< Deuteronomo 6 >

1 Awa ndi malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene Yehova Mulungu wanu anandilamula kuti ndikuphunzitseni kuti mukawatsatire mʼdziko limene mukuwolokera Yorodani kuti mukalitenge,
(And this *L(P)*) [is] the commandment the statutes and the judgments which he has commanded Yahweh God your to teach you to observe in the land where you [are] about to pass over there towards to take possession of it.
2 kuti inuyo, ana anu, ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo mudzaope Yehova Mulungu wanu moyo wanu wonse posunga malangizo ndi malamulo ake onse amene ndinakupatsani inu kuti musangalale ndi moyo wautali.
So that you may fear Yahweh God your to keep all statutes his and commandments his which I [am] commanding you you and child your and [the] child of child your all [the] days of life your and so that they may grow long! days your.
3 Mvera Israeli ndipo usamalitse kuchita malamulowa kuti zinthu zikuyendere bwino mʼdziko ndi kuti muchuluke kwambiri mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
And you will hear O Israel and you will take care to observe [them] that it will go well for you and that you will increase! exceedingly just as he spoke Yahweh [the] God of ancestors your to you a land flowing of milk and honey.
4 Tamvani inu Aisraeli, Yehova Mulungu wathu, Yehova ndi mmodzi.
Hear O Israel Yahweh God our Yahweh - [is] one.
5 Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse.
And you will love Yahweh God your with all heart your and with all being your and with all strength your.
6 Malamulo amene ndakupatsani lero ayenera kukhala mu mtima mwanu.
And they will be the words these which I [am] commanding you this day on heart your.
7 Muziwaphunzitsa mwachangu kwa ana anu. Muzikamba za malamulowa pamene muli mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mukugona ndi pamene mukudzuka.
And you will repeat them to children your and you will speak in them when sitting you in house your and when walking you on the road and when lying down you and when rising up you.
8 Muwamange ngati zizindikiro pa manja anu ndi kuwamangirira pa zipumi zanu.
And you will tie them for a sign on hand your and they will be for marks between eyes your.
9 Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu.
And you will write them on [the] doorposts of house your and on gates your.
10 Pamene Yehova Mulungu wanu akukulowetsani ndi kukupatsani dziko limene analumbirira makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo, dziko lokhala ndi mizinda ikuluikulu imene inu simunamange,
And it will be that he will bring you - Yahweh God your into the land which he swore to ancestors your to Abraham to Isaac and to Jacob to give to you cities large and good which not you built.
11 nyumba zodzaza ndi zinthu za mitundu yonse zimene inu simunayikemo, zitsime zimene inu simunakumbe, minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi zimene inuyo simunadzale, tsono mukadya ndi kukhuta,
And houses full every good thing which not you filled and wells dug out which not you dug vineyards and olive trees which not you planted and you will eat and you will be satisfied.
12 samalani kuti mungayiwale Yehova amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani mu ukapolo.
Take heed to yourself lest you should forget Yahweh who he brought out you from [the] land of Egypt from a house of slaves.
13 Muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iye yekha, ndipo muzilumbira pa dzina lake.
Yahweh God your you will fear and him you will serve and in name his you will swear oaths.
14 Musamatsatire milungu ina, milungu ya anthu ena okuzungulirani,
Not you will walk! after gods other any of [the] gods of the peoples which [are] around you.
15 pakuti Yehova Mulungu wanu amene ali pakati panu, ndi Mulungu wansanje ndipo adzakukwiyirani kwambiri ndi kukuwonongani, kukufafanizani mʼdziko.
For [is] a God jealous Yahweh God your in midst your lest it should burn [the] anger of Yahweh God your on you and he will destroy you from on [the] surface of the ground.
16 Musamuyese Yehova Mulungu wanu monga munachitira ku Masa.
Not you will put to [the] test Yahweh God your just as you put [him] to [the] test at Massah.
17 Onetsetsani kuti mukusunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, malangizo ake ndi zikhazikitso zake zimene anakulamulirani.
Certainly you will keep! [the] commandments of Yahweh God your and testimonies his and statutes his which he has commanded you.
18 Chitani zoyenera ndi zabwino pamaso pa Yehova, kuti zikuyendereni bwino ndi kuti mukhoza kukalowa ndi kulanda dziko labwinolo limene Yehova analonjeza molumbira kwa makolo anu,
And you will do the right and the good in [the] eyes of Yahweh so that it may go well for you and you will go and you will take possession of the land good which he swore Yahweh to ancestors your.
19 kupirikitsiratu adani anu onse, monga Yehova wanenera.
To drive out all enemies your from before you just as he has spoken Yahweh.
20 Mʼtsogolo muno, ana anu akadzakufunsani kuti, “Kodi tanthauzo la ndondomeko, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo amene Yehova Mulungu wathu anakulamulani nʼchiyani?”
If he will ask you child your tomorrow saying what? [are] the testimonies and the statutes and the judgments which he commanded Yahweh God our you.
21 Inu mudzawawuze kuti, “Ife tinali akapolo a Farao ku Igupto, koma Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lamphamvu.
And you will say to child your slaves we were of Pharaoh in Egypt and he brought out us Yahweh from Egypt by a hand strong.
22 Ifeyo tikuona Yehova anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, zazikulu ndi zoopsa, pa Aigupto ndi Farao pamodzi ndi banja lake lonse.
And he gave Yahweh signs and wonders great and bad - on Egypt on Pharaoh and on all household his to eyes our.
23 Koma anatitulutsa kumeneko ndi kutilowetsa kuno natipatsa dziko limene analonjeza mwa lumbiro kwa makolo athu.
And us he brought out from there so as to bring us to give to us the land which he swore to ancestors our.
24 Yehova anatilamula kuti tizimvera malamulo onsewa, kuti tizimuopa kuti zinthu zizitiyendera bwino pa moyo wathu monga momwe zilili leromu.
And he commanded us Yahweh to observe all the statutes these to fear Yahweh God our for good of us all the days to preserve alive us as the day this.
25 Ndipo ngati tisamala kumvera malamulo onsewa pamaso pa Yehova Mulungu wathu monga momwe anatilamulira ife, chimenecho chidzakhala chilungamo chathu.”
And righteousness it will belong to us that we will take care to observe all the commandment this before Yahweh God our just as he commanded us.

< Deuteronomo 6 >