< Deuteronomo 5 >

1 Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati: Tamverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuwuzeni lero. Muwaphunzire ndi kuonetsetsa kuti mukuwatsata.
UMozisi wasebiza uIsrayeli wonke, wathi kubo: Zwana, Israyeli, izimiso lezahlulelo engizikhuluma endlebeni zenu lamuhla, ukuze lizifunde, linanzelele ukuzenza.
2 Yehova Mulungu wathu anachita pangano ndi ife ku Horebu.
INkosi uNkulunkulu wethu yenza isivumelwano lathi eHorebe.
3 Yehova sanachite pangano ndi makolo athu koma ndi ife, tonse amene tili moyo lero.
INkosi kayisenzanga lesisivumelwano labobaba, kodwa lathi, thina sonke esilapha siphila lamuhla.
4 Yehova anayankhula nanu maso ndi maso kuchokera mʼmoto pa phiri paja.
INkosi yakhuluma lani ubuso lobuso entabeni, iphakathi komlilo,
5 (Pa nthawi imeneyo ine ndinayimirira pakati pa Yehova ndi inu kuti ndikuwuzeni mawu a Yehova, chifukwa inu munkachita mantha ndi moto ndipo simunakwere ku phiri). Ndipo Iye anati:
(ngema phakathi kweNkosi lani ngalesosikhathi, ukulazisa ilizwi leNkosi; ngoba lesaba ngenxa yomlilo, kalenyukelanga entabeni) isithi:
6 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
NgiyiNkosi uNkulunkulu wakho, eyakukhupha elizweni leGibhithe, endlini yobugqili.
7 “Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.
Ungabi labanye onkulunkulu phambi kwami.
8 “Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
Ungazenzeli isithombe esibaziweyo, loba yiwuphi umfanekiso wokusemazulwini phezulu loba wokusemhlabeni phansi, loba wokusemanzini ngaphansi komhlaba.
9 Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane,
Ungakukhothameli, ungakukhonzi; ngoba mina iNkosi, uNkulunkulu wakho, nginguNkulunkulu olobukhwele, ngiphindisela ububi baboyise phezu kwabantwana, kuze kube sesizukulwaneni sesithathu lesesine sabangizondayo,
10 koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda ndi kusunga malamulo anga.
njalo ngibenzela umusa abayizinkulungwane zabangithandayo lezabagcina imilayo yami.
11 “Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
Ungaliphathi ngeze ibizo leNkosi uNkulunkulu wakho; ngoba iNkosi kayiyikumyekela engelacala ophatha ibizo layo ngeze.
12 “Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika monga momwe Yehova Mulungu wako anakulamulira.
Gcina usuku lwesabatha, ukulungcwelisa, njengokukulaya kweNkosi uNkulunkulu wakho.
13 Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi,
Insuku eziyisithupha uzasebenza, uwenze wonke umsebenzi wakho;
14 koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi kapena wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu kapena ngʼombe yanu kapena bulu wanu kapena ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu, motero ndiye kuti wantchito wanu wamwamuna ndi wantchito wanu wamkazi adzapumula monga inuyo.
kodwa usuku lwesikhombisa lulisabatha leNkosi uNkulunkulu wakho; ungenzi loba yiwuphi umsebenzi ngalo, wena lendodana yakho lendodakazi yakho lenceku yakho lencekukazi yakho lenkabi yakho lobabhemi wakho loba yisiphi sezifuyo zakho, lowemzini wakho ophakathi kwamasango akho, ukuze iphumule inceku yakho lencekukazi yakho, njengawe.
15 Kumbukira kuti unali kapolo ku Igupto ndipo Yehova Mulungu wako anakutulutsa kumeneko ndi dzanja lamphamvu ndi lotambasuka. Choncho Yehova Mulungu wako akukulamula kuti uzisunga tsiku la Sabata.
Njalo ukhumbule ukuthi wawuyinceku elizweni leGibhithe, lokuthi iNkosi uNkulunkulu wakho yakukhupha khona ngesandla esilamandla langengalo eyeluliweyo. Ngakho iNkosi uNkulunkulu wakho yakulaya ukuthi ugcine usuku lwesabatha.
16 “Lemekeza abambo ako ndi amayi ako monga Yehova Mulungu wako wakulamulira iwe kuti ukhale ndi moyo wautali ndi kuti zikuyendere bwino mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
Hlonipha uyihlo lonyoko, njengokukulaya kweNkosi uNkulunkulu wakho, ukuze insuku zakho zelulwe, lokuthi kukulungele elizweni iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona.
17 “Usaphe.
Ungabulali.
18 “Usachite chigololo.
Njalo ungafebi.
19 “Usabe.
Njalo ungebi.
20 “Usapereke umboni womunamizira mnzako.
Njalo unganiki ubufakazi bamanga ngomakhelwane wakho.
21 “Usasirire mkazi wa mnzako. Usasirire nyumba ya mnzako kapena munda wake, wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
Njalo ungafisi umkamakhelwane wakho; ungahawukeli indlu kamakhelwane wakho, insimu yakhe, lenceku yakhe, lencekukazi yakhe, inkabi yakhe, lobabhemi wakhe, njalo loba yini ekamakhelwane wakho.
