< Deuteronomo 7 >

1 Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
When Yahweh your God brings you into the land that you go to possess, he will drive out many nations before you—the Hittites, the Girgashites, the Amorites, the Canaanites, the Perizzites, the Hivites, and the Jebusites—seven nations greater and mightier than you.
2 Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
It is Yahweh your God who gives them over to you when you defeat them, and then you must completely destroy them. You will make no covenant with them, and show them no mercy.
3 Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
Neither will you arrange any marriages with them. You will not give your daughters to their sons, and you will not take their daughters for your sons.
4 Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
For they will turn away your sons from following me, so that they may worship other gods. So the anger of Yahweh will be kindled against you, and he will destroy you quickly.
5 Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
This is how you will deal with them: You will break down their altars, dash their stone pillars in pieces, cut down their Asherah poles, and burn their cast idols.
6 Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
For you are a nation that is set apart to Yahweh your God. He has chosen you to be a people for him to possess, more than all the other peoples that are on the face of the earth.
7 Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
Yahweh did not set his love upon you or choose you because you were more in number than any people—for you were the fewest of all peoples—
8 Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
but because he loves you, and he wished to keep the oath that he had sworn to your fathers. This is why Yahweh has brought you out with a mighty hand and redeemed you out of the house of bondage, from the hand of Pharaoh, king of Egypt.
9 Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
Therefore know that Yahweh your God—he is God, the faithful God, who keeps covenants and faithfulness for a thousand generations with those who love him and keep his commandments,
10 Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
but repays those who hate him to their face, to destroy them; he will not be lenient on whoever hates him; he will repay him to his face.
11 Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
You will therefore keep the commandments, the statutes, and the decrees that I command you today, so that you will do them.
12 Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
If you listen to these decrees, and keep and do them, it will happen that Yahweh your God will keep with you the covenant and the faithfulness that he swore to your fathers.
13 Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
He will love you, bless you, and multiply you; he will also bless the fruit of your body and the fruit of your ground, your grain, your new wine, and your oil, the multiplication of your cattle and the young of your flocks, in the land that he swore to your fathers to give you.
14 Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
You will be blessed more than all other peoples; there will not be a childless male or a barren female among you or among your cattle.
15 Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
Yahweh will take away from you all sickness; none of the evil diseases of Egypt that you have known will he put on you, but he will put them on all those who hate you.
16 Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
You will consume all the peoples whom Yahweh your God will give over to you, and your eye will not pity them. You will not worship their gods, for that will be a trap for you.
17 Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
If you say in your heart, 'These nations are more numerous than I; how can I dispossess them?'—
18 Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
do not be afraid of them; you will call to mind what Yahweh your God did to Pharaoh and to all Egypt;
19 Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
the great sufferings that your eyes saw, the signs, the wonders, the mighty hand, and the outstretched arm by which Yahweh your God brought you out. Yahweh your God will do the same to all the peoples whom you fear.
20 Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
Moreover, Yahweh your God will send the hornet among them, until those who are left and who hide themselves from you perish from your presence.
21 Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
You will not be frightened at them, for Yahweh your God is among you, a great and fearsome God.
22 Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
Yahweh your God will drive out those nations before you little by little. You will not defeat them all at once, or the wild animals would become very many around you.
23 Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
But Yahweh your God will give you victory over them when you meet them in battle; he will greatly confuse them until they are destroyed.
24 Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
He will put their kings under your power, and you will make their name perish from under heaven. No one will be able to stand before you, until you have destroyed them.
25 Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
You will burn the carved figures of their gods—do not covet the silver or the gold that covers them and take it for yourself, because if you do, you will become trapped by it—for it is an abomination to Yahweh your God.
26 Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.
You will not bring any abomination into your house and start to worship it. You will utterly detest and abhor it, for it is set apart for destruction.

< Deuteronomo 7 >