< Deuteronomo 7 >
1 Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
"TUHAN Allahmu akan membawa kamu ke negeri yang bakal kamu diami, dan banyak bangsa akan diusir-Nya dari situ. Di depan matamu Ia akan mengusir tujuh bangsa yang lebih besar dan lebih kuat dari kamu, yaitu orang-orang Het, Girgasi, Amori, Kanaan, Feris, Hewi dan Yebus.
2 Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
Apabila TUHAN Allahmu menyerahkan bangsa-bangsa itu ke dalam kuasamu dan kamu mengalahkan mereka, bunuhlah mereka semua. Jangan mengasihani mereka atau membuat perjanjian dengan mereka.
3 Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
Kamu tak boleh kawin dengan mereka, dan jangan izinkan anak-anakmu kawin dengan mereka,
4 Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
supaya mereka jangan menjauhkan anak-anakmu dari TUHAN untuk menyembah ilah-ilah lain. Kalau kamu menyembah ilah-ilah lain, TUHAN marah dan kamu akan segera dibinasakan-Nya.
5 Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
Sebab itu, robohkanlah mezbah-mezbah bangsa-bangsa itu, hancurkan tiang-tiang batu yang mereka anggap keramat, tumbangkan lambang-lambang Asyera, dan bakarlah patung-patung berhala yang mereka sembah.
6 Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
Lakukanlah semuanya itu karena kamu milik TUHAN Allahmu. Dari segala bangsa di muka bumi, kamulah yang dipilih TUHAN Allahmu untuk menjadi umat-Nya yang istimewa.
7 Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
Kamu dicintai dan dipilih TUHAN, bukan karena kamu lebih besar dari bangsa-bangsa lain; sesungguhnya kamu adalah bangsa yang paling kecil di muka bumi.
8 Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
Tetapi TUHAN memilih kamu karena Ia mengasihi kamu dan ingin menepati janji yang dibuat-Nya dengan nenek moyangmu. Itulah sebabnya Ia telah menyelamatkan kamu dengan kuasa yang besar dan membebaskan kamu dari perhambaan kepada raja Mesir.
9 Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
Ingatlah bahwa TUHAN Allahmu adalah satu-satunya Allah, dan Ia Allah yang setia. TUHAN memenuhi janji-Nya dan menunjukkan kasih-Nya yang tetap sampai seribu keturunan kepada orang yang mencintai Dia dan taat kepada perintah-perintah-Nya.
10 Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
Tetapi dengan tidak segan-segan Ia menghukum mereka yang benci kepada-Nya.
11 Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
Jadi, taatilah semua hukum yang saya sampaikan kepadamu hari ini."
12 Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
"Kalau kamu perhatikan perintah-perintah itu, dan melakukannya dengan setia, maka TUHAN Allahmu pun akan setia kepada perjanjian yang dibuat-Nya dengan kamu. Ia akan menunjukkan kasih-Nya yang tetap kepada kamu, seperti yang dijanjikan-Nya kepada leluhurmu.
13 Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
Ia akan mengasihi dan memberkati kamu, sehingga anakmu banyak dan jumlahmu bertambah-tambah. Ia akan memberkati ladang-ladangmu, sehingga menghasilkan gandum, anggur dan minyak zaitun. Ia akan memberkati kamu sehingga banyak sapi dan kambing dombamu. Semua berkat itu akan kamu terima di negeri yang diberikan TUHAN kepadamu, sesuai dengan janji-Nya kepada nenek moyangmu.
14 Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
Dari semua bangsa di dunia, tidak satu pun mendapat berkat begitu berlimpah-limpah seperti kamu. Dari kamu semua dan dari segala ternakmu tidak satu pun akan mandul.
15 Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
Kamu akan dilindungi TUHAN dari segala penyakit dan dijauhkan dari segala bencana yang kamu saksikan di Mesir, tetapi bencana-bencana itu akan ditimpakan-Nya kepada musuh-musuhmu.
16 Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
Setiap bangsa yang diserahkan TUHAN Allahmu ke dalam kuasamu harus kamu binasakan; jangan menunjukkan kasihan kepada mereka. Jangan menyembah ilah-ilah mereka, karena perbuatan itu mendatangkan celaka kepadamu.
17 Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
Barangkali kamu berpikir bangsa-bangsa itu lebih besar jumlahnya sehingga kamu tak dapat mengusir mereka.
18 Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
Tetapi jangan takut kepada mereka; ingatlah apa yang dilakukan TUHAN Allahmu terhadap raja Mesir dan seluruh rakyatnya.
19 Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
Ingatlah bencana-bencana hebat yang kamu saksikan sendiri, keajaiban-keajaiban, dan kekuatan besar yang digunakan TUHAN Allahmu untuk membebaskan kamu. Begitu pula TUHAN Allahmu akan bertindak terhadap semua bangsa yang kamu takuti.
20 Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
Bahkan TUHAN Allahmu akan menimbulkan kegemparan di antara mereka, sehingga orang-orang yang dapat melarikan diri dan bersembunyi juga akan binasa.
21 Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
Jadi janganlah takut kepada bangsa-bangsa itu. TUHAN Allahmu melindungi kamu. Ia adalah Allah yang agung dan dahsyat.
22 Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
Bangsa-bangsa itu akan diusir-Nya sedikit demi sedikit dari hadapanmu. Kamu tak boleh memusnahkan mereka dengan segera, supaya binatang-binatang buas jangan bertambah banyak dan menjadi ancaman bagimu.
23 Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
Begitulah TUHAN Allahmu akan menyerahkan musuh-musuhmu kepadamu. Ia akan mengacaubalaukan mereka sampai mereka binasa.
24 Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
Ia akan menyerahkan raja-raja mereka kepadamu. Mereka akan kamu bunuh, dan nama mereka akan dilupakan. Tak seorang pun dapat bertahan menghadapi kamu; mereka semua akan kamu musnahkan.
25 Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
Bakarlah patung-patung berhala yang mereka sembah. Jangan menginginkan perak atau emas yang melekat padanya dan jangan mengambilnya untuk dirimu sendiri. Kalau kamu melanggar perintah itu kamu akan mati, sebab TUHAN Allahmu membenci penyembahan patung berhala.
26 Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.
Jangan menempatkan sebuah patung berhala di dalam rumahmu, supaya kutuk yang menimpanya jangan menimpa kamu juga. Hal itu harus kamu benci dan pandang rendah, karena dikutuk oleh TUHAN."