< Deuteronomo 6 >

1 Awa ndi malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene Yehova Mulungu wanu anandilamula kuti ndikuphunzitseni kuti mukawatsatire mʼdziko limene mukuwolokera Yorodani kuti mukalitenge,
“Le yiyo imilayo, izimiso lemithetho uThixo uNkulunkulu wenu angithuma ukuthi ngilifundise ukuyigcina elizweni elizachapha uJodani lilithathe libe ngelenu,
2 kuti inuyo, ana anu, ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo mudzaope Yehova Mulungu wanu moyo wanu wonse posunga malangizo ndi malamulo ake onse amene ndinakupatsani inu kuti musangalale ndi moyo wautali.
ukuze lina, labantwabenu kanye labantwababo abezayo bamesabe uThixo uNkulunkulu wenu ekuphileni kwenu ngokugcina izimiso lemilayo engizalinika yona, ukuze libe lempilo ende.
3 Mvera Israeli ndipo usamalitse kuchita malamulowa kuti zinthu zikuyendere bwino mʼdziko ndi kuti muchuluke kwambiri mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
Zwana, wena Israyeli, njalo unanzelele ukuthi uyalalela ukuze kukulungele njalo wande kakhulu elizweni eligeleza uchago loluju, njengokuthembisa kukaThixo, uNkulunkulu wabokhokho benu.
4 Tamvani inu Aisraeli, Yehova Mulungu wathu, Yehova ndi mmodzi.
Zwana, wena Israyeli: UThixo uNkulunkulu wethu, nguThixo munye.
5 Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse.
Thanda uThixo uNkulunkulu wakho ngenhliziyo yakho yonke langomphefumulo wakho wonke kanye langamandla akho wonke.
6 Malamulo amene ndakupatsani lero ayenera kukhala mu mtima mwanu.
Imilayo le engikupha yona lamuhla kumele ibe sezinhliziyweni zenu.
7 Muziwaphunzitsa mwachangu kwa ana anu. Muzikamba za malamulowa pamene muli mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mukugona ndi pamene mukudzuka.
Igcizeleleni ebantwaneni benu. Likhulume ngayo nxa lihlezi emakhaya enu lalapho lihamba endleleni, lapho lilala lanxa livuka.
8 Muwamange ngati zizindikiro pa manja anu ndi kuwamangirira pa zipumi zanu.
Ibopheleni ezandleni zenu ibe luphawu, liyibophele lasemabunzini enu.
9 Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu.
Ibhaleni emigubazini yezindlu zenu kanye lasemasangweni enu.
10 Pamene Yehova Mulungu wanu akukulowetsani ndi kukupatsani dziko limene analumbirira makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo, dziko lokhala ndi mizinda ikuluikulu imene inu simunamange,
Kuzakuthi uThixo uNkulunkulu wenu eselingenisa elizweni afunga ngalo kuboyihlo, u-Abhrahama, u-Isaka loJakhobe, ukulinika lona, ilizwe elilamadolobho amakhulu, aphumelelayo kodwa elingazakhelanga wona,
11 nyumba zodzaza ndi zinthu za mitundu yonse zimene inu simunayikemo, zitsime zimene inu simunakumbe, minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi zimene inuyo simunadzale, tsono mukadya ndi kukhuta,
izindlu ezigcwele konke okuhle elingazange likuhluphekele, imithombo yamanzi elingazange liyigebhe, kanye lezivini lezihlahla zama-oliva elingazihlanyelanga, ukuze kuthi lingadla lisuthe,
12 samalani kuti mungayiwale Yehova amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani mu ukapolo.
linanzelele ukuthi alimkhohlwa uThixo, yena owalikhupha eGibhithe, elizweni lobugqili.
13 Muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iye yekha, ndipo muzilumbira pa dzina lake.
Mesabeni uThixo uNkulunkulu wenu, mkhonzeni yena yedwa njalo lifunge ngebizo lakhe.
