< Deuteronomo 7 >

1 Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
When the Lord thy God shall bring thee into the land whither thou goest to possess it, and cast out many nations before thee, the Hittites, and the Girgashites, and the Emorites, and the Canaanites, and the Perizzites, and the Hivites, and the Jebusites, seven nations, greater in number and mightier than thou;
2 Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
And when the Lord thy God shall give them up before thee, and thou dost smite them: thou shalt utterly destroy them; thou shalt not make any covenant with them, nor show mercy unto them.
3 Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
Neither shalt thou make marriages with them; thy daughters shalt thou not give unto his son, and his daughter shalt thou not take unto thy son.
4 Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
For he would turn away thy son from following me, so that they might serve other gods; and the anger of the Lord would be kindled against you, and he would destroy thee speedily.
5 Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
But thus shall ye do unto them: their altars shall ye pull down, and their statues shall ye break, and their groves shall ye cut down, and their graven images shall ye burn with fire.
6 Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
For thou art a holy people unto the Lord thy God; of thee the Lord thy God hath made choice to be unto himself a special people, above all the nations that are upon the face of the earth.
7 Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
Not because ye are more in number than all the nations, did the Lord desire you and make choice of you; for ye are the fewest of all the nations;
8 Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
But on account of the love of the Lord for you, and because he keepeth the oath which he hath sworn unto your fathers, hath the Lord brought you out with a mighty hand, and redeemed you out of the house of bond-men, out of the hand of Pharaoh the king of Egypt.
9 Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
Know then that the Eternal thy God, is the God, the faithful God, who keepeth the covenant and the mercy with those that love him and with those that keep his commandments to the thousandth generation;
10 Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
And repayeth those that hate him to their face, to destroy them; he will not delay to him that hateth him, he will repay him to his face.
11 Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
Therefore shalt thou keep the commandment, and the statutes, and the ordinances, which I command thee this day, to do them.
12 Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
And it shall come to pass in reward for that ye will hearken to these ordinances, and keep, and do them, that the Lord thy God will keep unto thee the covenant and the kindness which he hath sworn unto thy fathers:
13 Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
And he will love thee, and bless thee, and multiply thee; and he will bless the fruit of thy womb, and the fruit of thy land, thy corn, and thy wine, and thy oil, the increase of thy cattle, and the young of thy flocks, in the land which he hath sworn unto thy fathers to give unto thee.
14 Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
Blessed shalt thou be above all the nations; there shall not be a barren male or female among thee, nor among thy cattle.
15 Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
And the Lord will take away from thee all sickness; and all the evil diseases of Egypt, which thou knowest, will he not put upon thee; but he will lay them upon all those that hate thee.
16 Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
And thou shalt consume all the nations which the Lord thy God giveth unto thee; thy eye shall not look with pity upon them: and thou shalt not serve their gods; for that would be a snare unto thee.
17 Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
If thou shouldst say in thy heart, These nations are more numerous than I: how shall I be able to dispossess them?
18 Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
Thou shalt not be afraid of them; [but] thou shalt well remember what the Lord thy God did unto Pharaoh, and unto all Egypt;
19 Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
The great proofs which thy eyes have seen, and the signs, and the wonders, and the mighty hand, and the outstretched arm, whereby the Lord thy God brought thee out: in this wise will the Lord thy God do unto all the people of whom thou art afraid.
20 Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
Moreover the hornet will the Lord thy God send out against them, until they that are left, and hide themselves from thee, be destroyed.
21 Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
Thou shalt not be affrighted at them; for the Lord thy God is in the midst of thee, a mighty and terrible God.
22 Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
And the Lord thy God will chase out these nations before thee, little by little: thou shalt not be able to make an end of them speedily, lest the beasts of the field increase upon thee.
23 Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
And the Lord thy God will give them up before thee, and he will bring among them a mighty confusion, until they be destroyed.
24 Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
And he will give their kings into thy hand, and thou shalt destroy their name from under the heavens: no man shall be able to stand up before thee, until thou have destroyed them.
25 Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
The graven images of their gods shall ye burn with fire: thou shalt not covet the silver or gold that is on them, so that thou wouldst take it unto thyself, lest thou be ensnared thereby; for it is an abomination to the Lord thy God.
26 Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.
And thou shalt not bring an abomination into thy house, lest thou become accursed like it: thou shalt utterly detest it, and thou shalt utterly abhor it; for it is accursed.

< Deuteronomo 7 >