< Deuteronomo 8 >

1 Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu.
Všelikého přikázaní, kteréž já přikazuji tobě dnes, skutečně ostříhejte, abyste živi byli a rozmnožili se, a vešli k dědičnému obdržení země, kterouž s přísahou zaslíbil Hospodin otcům vašim.
2 Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi.
A rozpomínati se budeš na všecku cestu, kterouž tě vedl Hospodin Bůh tvůj již teď čtyřidceti let po poušti, aby ponížil tebe a zkusil tě, aby známé bylo, co jest v srdci tvém, budeš-li ostříhati přikázaní jeho, čili nic.
3 Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova.
I ponížil tě a dopustil na tebe hlad, potom tě krmil mannou, kteréž jsi ty neznal, ani otcové tvoji, aby známé učinil tobě, že ne samým chlebem živ bude člověk, ale vším tím, což vychází z úst Hospodinových, živ bude člověk.
4 Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe.
Roucho tvé nevetšelo na tobě, a noha tvá se neodhnetla, již od čtyřidceti let.
5 Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.
Znejž tedy v srdci svém, že jakož cvičí člověk syna svého, tak Hospodin Bůh tvůj cvičí tebe.
6 Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye.
A ostříhej přikázaní Hospodina Boha svého, chodě po cestách jeho, a boje se jeho.
7 Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri,
Nebo Hospodin Bůh tvůj uvozuje tě do země výborné, země, v níž jsou potokové vod, studnice a propasti prýštící se po údolích i po horách,
8 dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi;
Do země hojné na pšenici a ječmen, na vinice a fíky a jablka zrnatá, do země, v níž jest hojnost olivoví olej přinášejícího a medu,
9 dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.
Země, v níž bez nedostatku chléb jísti budeš, a v ničemž nouze trpěti nebudeš, země, jejíž kamení jest železo, a z hor jejích měď sekati budeš.
10 Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani.
Kdyžkoli jísti budeš a nasytíš se, dobrořečiti budeš Hospodina Boha svého za zemi výbornou, kterouž dal tobě.
11 Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero,
Aniž se kdy toho dopouštěj, abys se měl zapomenouti na Hospodina Boha svého, a neostříhati přikázaní a soudů jeho i ustanovení jeho, kteráž já dnes přikazuji tobě,
12 kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo,
Aby, když bys jedl a nasycen byl, a domů krásných nastavěje, v nich bys bydlil,
13 ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka,
A volové i ovce tvé rozmnoženy byly by, stříbra také a zlata měl bys mnoho, a hojnost ve všech věcech svých,
14 mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo.
Nepozdvihlo se srdce tvé, a zapomenul bys na Hospodina Boha svého, kterýž tě vyvedl z země Egyptské, z domu služby,
15 Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma.
A vedl tě přes poušť velikou a hroznou, na níž byli hadové ohniví a štírové, poušť žíznivou, na níž nebylo žádné vody, a vyvedl tobě vodu z přetvrdé skály,
16 Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino.
Kterýž tě krmil na poušti mannou, o kteréž nevěděli otcové tvoji, aby tě potrápil a zkusil tebe, naposledy však aby dobře učinil tobě.
17 Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.”
Aniž říkej v srdci svém: Moc má a síla ruky mé způsobila mi tato zboží,
18 Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.
Ale pamatuj na Hospodina Boha svého, nebo on dává tobě moc k dobývání zboží, aby utvrdil smlouvu svou, kterouž s přísahou učinil s otci tvými, jakož to ukazuje dnešní den.
19 Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu.
Pakli zapomena se na Hospodina Boha svého, postoupil bys po bozích cizích, a sloužil bys jim a klaněl bys se jim: osvědčuji proti vám dnes, že konečně zahynete.
20 Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.
Jako pohané, kteréž Hospodin zahladil před tváří vaší, tak zahynete, proto že jste neposlouchali hlasu Hospodina Boha svého.

< Deuteronomo 8 >