14 Musamatsatire milungu ina, milungu ya anthu ena okuzungulirani,
Lingabalandeli abanye onkulunkulu babantu elakhelene labo;
15 pakuti Yehova Mulungu wanu amene ali pakati panu, ndi Mulungu wansanje ndipo adzakukwiyirani kwambiri ndi kukuwonongani, kukufafanizani mʼdziko.
ngoba uThixo uNkulunkulu wenu, ophakathi kwenu, nguThixo olobukhwele njalo ongalithukuthelela, alitshabalalise ebusweni bomhlaba.
16 Musamuyese Yehova Mulungu wanu monga munachitira ku Masa.
Lingamlingi uThixo uNkulunkulu wenu njengalokhu elakwenza eMasa.
17 Onetsetsani kuti mukusunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, malangizo ake ndi zikhazikitso zake zimene anakulamulirani.
Nanzelelani ukuthi liyayigcina imilayo kaThixo uNkulunkulu wenu lezimiso kanye lemilayo aliphe yona.
18 Chitani zoyenera ndi zabwino pamaso pa Yehova, kuti zikuyendereni bwino ndi kuti mukhoza kukalowa ndi kulanda dziko labwinolo limene Yehova analonjeza molumbira kwa makolo anu,
Yenzani okuqondileyo lokuhle emehlweni kaThixo, ukuze konke kulihambele kuhle njalo lingene liyethatha ilizwe uThixo alithembisa okhokho benu ngesifungo,
19 kupirikitsiratu adani anu onse, monga Yehova wanenera.
lidudule zonke izitha eziphambi kwenu, njengokutsho kukaThixo.
20 Mʼtsogolo muno, ana anu akadzakufunsani kuti, “Kodi tanthauzo la ndondomeko, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo amene Yehova Mulungu wathu anakulamulani nʼchiyani?”
Kuzakuthi ngokuqhubeka kwesikhathi nxa indodana yakho ikubuza isithi, ‘Zitshoni izimiso, imilayo lemithetho leyo uThixo uNkulunkulu wethu alipha yona?’
21 Inu mudzawawuze kuti, “Ife tinali akapolo a Farao ku Igupto, koma Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lamphamvu.
Wena uzakuthi: ‘Sasiyizigqili zikaFaro eGibhithe, kodwa uThixo wasikhupha eGibhithe ngesandla sakhe esilamandla.
22 Ifeyo tikuona Yehova anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, zazikulu ndi zoopsa, pa Aigupto ndi Farao pamodzi ndi banja lake lonse.
Thina sazibonela ngawethu amehlo uThixo ethumela izibonakaliso lezimangaliso ezinkulu lezesabekayo phezu kweleGibhithe laphezu kukaFaro labo bonke abendlu yakhe.
23 Koma anatitulutsa kumeneko ndi kutilowetsa kuno natipatsa dziko limene analonjeza mwa lumbiro kwa makolo athu.
Kodwa wasikhupha khonale wasiletha lapha ukuze asinike ilizwe alithembisa okhokho bethu ngesifungo.
24 Yehova anatilamula kuti tizimvera malamulo onsewa, kuti tizimuopa kuti zinthu zizitiyendera bwino pa moyo wathu monga momwe zilili leromu.
UThixo wasilaya ukuba silalele zonke lezi zimiso lokwesaba uThixo uNkulunkulu wethu, ukuze sithole ukuphumelela lokuphila, njengoba kunje lamhlanje.
25 Ndipo ngati tisamala kumvera malamulo onsewa pamaso pa Yehova Mulungu wathu monga momwe anatilamulira ife, chimenecho chidzakhala chilungamo chathu.”
Kanti-ke nxa sinanzelela silalela wonke umthetho lo phambi kukaThixo uNkulunkulu wethu, njengokusilaya kwakhe, lokhu kuzakuba yikulunga kwethu.’”

< Deuteronomo 6 >