< Deuteronomo 8 >

1 Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu.
Beduru motangʼ kurito chike duto ma amiyou kawuononi, mondo omi ubed mangima kendo unyaa mi udonji e piny ma Jehova Nyasaye nosingore ni nomi kwereu.
2 Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi.
Parieuru kaka Jehova Nyasaye ma Nyasachu ne otelonu ka ukalo e piny motwo kuom higni piero angʼwen-gi duto, mondo opuonju bolruok, kopimo paro ma un-godo e chunyu ka bende unyalo rito chikene.
3 Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova.
Nodwokou piny momiyo kech okayou, eka bangʼe nomiyou manna mondo ucham ma en chiemo mane pok uneno ma kata mana kwereu bende ne pok oneno. Notimonu kamano mondo opuonjugo ni dhano ok bed mangima nikech chiemo kende to nikech wach ka wach moa e dho Jehova Nyasaye.
4 Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe.
Lepu ne ok oti kendo tiendeu ne ok opudhore kata okuot kuom higni piero angʼwen-go duto.
5 Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.
Ngʼeuru e chunyu ni kaka ngʼato kumo wuode, omiyo Jehova Nyasaye ma Nyasachu bende koro kumou.
6 Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye.
Rituru chike duto mag Jehova Nyasaye ma Nyasachu, kuwuotho e yorene bende ka umiye luor.
7 Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri,
Nimar Jehova Nyasaye ma Nyasachu kelou e piny maber, piny man-gi aore kod pi maber, man-gi thidhna mamol e holo koa e gode;
8 dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi;
ma en piny machiego ngano kod shairi, mzabibu kod ngʼowu, olemo mongʼinore, zeituni kod mor kich.
9 dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.
Pinyno nobed gi chiemo mangʼeny, bende ok unuchand gimoro; en piny ma kite mayudore gin nyinyo kendo en piny ma mula unyalo kunyo e godene.
10 Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani.
Ka usechiemo ma uyiengʼ, to pakuru Jehova Nyasaye ma Nyasachu kuom piny maber ma osemiyou.
11 Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero,
Beduru motangʼ mondo kik wiu wil kod Jehova Nyasaye ma Nyasachu, ka uweyo luwo yorene, chikene kod buchene ma amiyou kawuononi.
12 kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo,
Ka ok kamano, ka usechiemo ma uyiengʼ, ka usegero ute mabeyo ma udakie
13 ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka,
ka dhou kod jambu omedore, fedha kod dhahabu bende omedore ma gik ma un-godo duto omedore
14 mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo.
to chunyu biro donjo e sunga ma wiu nowil kod Jehova Nyasaye ma Nyasachu, mane ogolou Misri, e piny mane unie wasumbini.
15 Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma.
Ne otelonu kokalo piny malach mar ongoro piny motwo maonge kata pi, motingʼo thuonde kwiri kod thomoni, ne omiyou pi koa e lwanda matek.
16 Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino.
Ne omiyou manna ma uchamo e thim gimane kwereu ne ok ongʼeyo, mondo omi ubed ka uboloru kendo ka otemou mondo giko udhi maber.
17 Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.”
Unyalo wacho e chunyu niya, “Tekona kod lucha kod tich lweta ema omiyo ayudo mwandugi.”
18 Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.
To par Jehova Nyasaye ma Nyasachi, nimar en ema omiyi teko mar loso mwandu, kochopogo singruok mare mane osingore gi kwereu mana kaka en kawuononi.
19 Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu.
Kapo ni wiu owil gi Jehova Nyasaye ma Nyasachu ma uluwo nyiseche moko, ulamo kendo ukulorunegi, to akwongʼora kawuononi ni notieku maonge kiawa.
20 Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.
Mana kaka ogendini mane Jehova Nyasaye otieko e wangʼu kuneno, omiyo un bende ibiro tieku nikech ok uluoro Jehova Nyasaye ma Nyasachu.

< Deuteronomo 8 >