< Deuteronomo 6 >

1 Awa ndi malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene Yehova Mulungu wanu anandilamula kuti ndikuphunzitseni kuti mukawatsatire mʼdziko limene mukuwolokera Yorodani kuti mukalitenge,
Toto pak jest přikázaní, ustanovení a soudové, kteréž přikázal Hospodin Bůh váš, abych učil vás, abyste činili je v zemi, do kteréž jdete k dědičnému držení jí,
2 kuti inuyo, ana anu, ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo mudzaope Yehova Mulungu wanu moyo wanu wonse posunga malangizo ndi malamulo ake onse amene ndinakupatsani inu kuti musangalale ndi moyo wautali.
Abys se bál Hospodina Boha svého, ostříhaje všech ustanovení jeho a přikázaní jeho, kteráž já přikazuji tobě, ty i syn tvůj i vnuk tvůj, po všecky dny života svého, aby se prodlili dnové tvoji.
3 Mvera Israeli ndipo usamalitse kuchita malamulowa kuti zinthu zikuyendere bwino mʼdziko ndi kuti muchuluke kwambiri mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
Slyšiž tedy, Izraeli, a hleď tak skutečně činiti, aby tobě dobře bylo, a abyste se velmi rozmnožili, (jakož mluvil Hospodin Bůh otců tvých tobě, ) v zemi oplývající mlékem a strdí.
4 Tamvani inu Aisraeli, Yehova Mulungu wathu, Yehova ndi mmodzi.
Slyš, Izraeli, Hospodin Bůh náš, Hospodin jeden jest.
5 Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse.
Protož milovati budeš Hospodina Boha svého z celého srdce svého, a ze vší duše své, a ze vší síly své.
6 Malamulo amene ndakupatsani lero ayenera kukhala mu mtima mwanu.
A budou slova tato, kteráž já přikazuji tobě dnes, v srdci tvém.
7 Muziwaphunzitsa mwachangu kwa ana anu. Muzikamba za malamulowa pamene muli mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mukugona ndi pamene mukudzuka.
A budeš je často opětovati synům svým, a mluviti o nich, když sedneš v domě svém, když půjdeš cestou, a léhaje i vstávaje.
8 Muwamange ngati zizindikiro pa manja anu ndi kuwamangirira pa zipumi zanu.
Uvážeš je za znamení na ruce své, a jako náčelník mezi očima svýma.
9 Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu.
Napíšeš je také na veřejích domu svého a na branách svých.
10 Pamene Yehova Mulungu wanu akukulowetsani ndi kukupatsani dziko limene analumbirira makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo, dziko lokhala ndi mizinda ikuluikulu imene inu simunamange,
A když tě uvede Hospodin Bůh tvůj do země, kterouž s přísahou zaslíbil otcům tvým, Abrahamovi, Izákovi a Jákobovi, že ji tobě dá, i města veliká a výborná, kterýchžs nestavěl,
11 nyumba zodzaza ndi zinthu za mitundu yonse zimene inu simunayikemo, zitsime zimene inu simunakumbe, minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi zimene inuyo simunadzale, tsono mukadya ndi kukhuta,
A domy plné všech dobrých věcí, kterýchž jsi nenaplnil, a studnice vykopané, kterýchž jsi nekopal, a vinice i olivoví, jichž jsi neštípil, a jedl bys a nasytil se:
12 samalani kuti mungayiwale Yehova amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani mu ukapolo.
Varuj se, abys nezapomenul na Hospodina, kterýž tě vyvedl z země Egyptské, z poroby těžké.
13 Muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iye yekha, ndipo muzilumbira pa dzina lake.
Hospodina Boha svého báti se budeš, a jemu sloužiti, a ve jméno jeho přisahati.
14 Musamatsatire milungu ina, milungu ya anthu ena okuzungulirani,
Neodejdeš po bozích cizích, z bohů jiných národů, kteříž vůkol vás jsou,
15 pakuti Yehova Mulungu wanu amene ali pakati panu, ndi Mulungu wansanje ndipo adzakukwiyirani kwambiri ndi kukuwonongani, kukufafanizani mʼdziko.
(Nebo Bůh silný, horlivý, Hospodin tvůj u prostřed tebe jest, ) aby se neroznítila prchlivost Hospodina Boha tvého na tebe, a shladil by tě se svrchku země.
16 Musamuyese Yehova Mulungu wanu monga munachitira ku Masa.
Nebudete pokoušeti Hospodina Boha svého, jako jste pokoušeli v Massah.
17 Onetsetsani kuti mukusunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, malangizo ake ndi zikhazikitso zake zimene anakulamulirani.
Pilně ostříhejte přikázaní Hospodina Boha svého, a svědectví jeho, i ustanovení jeho, kteráž přikázal tobě,
18 Chitani zoyenera ndi zabwino pamaso pa Yehova, kuti zikuyendereni bwino ndi kuti mukhoza kukalowa ndi kulanda dziko labwinolo limene Yehova analonjeza molumbira kwa makolo anu,
A čiň to, což pravého a dobrého jest před očima Hospodinovýma, aby tobě dobře bylo, a vejda, abys dědičně obdržel zemi výbornou, kterouž s přísahou zaslíbil Hospodin otcům tvým,
19 kupirikitsiratu adani anu onse, monga Yehova wanenera.
Aby vypudil všecky nepřátely tvé od tváři tvé, jakož mluvil Hospodin.
20 Mʼtsogolo muno, ana anu akadzakufunsani kuti, “Kodi tanthauzo la ndondomeko, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo amene Yehova Mulungu wathu anakulamulani nʼchiyani?”
Když by se potom syn tvůj otázal tebe, řka: Co jsou to za svědectví a ustanovení i soudy, kteréž přikázal Hospodin Bůh náš vám?
21 Inu mudzawawuze kuti, “Ife tinali akapolo a Farao ku Igupto, koma Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lamphamvu.
Tedy díš synu svému: Služebníci jsme byli Faraonovi v Egyptě, i vyvedl nás Hospodin z Egypta v ruce silné.
22 Ifeyo tikuona Yehova anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, zazikulu ndi zoopsa, pa Aigupto ndi Farao pamodzi ndi banja lake lonse.
A činil Hospodin znamení a zázraky veliké a škodlivé v Egyptě proti Faraonovi, a proti všemu domu jeho před očima našima,
23 Koma anatitulutsa kumeneko ndi kutilowetsa kuno natipatsa dziko limene analonjeza mwa lumbiro kwa makolo athu.
Nás pak vyvedl odtud, aby uvedl nás, a dal nám zemi, kterouž s přísahou zaslíbil otcům našim.
24 Yehova anatilamula kuti tizimvera malamulo onsewa, kuti tizimuopa kuti zinthu zizitiyendera bwino pa moyo wathu monga momwe zilili leromu.
Protož přikázal nám Hospodin, abychom ostříhali všech ustanovení těchto, bojíce se Hospodina Boha svého, aby nám dobře bylo po všecky dny, a aby zachoval nás při životu, jakž to činí i v dnešní den.
25 Ndipo ngati tisamala kumvera malamulo onsewa pamaso pa Yehova Mulungu wathu monga momwe anatilamulira ife, chimenecho chidzakhala chilungamo chathu.”
A spravedlnost míti budeme, když ostříhati budeme a činiti všecka přikázaní tato před Hospodinem Bohem svým, jakož přikázal nám.

< Deuteronomo 6 >