< Deuteronomo 4 >

1 Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
Teraz więc, o Izraelu, słuchaj nakazów i praw, których uczę was wypełniać, abyście żyli i weszli, i posiedli ziemię, którą daje wam PAN, Bóg waszych ojców.
2 Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
Nie dodawajcie do słowa, które ja wam nakazuję, ani z niego nie ujmujcie, abyście przestrzegali przykazań PANA, waszego Boga, które ja wam nakazuję.
3 Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
Wasze oczy widziały, co PAN uczynił z powodu Baal-Peora, jak każdego człowieka, który poszedł za Baal-Peorem, PAN, twój Bóg, wytracił spośród was.
4 Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
A wy, którzy przylgnęliście do PANA, swojego Boga, żyjecie wszyscy aż do dziś.
5 Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
Spójrzcie, nauczyłem was nakazów i praw, jak mi nakazał PAN, mój Bóg, abyście tak czynili w tej ziemi, do której wchodzicie, aby ją wziąć w posiadanie.
6 Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
Przestrzegajcie [ich] więc i wypełniajcie je; to bowiem [jest] wasza mądrość i wasz rozum w oczach narodów, które usłyszą o wszystkich tych nakazach i powiedzą: Zaprawdę, ten wielki naród jest mądrym i rozumnym ludem.
7 Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
Który bowiem naród jest tak wielki, by mieć bogów tak bliskich jak PAN, nasz Bóg, we wszystkim, ilekroć go wzywamy?
8 Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
Albo który naród [jest tak] wielki, by mieć nakazy i prawa [tak] sprawiedliwe jak całe to prawo, które dziś wam przedkładam?
9 Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
Tylko miej się na baczności i strzeż swej duszy pilnie, abyś nie zapomniał o tych rzeczach, które twoje oczy widziały, i aby nie odstępowały [one] od twego serca po wszystkie dni twego życia. Ale ucz ich swoich synów i synów swoich synów.
10 Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
[Nie zapominaj] o dniu, w którym stałeś przed PANEM, swoim Bogiem, na Horebie, gdy PAN powiedział do mnie: Zgromadź mi lud, abym im przekazał swoje słowa, aby nauczyli się mnie bać przez wszystkie dni swego życia na ziemi i żeby uczyli [tego] swoich synów.
11 Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
Wtedy zbliżyliście się i stanęliście pod górą, a góra płonęła ogniem aż po samo niebo, [okryta] ciemnością, obłokiem i mrokiem.
12 Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
I PAN przemówił do was spośród ognia. Usłyszeliście dźwięk słów, lecz nie widzieliście żadnej postaci, tylko głos [usłyszeliście].
13 Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
Wówczas oznajmił wam swoje przymierze, które nakazał wam wypełniać, dziesięć przykazań, które napisał na dwóch kamiennych tablicach.
14 Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
W tym czasie PAN rozkazał mi nauczać was nakazów i praw, abyście je wypełniali w ziemi, do której idziecie, aby ją wziąć w posiadanie.
15 Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
Strzeżcie więc pilnie swoich dusz, gdyż nie widzieliście żadnej postaci w dniu, w którym PAN przemówił do was na Horebie spośród ognia;
16 kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
Abyście się nie zepsuli i nie czynili sobie rzeźbionego posągu, podobizny wszelkiej postaci w kształcie mężczyzny lub kobiety;
17 kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
W kształcie jakiegokolwiek zwierzęcia, które jest na ziemi, w kształcie wszelkiego ptaka skrzydlatego, który lata w powietrzu;
18 Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
W kształcie czegokolwiek, co pełza po ziemi, w kształcie wszelkiej ryby, która jest w wodach pod ziemią.
19 Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
I abyś – gdy podniesiesz swoje oczy ku niebu i ujrzysz słońce, księżyc i gwiazdy, cały zastęp niebios – nie dał się zwieść, by oddać im pokłon i im służyć, ponieważ PAN, twój Bóg, przydzielił je wszystkim ludom pod całym niebem.
20 Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
Lecz PAN was wziął i wyprowadził z pieca do topienia żelaza, z Egiptu, abyście byli jego ludem, jego dziedzictwem, jak dziś [jesteście].
21 Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
I PAN rozgniewał się na mnie z waszego powodu, i przysiągł, że nie przejdę Jordanu i nie wejdę do tej dobrej ziemi, którą PAN, twój Bóg, daje tobie w dziedzictwo.
22 Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
Ja bowiem umrę w tej ziemi, nie przejdę Jordanu. Wy zaś przejdziecie i posiądziecie tę dobrą ziemię.
23 Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
Strzeżcie się, abyście nie zapomnieli o przymierzu PANA, swojego Boga, które z wami zawarł, i nie czynili sobie żadnego rzeźbionego posągu lub podobizny czegokolwiek, czego ci zakazał PAN, twój Bóg.
24 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
Bo PAN, twój Bóg, jest ogniem trawiącym, Bogiem zazdrosnym.
