< Deuteronomo 7 >

1 Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
Lorsque le Seigneur ton Dieu t’aura introduit dans la terre dans laquelle tu entres pour la posséder, et qu’il aura détruit beaucoup de nations devant toi, l’Héthéen, le Gergézéen, l’Amorrhéen, le Chananéen, le Phérézéen, l’Hévéen et le Jébuséen, sept nations beaucoup plus nombreuses que toi et beaucoup plus fortes que toi,
2 Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
Et que le Seigneur ton Dieu te les aura livrées, tu les battras jusqu’à une entière extermination. Tu ne feras point d’alliance avec elles, et tu n’auras pas pitié d’elles;
3 Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
Tu ne contracteras pas non plus de mariages avec elles. Tu ne donneras point ta fille à son fils, et tu n’accepteras pas sa fille pour ton fils,
4 Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
Parce qu’elle persuadera à ton fils de ne pas me suivre, et de servir plutôt des dieux étrangers; ainsi s’irritera la fureur du Seigneur, et il te perdra soudain.
5 Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
Mais au contraire, voici ce que vous leur ferez: Renversez leurs autels, brisez leurs statues, coupez leurs bois sacrés, et brûlez leurs images taillées au ciseau:
6 Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
Parce que tu es un peuple consacré au Seigneur ton Dieu. C’est toi qu’a choisi le Seigneur ton Dieu, afin que tu sois son peuple particulier entre tous les peuples qui sont sur la terre.
7 Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
Ce n’est pas parce que vous l’emportiez par le nombre sur toutes les nations, que le Seigneur s’est uni à vous, et vous a choisis, puisque vous êtes moins nombreux que tous les peuples;
8 Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
Mais c’est parce que le Seigneur vous a aimés et qu’il a gardé le serment qu’il a juré à vos pères; c’est pour cela qu’il vous a retirés de l’Egypte par une main puissante, et qu’il vous a délivrés de la maison de servitude, de la main de Pharaon, roi d’Egypte.
9 Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
Ainsi, tu sauras que le Seigneur ton Dieu est lui-même le Dieu fort et fidèle, gardant son alliance et sa miséricorde à ceux qui l’aiment, et à ceux qui gardent ses préceptes, jusqu’à mille générations;
10 Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
Et rendant soudain à ceux qui le haïssent, en sorte qu’il les détruit, et ne diffère pas, leur rendant sur-le-champ ce qu’ils méritent.
11 Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
Garde donc les préceptes, les cérémonies et les ordonnances que moi, je te commande aujourd’hui de pratiquer.
12 Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
Si, après avoir entendu ces ordonnances, tu les gardes et les pratiques, le Seigneur ton Dieu aussi te gardera l’alliance et la miséricorde qu’il a jurée à tes pères;
13 Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
Il t’aimera, il te multipliera, il bénira les enfants, et le fruit de ta terre, ton blé et tes vignes, ton huile et ton gros bétail, les troupeaux de tes brebis dans la terre, au sujet de laquelle il a juré à tes pères qu’il te la donnerait.
14 Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
Car tu seras béni entre tous les peuples. Il n’y aura pas chez toi de stérile de l’un et de l’autre sexe, tant dans les hommes que dans tes troupeaux.
15 Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
Le Seigneur éloignera de toi toute langueur; et les infirmités terribles de l’Egypte que tu connais, il ne te les apportera pas, à toi, mais à tous tes ennemis.
16 Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
Tu dévoreras tous les peuples que le Seigneur ton Dieu doit te donner. Ton œil ne les ménagera pas, et tu ne serviras point leurs dieux, afin qu’ils ne soient pas pour toi une ruine.
17 Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
Si tu dis en ton cœur: Ces nations sont plus nombreuses que moi; comment pourrai-je les détruire?
18 Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
Ne crains point, mais rappelle-toi ce qu’a fait le Seigneur ton Dieu à Pharaon et à tous les Egyptiens,
19 Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
Les très grandes plaies, qu’ont vues tes yeux, les signes et les prodiges, la main forte et le bras étendu, pour que le Seigneur ton Dieu te retirât de l’Egypte: ainsi fera-t-il à tous les peuples que tu redoutes.
20 Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
De plus, le Seigneur ton Dieu enverra aussi les frelons contre eux, jusqu’à ce qu’il détruise et perde entièrement tous ceux qui t’auront échappé et qui auront pu se cacher.
21 Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
Tu ne les craindras point, parce que le Seigneur ton Dieu est au milieu de toi, Dieu grand et terrible.
22 Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
Lui-même, il exterminera ces nations en ta présence, peu à peu et par parties. Tu ne pourras pas les détruire toutes à la fois, de peur que les bêtes de la terre ne se multiplient contre toi.
23 Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
Mais le Seigneur ton Dieu les mettra en ta présence, et il les fera mourir jusqu’à ce qu’ils soient entièrement détruits.
24 Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
Et il livrera leurs rois en tes mains, et tu extermineras leurs noms de dessous le ciel; nul ne pourra te résister, jusqu’à ce que tu les aies brisés.
25 Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
Tu brûleras au feu leurs images taillées au ciseau; tu ne convoiteras point l’argent et l’or dont elles ont été faites, et tu n’en prendras rien pour toi, de peur que tu ne tombes dans un piège, parce que c’est l’abomination du Seigneur ton Dieu.
26 Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.
Et tu ne porteras rien de l’idole dans ta maison, afin que tu ne deviennes pas anathème, comme elle-même l’est. Tu la détesteras comme de la fange, et tu l’auras en abomination comme de la souillure et des ordures, parce que c’est un anathème.

< Deuteronomo 7 >