< Deuteronomo 4 >

1 Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
А сада, Израиљу, чуј уредбе моје и законе, које вас учим да творите, да бисте поживели и ушли у земљу коју вам даје Господ Бог отаца ваших и да бисте је наследили.
2 Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
Ништа не додајте к речи коју вам ја заповедам, нити одузмите од ње, да бисте сачували заповести Господа Бога свог које вам ја заповедам.
3 Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
Очи су ваше виделе шта учини Господ с Велфегора; јер сваког човека који пође за Велфегором истреби Господ Бог твој између тебе.
4 Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
А ви који се држасте Господа Бога свог, ви сте сви живи данас.
5 Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
Гле, учио сам вас уредбама и законима, као што ми заповеди Господ Бог мој, да бисте тако творили у земљи коју идете да је наследите.
6 Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
Држите дакле и извршујте их, јер је то мудрост ваша и разум ваш пред народима, који ће кад чују све ове уредбе рећи: Само је овај велики народ мудар и разуман.
7 Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
Јер који је велики народ коме је Господ близу као што је Господ Бог наш кад Га год зазовемо?
8 Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
И који је народ велики који има уредбе и законе праведне као што је сав овај закон који износим данас пред вас?
9 Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
Само пази на се и добро чувај душу своју, да не заборавиш оне ствари које су виделе очи твоје, и да не изиђу из срца твог докле си год жив; него да их обзнаниш синовима својим и синовима синова својих.
10 Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
Онај дан кад стајасте пред Господом Богом својим код Хорива, кад ми Господ рече: Сабери ми народ да им кажем речи своје, којима ће се научити да ме се боје док су живи на земљи, и да уче томе и синове своје;
11 Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
Кад приступисте и стајасте под гором, а гора огњем гораше до самог неба и беше на њој тама и облак и мрак;
12 Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
И проговори Господ к вама исред огња; глас од речи чусте, али осим гласа лик не видесте;
13 Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
И објави вам завет свој, који вам заповеди да држите, десет речи, које написа на две плоче камене.
14 Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
И мени заповеди онда Господ да вас учим уредбама и законима да их творите у земљи у коју идете да је наследите.
15 Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
Зато чувајте добро душе своје; јер не видесте никакав лик у онај дан кад вам говори Господ на Хориву исред огња,
16 kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
Да се не бисте покварили и начинили себи лик резан или какву год слику од човека или од жене,
17 kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
Слику од каквог живинчета које је на земљи, или слику од какве птице крилате која лети испод неба;
18 Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
Слику од чега што пуже по земљи, или слику од какве рибе која је у води под земљом;
19 Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
И да не би подигавши очи своје к небу и видевши сунце и месец и звезде, сву војску небеску, преварио се и клањао им се и служио им; јер их Господ Бог твој даде свим народима под целим небом;
20 Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
А вас узе Господ и изведе вас из пећи гвоздене, из Мисира, да му будете народ наследни, као што се види данас.
21 Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
Али се Господ разгневи на ме за ваше речи, и закле се да нећу прећи преко Јордана ни ући у добру земљу, коју ти Господ Бог твој даје у наследство.
22 Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
И ја ћу умрети у овој земљи и нећу прећи преко Јордана; а ви ћете прећи и наследити ону добру земљу.
23 Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
Пазите да не заборавите завет Господа Бога свог, који учини с вама, и да не градите себи лик резани, слику од које год твари, као што ти је забранио Господ Бог твој.
24 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
Јер је Господ Бог твој огањ који спаљује и Бог који ревнује.
25 Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
Кад изродиш синове и унуке, и остарите у оној земљи, ако се покварите и начините слику резану од какве твари и учините шта није угодно Господу Богу вашем, дражећи Га,
26 ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
Сведочим вам данас небом и земљом да ће вас брзо нестати са земље у коју идете преко Јордана да је наследите, нећете бити дуго у њој, него ћете се истребити.
27 Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
Или ће вас расејати Господ међу народе, и мало ће вас остати међу народима у које вас одведе Господ;
28 Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
И служићете онде боговима које су начиниле руке човечије, од дрвета и од камена, који не виде ни чују, нити једу ни миришу.
29 Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Али ако и онде потражиш Господа Бога свог, наћи ћеш Га, ако Га потражиш свим срцем својим и свом душом својом.
30 Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
Кад будеш у невољи и све те то снађе, ако се у последње време обратиш ка Господу Богу свом, и послушаш глас Његов,
31 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
Господ је Бог твој милостив Бог, неће те оставити ни истребити, јер неће заборавити завет с оцима твојим, за који им се заклео.
32 Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
Јер запитај сада за стара времена, која су била пре тебе, од оног дана кад створи Бог човека на земљи, и од једног краја неба до другог, је ли кад била оваква ствар велика, и је ли се кад чуло шта такво?
33 Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
Је ли кад чуо који народ глас Божји где говори исред огња, као што си ти чуо и остао жив?
34 Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
Или, је ли Бог покушао да дође те узме себи народ из другог народа кушањем, знацима и чудесима и ратом и руком крепком и мишицом подигнутом и страхотама великим, као што је учинио све то за вас Господ Бог наш у Мисиру на ваше очи?
35 Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
Теби је то показано да познаш да је Господ Бог, и да нема другог осим Њега.
36 Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
Дао ти је да чујеш глас Његов с неба да би те научио, и показао ти је на земљи огањ свој велики, и речи Његове чуо си исред огња.
37 Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
И што му мили беху оци твоји, зато изабра семе њихово након њих, и изведе те сам великом силом својом из Мисира,
38 kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
Да отера испред тебе народе веће и јаче од тебе, и да тебе уведе у њихову земљу и даде ти је у наследство, као што се види данас.
39 Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
Знај дакле и памти у срцу свом да је Господ Бог, горе на небу и доле на земљи, нема другог.
40 Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
И држи уредбе Његове и заповести Његове, које ти ја данас заповедам, да би добро било теби и синовима твојим након тебе, да би ти се продужили дани на земљи коју ти Господ Бог твој даје засвагда.
41 Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
Тада одели Мојсије три града с ове стране Јордана према истоку,
42 kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
Да би бежао у њих крвник који убије ближњег свог нехотице не мрзевши пре на њ, и кад побегне у који од тих градова, да би остао жив:
43 Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
Восор у пустињи, на равници у земљи племена Рувимовог, и Рамот у Галаду у племену Гадовом, Голан у васанској у племену Манасијином.
44 Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
Ово је закон који постави Мојсије синовима Израиљевим.
45 Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
Ово су сведочанства и уредбе и закони, које каза Мојсије синовима Израиљевим кад изиђоше из Мисира,
46 Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
С ове стране Јордана у долини према Вет-Фегору у земљи Сиона цара аморејског, који живљаше у Есевону, ког уби Мојсије и синови Израиљеви кад изиђоше из Мисира,
47 Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
И освојише земљу његову и земљу Ога, цара васанског, два цара аморејска, која је с оне стране Јордана према истоку,
48 Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
Од Ароира, који је на потоку Арнону, до горе Сиона, а то је Ермон,
49 ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.
И све поље с ове стране Јордана према истоку до мора уз равницу под Аздот-Фазгом.

< Deuteronomo 4 >