limene anawalonjeza ndipo anadana nawo.’
lest to say [the] land: country/planet which to come out: send us from there from without be able LORD to/for to come (in): bring them to(wards) [the] land: country/planet which to speak: promise to/for them and from hating his [obj] them to come out: send them to/for to die them in/on/with wilderness
29 Koma iwowa ndi anthu anu, chuma chanu chimene munachitulutsa ndi mphamvu yanu yayikulu ndi mkono wanu wotambasuka.”
and they(masc.) people your and inheritance your which to come out: send in/on/with strength your [the] great: large and in/on/with arm your [the] to stretch

< Deuteronomo 9 >