< Deuteronomo 8 >

1 Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu.
Every commandment which I command thee this day shall ye take heed to do, that ye may live, and multiply, and enter in and possess the land which Jehovah swore unto your fathers.
2 Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi.
And thou shalt remember all the way which Jehovah thy God led thee these forty years in the wilderness, to humble thee, and to prove thee, to know what was in thy heart, whether thou wouldest keep his commandments or not.
3 Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova.
And he humbled thee, and suffered thee to hunger, and fed thee with the manna, which thou hadst not known, and which thy fathers knew not; that he might make thee know that man doth not live by bread alone, but by everything that goeth out of the mouth of Jehovah doth man live.
4 Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe.
Thy clothing grew not old upon thee, neither did thy foot swell, these forty years.
5 Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.
And know in thy heart that, as a man chasteneth his son, so Jehovah thy God chasteneth thee;
6 Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye.
and thou shalt keep the commandments of Jehovah thy God, to walk in his ways, and to fear him.
7 Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri,
For Jehovah thy God bringeth thee into a good land, a land of water-brooks, of springs, and of deep waters, that gush forth in the valleys and hills;
8 dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi;
a land of wheat, and barley, and vines, and fig-trees, and pomegranates; a land of olive-trees and honey;
9 dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.
a land wherein thou shalt eat bread without scarceness, where thou shalt lack nothing; a land whose stones are iron, and out of whose mountains thou wilt dig copper.
10 Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani.
And thou shalt eat and be filled, and shalt bless Jehovah thy God for the good land which he hath given thee.
11 Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero,
Beware that thou forget not Jehovah thy God, in not keeping his commandments, and his ordinances, and his statutes, which I command thee this day;
12 kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo,
lest when thou hast eaten and art full, and hast built and inhabited fine houses,
13 ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka,
and thy herds and thy flocks multiply, and thy silver and thy gold is multiplied, and all that thou hast is multiplied,
14 mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo.
then thy heart be lifted up, and thou forget Jehovah thy God, who brought thee forth out of the land of Egypt, out of the house of bondage;
15 Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma.
who led thee through the great and terrible wilderness, [a wilderness of] fiery serpents, and scorpions, and drought, where there is no water; who brought thee forth water out of the rock of flint;
16 Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino.
who fed thee in the wilderness with manna, which thy fathers knew not, that he might humble thee, and that he might prove thee, to do thee good at thy latter end;
17 Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.”
— and thou say in thy heart, My power and the might of my hand has procured me this wealth.
18 Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.
But thou shalt remember Jehovah thy God, that it is he who giveth thee power to get wealth, that he may establish his covenant which he swore unto thy fathers, as it is this day.
19 Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu.
And it shall be, if thou do at all forget Jehovah thy God, and go after other gods, and serve them, and bow down to them, I testify against you this day that ye shall utterly perish.
20 Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.
As the nations which Jehovah is causing to perish before you, so shall ye perish; because ye would not hearken unto the voice of Jehovah your God.

< Deuteronomo 8 >