25 Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
Gdy urodzisz synów i wnuki i zestarzejecie się w tej ziemi, jeśli popsujecie się i uczynicie [sobie] rzeźbiony posąg lub podobiznę czegokolwiek, i dopuścicie się zła w oczach PANA, swojego Boga, pobudzając go do gniewu;
26 ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
To biorę dziś na świadków przeciwko wam niebo i ziemię, że prędko wyginiecie doszczętnie z ziemi, do której przejdziecie przez Jordan, aby ją posiąść; nie przedłużycie w niej swych dni, bo zostaniecie całkowicie wytępieni.
27 Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
PAN rozproszy was między narodami i mało z was zostanie pośród narodów, do których PAN was zaprowadzi.
28 Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
Tam będziecie służyli bogom, dziełom ludzkich rąk, drewnu i kamieniowi, które nie widzą ani nie słyszą, nie jedzą ani nie wąchają.
29 Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Jeśli jednak stamtąd będziesz szukać PANA, swego Boga, wtedy znajdziesz [go], jeśli będziesz go szukał całym swym sercem i całą swą duszą.
30 Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
Gdy znajdziesz się w ucisku i spotka cię to wszystko w ostatnich dniach, jeśli wtedy zawrócisz do PANA, swego Boga, i będziesz słuchał jego głosu;
31 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
Ponieważ PAN, twój Bóg, jest miłosiernym Bogiem, nie opuści cię ani cię nie zniszczy, ani nie zapomni o przymierzu z twoimi ojcami, które im poprzysiągł.
32 Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
Zapytaj się bowiem dawnych czasów, które były przed tobą od dnia, kiedy Bóg stworzył człowieka na ziemi, i od jednego krańca nieba aż do drugiego, czy stała się kiedykolwiek rzecz podobna do tej tak wielkiej albo czy słyszano kiedykolwiek o czymś takim?
33 Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
Czy słyszał [kiedykolwiek jakiś] naród głos Boga mówiącego spośród ognia, tak jak ty słyszałeś, i pozostał żywy?
34 Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
Albo czy Bóg spróbował przyjść i wziąć sobie naród spośród [innego] narodu przez doświadczenia, przez znaki, przez cuda i przez wojny, potężną ręką i wyciągniętym ramieniem, wśród wielkich i strasznych [dzieł] jak to wszystko, co na twoich oczach PAN, wasz Bóg, uczynił dla was w Egipcie?
35 Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
Tobie to ukazano, abyś wiedział, że PAN jest Bogiem i nie ma innego oprócz niego.
36 Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
Dał ci słyszeć swój głos z nieba, aby cię pouczyć, a na ziemi ukazał ci swój wielki ogień i usłyszałeś jego słowa spośród ognia.
37 Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
A ponieważ umiłował twoich ojców, wybrał ich potomstwo po nich i wyprowadził cię z Egiptu przed sobą swoją wielką mocą;
38 kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
Aby wypędzić przed tobą narody większe i potężniejsze od ciebie, by cię wprowadzić i dać ci ich ziemię w dziedzictwo, jak to [jest] dzisiaj.
39 Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
Poznaj więc dziś i weź to sobie do swego serca, że PAN jest Bogiem wysoko na niebie i nisko na ziemi. Nie ma innego.
40 Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
Przestrzegaj więc jego nakazów i przykazań, które dziś tobie nakładam, aby się dobrze powodziło tobie i twoim synom po tobie; abyś też przedłużył swe dni na ziemi, którą PAN, twój Bóg, daje tobie przez wszystkie dni.
41 Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
Wtedy Mojżesz wydzielił trzy miasta po tej stronie Jordanu na wschodzie;
42 kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
Aby mógł tam uciec zabójca, który zabił swego bliźniego nieumyślnie i wcześniej nie nienawidził go, aby uciekł [on] do jednego z tych miast i pozostał żywy:
43 Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
Beser na pustyni, w ziemi równinnej Rubenitów, Ramot w Gileadzie Gadytów i Golan w Baszanie Manassytów.
44 Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
Oto prawo, które Mojżesz przedłożył synom Izraela.
45 Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
To są świadectwa, nakazy i prawa, które Mojżesz ogłosił synom Izraela, kiedy wyszli z Egiptu;
46 Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
Po tej stronie Jordanu, w dolinie naprzeciw Bet-Peor, w ziemi Sichona, króla Amorytów, mieszkającego w Cheszbonie, którego Mojżesz i synowie Izraela pobili po wyjściu z Egiptu;
47 Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
I posiedli jego ziemię i ziemię Oga, króla Baszanu – dwóch królów Amorytów, którzy [byli] po tej stronie Jordanu na wschodzie;
48 Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
Od Aroeru, leżącego nad brzegiem rzeki Arnon, aż do góry Sirion, czyli Hermon;
49 ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.
I całą równinę po tej stronie Jordanu na wschodzie aż do Morza Pustego, pod zdrojami Pizga.

< Deuteronomo 4 >