22 Awa ndi malamulo amene Yehova anayankhula ndi mawu okweza kwa gulu lanu lonse pa phiri paja mʼmoto, mtambo ndi mdima woopsa, sanawonjezerepo kanthu. Ndipo anawalemba pa mapale awiri amiyala ndi kundipatsa.
Amazwi la iNkosi yawakhuluma ebandleni lenu lonke entabeni, iphakathi komlilo, eyezini, lemnyameni onzima, ngelizwi elikhulu; njalo kayengezelelanga. Yawabhala ezibhebheni ezimbili zamatshe, yanginika zona.
23 Mutamva mawu kuchokera mu mdimawo, phiri lili moto lawilawi, atsogoleri onse a mafuko anu ndi akuluakulu anu anabwera kwa ine.
Kwasekusithi lilizwa ilizwi livela phakathi komnyama, lentaba ivutha umlilo, lasondela kimi, zonke inhloko zezizwe zenu, labadala benu,
24 Ndipo munati, “Yehova Mulungu wathu wationetsa ulemerero ndi ukulu wake, ndipo tamva mawu ake kuchokera mʼmoto. Lero taona kuti munthu akhoza kukhala ndi moyo ngakhale Mulungu atayankhula naye.
lathi: Khangela, iNkosi uNkulunkulu wethu isitshengisile inkazimulo yayo lobukhulu bayo, lelizwi layo silizwile livela phakathi komlilo; lamuhla sibonile ukuthi uNkulunkulu uyakhuluma lomuntu aphile.
25 Koma tsopano tife chifukwa chiyani? Moto waukuluwu utinyeketsa, ndipo tifa tikapitirirabe kumva mawu a Yehova Mulungu wathu.
Ngakho-ke sizafelani? Ngoba lumlilo omkhulu uzasiqothula. Uba siphinda silizwa ilizwi leNkosi uNkulunkulu wethu futhi, sizakufa-ke.
26 Pakuti ndi munthu uti wolengedwa amene anamvapo mawu a Mulungu wamoyo akuyankhula kuchokera mʼmoto, monga tachitiramu, nakhala ndi moyo?
Ngoba ngubani enyameni yonke owezwa ilizwi likaNkulunkulu ophilayo likhuluma livela phakathi komlilo, njengathi, waphila?
27 Pita pafupi kuti ukamvetsere zonse zimene Yehova Mulungu wathu akunena. Kenaka udzatiwuze chilichonse chimene Yehova Mulungu wathu akunena ndipo tidzamvera ndi kuchita.”
Sondela wena, uzwe konke iNkosi uNkulunkulu wethu ezakutsho, usitshele wena konke iNkosi uNkulunkulu wethu ezakutsho kuwe, sizakuzwa, sikwenze.
28 Yehova anakumvani pamene munkayankhula kwa ine ndipo Yehova anati kwa ine, “Ndamva zimene anthuwa anena kwa iwe. Chilichonse chimene anena ndi chabwino.
INkosi yasisizwa ilizwi lamazwi enu ekukhulumeni kwenu kimi; iNkosi yasisithi kimi: Ngizwile ilizwi lamazwi alababantu abawakhulume kuwe; kulungile konke abakukhulumileyo.
29 Zikanakhala bwino akanakhala ndi mtima wondiopa ndi kusunga malamulo anga nthawi zonse kuti zinthu ziziwayendera bwino, iwowo pamodzi ndi ana awo kwamuyaya.
O kungathi bangaba lenhliziyo enjalo yokungesaba, bagcine yonke imilayo yami, insuku zonke, ukuze kubalungele labantwana babo kuze kube nininini!
30 “Pita uwawuze kuti abwerere ku matenti awo.
Hamba uthi kibo: Zibuyeleleni emathenteni enu.
31 Koma iwe ukhale kuno ndi ine kuti ndikupatse malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene azitsatira mʼdziko limene ndiwapatse kuti alitenge.”
Kodwa wena, mana lapha phansi kwami, ke ngikhulume kuwe yonke imilayo lezimiso lezahlulelo ozabafundisa zona, ukuze bazenze elizweni engibanika lona ukuthi badle ilifa lalo.
32 Choncho samalirani kuchita zimene Yehova Mulungu wanu akukulamulirani inu, musapatukire kudzanja lamanja kapena lamanzere.
Ngakho qaphelani ukuthi lenze njengokulilaya kweNkosi uNkulunkulu wenu; lingaphambukeli ngakwesokunene langakwesokhohlo.
33 Muyende mʼnjira yonse imene Yehova Mulungu wanu wakulamulirani kuti mukhale ndi moyo ndi kupambana, ndi kuti masiku anu achuluke mʼdziko limene mudzatengelo.
Lizahamba endleleni yonke iNkosi uNkulunkulu wenu elilaye yona, ukuze liphile, njalo kulilungele, libe seliselula izinsuku elizweni elizakudla ilifa lalo.

< Deuteronomo 5 >