< Deuteronomo 7 >
1 Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
Lorsque le Seigneur t'aura introduit en la terre où tu vas, pour qu'elle soit ton héritage, et que devant tes yeux il aura fait disparaître de grandes nations: l'Hettéen, le Gergéséen, l'Amorrhéen, le Chananéen, le Phérézéen, l'Evéen et le Jébuséen, sept nations nombreuses et plus fortes que toi,
2 Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
Et que le Seigneur ton Dieu te les aura livrées, et que tu les auras vaincues, tu les effaceras entièrement, tu ne feras pas d'alliance avec elles, tu seras pour elles sans pitié.
3 Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
Vous ne ferez point de mariages avec elles; tu ne donneras point à son fils ta fille, et tu ne prendras point sa fille pour ton fils.
4 Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
Car sa fille détournerait ton fils de moi, et il servirait d'autres dieux, et le Seigneur se courroucerait contre son peuple, et il t'exterminerait tout à coup.
5 Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
Voici comme vous les traiterez: vous enlèverez leurs autels, vous briserez leurs colonnes, vous arracherez leurs bois sacrés, vous consumerez par la flamme les images sculptées de leurs dieux.
6 Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
Car tu es un peuple saint, le peuple du Seigneur ton Dieu, et le Seigneur ton Dieu t'a choisi pour que tu sois son propre peuple, séparé de toutes les nations qui existent sur la surface de la terre.
7 Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
Le Seigneur ne vous a point préférés, il ne vous a pas choisis parce que vous êtes plus nombreux qu'aucune de ces nations; car vous êtes moindres en nombre que chacun de ces peuples.
8 Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
Mais il vous aime et il tient le serment qu'il a fait à vos pères. Voilà pourquoi le Seigneur vous a guidés d'une main puissante; il t'a fait sortir de la maison de servitude, il t'a délivré de la maison du Pharaon, roi d'Egypte.
9 Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
Tu sauras que le Seigneur ton Dieu, le seul Dieu, est un Dieu fidèle, réservant son alliance et sa miséricorde à ceux qui l'aiment et à ceux qui observent ses commandements, pendant des milliers de générations,
10 Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
Mais se vengeant dès le début de ceux qui le haïssent; ceux-là, il les extermine; il ne met point de retard avec ceux qui le haïssent, il en tirera une vengeance soudaine.
11 Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
Tu observeras les commandements, les jugements et les ordonnances que je t'intime aujourd'hui.
12 Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
Aussi longtemps que tu obéiras à ces préceptes, que tu t'appliqueras à les mettre en pratique, le Seigneur ton Dieu te conservera l'alliance et la miséricorde qu'il a promises à tes pères.
13 Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
Et il t'aimera, et il te bénira; il te multipliera, il bénira les fruits de tes entrailles, et les produits de ta terre: ton blé, ton vin, ton huile, tes grands et menus troupeaux sur la terre que le Seigneur a juré à tes pères de te donner.
14 Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
Tu seras béni au-dessus de toutes les nations; il n'y aura point parmi vous d'hommes sans enfants, ni de femme stérile; il n'y aura point non plus de stérilité parmi les troupeaux.
15 Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
Et le Seigneur ton Dieu te préservera de toute maladie, et de ces mauvaises contagions de l'Egypte que tu as vues; il ne fera tomber sur toi aucune de celles que tu y as connues, et il en frappera ceux qui te haïssent.
16 Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
Et tu mangeras ce que tu auras enlevé à ces nations; le Seigneur te le donne; ton œil ne les prendra pas en pitié, et tu ne serviras point leurs dieux, car ce serait pour toi un achoppement.
17 Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
Et si, en ta pensée, tu dis: Telle de ces nations est plus forte que moi, comment pourrai-je l'exterminer?
18 Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
Rassure-toi; rappelle à ton souvenir tout ce qu'a fait le Seigneur ton Dieu au Pharaon et aux Egyptiens,
19 Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
Les grandes épreuves que tes yeux ont vues, les signes et les grands prodiges, la main puissante et le bras très-haut; de même que le Seigneur ton Dieu t'a délivré, de même il te fera triompher de toutes les nations dont tu redoutes la face.
20 Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
Le Seigneur ton Dieu enverra contre elles des essaims de guêpes, jusqu'à ce qu'ils aient détruit celles qui t'auraient échappé et se seraient cachées devant toi.
21 Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
Tu ne seras pas blessé en face d'elles: parce que le Seigneur ton Dieu est avec toi: Dieu grand et puissant.
22 Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
Le Seigneur ton Dieu les détruira peu à peu devant toi; tu ne pourras les exterminer soudain, de peur que la contrée ne devienne un désert, et que les bêtes farouches ne se multiplient contre toi.
23 Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
Le Seigneur ton Dieu te les livrera; tu les détruiras lentement jusqu'à ce qu'enfin tu les aies exterminées.
24 Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
Et il te livrera leurs rois, et tu effaceras leur nom de ce pays; nul ne te résistera face à face, jusqu'à ce que tu les aies exterminées.
25 Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
Tu consumeras par la flamme les images sculptées de leurs dieux; tu ne convoiteras ni l'or ni l'argent qui les ornent; tu ne le prendras pas pour toi, de peur que tu n'en sois puni; car c'est une abomination pour le Seigneur ton Dieu.
26 Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.
Tu n'emporteras point d'abominations en ta demeure, car tu serais anathème comme elles; tu les détesteras, tu les auras en abomination: elles sont anathèmes.