< Deuteronomo 6 >

1 Awa ndi malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene Yehova Mulungu wanu anandilamula kuti ndikuphunzitseni kuti mukawatsatire mʼdziko limene mukuwolokera Yorodani kuti mukalitenge,
Dette er Budet, Anordningerne og Lovbudene, som HERREN eders Gud har paabudt at lære eder at handle efter i det Land, I skal over og tage i Besiddelse,
2 kuti inuyo, ana anu, ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo mudzaope Yehova Mulungu wanu moyo wanu wonse posunga malangizo ndi malamulo ake onse amene ndinakupatsani inu kuti musangalale ndi moyo wautali.
for at du alle dine Levedage maa frygte HERREN din Gud og holde alle hans Anordninger og Bud, som jeg giver dig, du selv, din Søn og din Sønnesøn, og faa et langt Liv.
3 Mvera Israeli ndipo usamalitse kuchita malamulowa kuti zinthu zikuyendere bwino mʼdziko ndi kuti muchuluke kwambiri mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
Hør derfor, Israel, og gør omhyggeligt efter dem, for at det kan gaa dig vel, og for at I maa blive overvættes talrige, saaledes som HERREN, dine Fædres Gud, har forjættet dig, i et Land, der flyder med Mælk og Honning.
4 Tamvani inu Aisraeli, Yehova Mulungu wathu, Yehova ndi mmodzi.
Hør, Israel! HERREN vor Gud, HERREN er een.
5 Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse.
Og du skal elske HERREN din Gud af hele dit Hjerte, af hele din Sjæl og af hele din Styrke.
6 Malamulo amene ndakupatsani lero ayenera kukhala mu mtima mwanu.
Disse Bud, som jeg paalægger dig i Dag, skal du tage dig til Hjerte;
7 Muziwaphunzitsa mwachangu kwa ana anu. Muzikamba za malamulowa pamene muli mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mukugona ndi pamene mukudzuka.
og du skal indprente dine Børn dem og tale om dem, baade naar du sidder i dit Hus, og naar du vandrer paa Vejen, baade naar du lægger dig, og naar du staar op;
8 Muwamange ngati zizindikiro pa manja anu ndi kuwamangirira pa zipumi zanu.
du skal binde dem som et Tegn om din Haand, de skal være som et Erindringsmærke paa din Pande,
9 Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu.
og du skal skrive dem paa Dørstolperne af dit Hus og paa dine Porte.
10 Pamene Yehova Mulungu wanu akukulowetsani ndi kukupatsani dziko limene analumbirira makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo, dziko lokhala ndi mizinda ikuluikulu imene inu simunamange,
Og naar HERREN din Gud fører dig ind i det Land, han tilsvor dine Fædre Abraham, Isak og Jakob at ville give dig, store og smukke Byer, som du ikke har bygget,
11 nyumba zodzaza ndi zinthu za mitundu yonse zimene inu simunayikemo, zitsime zimene inu simunakumbe, minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi zimene inuyo simunadzale, tsono mukadya ndi kukhuta,
Huse, der er fulde af alt godt, som du ikke har samlet, udhuggede Cisterner, som du ikke har udhugget, Vingaarde og Olivenhaver, som du ikke har plantet, og du spiser dig mæt,
12 samalani kuti mungayiwale Yehova amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani mu ukapolo.
vogt dig da for at glemme HERREN, som førte dig ud af Ægypten, af Trællehuset;
13 Muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iye yekha, ndipo muzilumbira pa dzina lake.
HERREN din Gud skal du frygte, ham skal du dyrke, og ved hans Navn skal du sværge!
14 Musamatsatire milungu ina, milungu ya anthu ena okuzungulirani,
I maa ikke holde eder til andre Guder, til nogen af de omboende Folks Guder,
15 pakuti Yehova Mulungu wanu amene ali pakati panu, ndi Mulungu wansanje ndipo adzakukwiyirani kwambiri ndi kukuwonongani, kukufafanizani mʼdziko.
thi HERREN din Gud er en nidkær Gud i din Midte; ellers vil HERREN din Guds Vrede blusse op imod dig, saa han udrydder dig af Jorden.
16 Musamuyese Yehova Mulungu wanu monga munachitira ku Masa.
I maa ikke friste HERREN eders Gud, som I gjorde ved Massa.
17 Onetsetsani kuti mukusunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, malangizo ake ndi zikhazikitso zake zimene anakulamulirani.
I skal omhyggeligt holde HERREN eders Guds Bud, Vidnesbyrd og Anordninger, som han har paalagt dig;
18 Chitani zoyenera ndi zabwino pamaso pa Yehova, kuti zikuyendereni bwino ndi kuti mukhoza kukalowa ndi kulanda dziko labwinolo limene Yehova analonjeza molumbira kwa makolo anu,
og du skal gøre, hvad der er ret og godt i HERRENS Øjne, for at det maa gaa dig vel, og du maa komme ind og faa det herlige Land i Eje, som HERREN tilsvor dine Fædre,
19 kupirikitsiratu adani anu onse, monga Yehova wanenera.
idet han jager alle dine Fjender bort foran dig, som HERREN har sagt!
20 Mʼtsogolo muno, ana anu akadzakufunsani kuti, “Kodi tanthauzo la ndondomeko, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo amene Yehova Mulungu wathu anakulamulani nʼchiyani?”
Naar din Søn i Fremtiden spørger dig: »Hvorledes har det sig med de Vidnesbyrd, Anordninger og Lovbud, som HERREN vor Gud gav eder?«
21 Inu mudzawawuze kuti, “Ife tinali akapolo a Farao ku Igupto, koma Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lamphamvu.
saa skal du svare din Søn saaledes: »Vi var engang Faraos Trælle i Ægypten; men HERREN førte os ud af Ægypten med stærk Haand.
22 Ifeyo tikuona Yehova anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, zazikulu ndi zoopsa, pa Aigupto ndi Farao pamodzi ndi banja lake lonse.
Og HERREN udførte Tegn og store, ødelæggende Undere paa Ægypten, paa Farao og hele hans Hus, lige for vore Øjne;
23 Koma anatitulutsa kumeneko ndi kutilowetsa kuno natipatsa dziko limene analonjeza mwa lumbiro kwa makolo athu.
men os førte han ud derfra for at føre os ind og give os det Land, han havde tilsvoret vore Fædre.
24 Yehova anatilamula kuti tizimvera malamulo onsewa, kuti tizimuopa kuti zinthu zizitiyendera bwino pa moyo wathu monga momwe zilili leromu.
Dengang paalagde HERREN os at handle efter alle disse Anordninger, idet vi frygter HERREN vor Gud, for at det altid maa gaa os vel, for at han kan lade os blive i Live, som det hidtil er sket.
25 Ndipo ngati tisamala kumvera malamulo onsewa pamaso pa Yehova Mulungu wathu monga momwe anatilamulira ife, chimenecho chidzakhala chilungamo chathu.”
Og vi skal staa som retfærdige for HERREN vor Guds Ansigt, naar vi handler efter alle disse Anordninger, saaledes som han har paalagt os!«

< Deuteronomo 6 >