< Deuteronomo 4 >

1 Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
اکنون ای اسرائیل، به قوانینی که به شما یاد می‌دهم به دقت گوش کنید و اگر می‌خواهید زنده مانده، به سرزمینی که خداوند، خدای پدرانتان به شما داده است داخل شوید و آن را تصاحب کنید از این دستورها اطاعت نمایید.
2 Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
قوانین دیگری به اینها نیفزایید و چیزی کم نکنید، بلکه فقط این دستورها را اجرا کنید؛ زیرا این قوانین از جانب خداوند، خدایتان می‌باشد.
3 Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
دیدید که چگونه یهوه خدایتان در بعل فغور همهٔ کسانی را که بت بعل را پرستیدند از بین برد،
4 Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
ولی همگی شما که به خداوند، خدایتان وفادار بودید تا به امروز زنده مانده‌اید.
5 Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
تمام قوانینی را که یهوه، خدایم به من داده است، به شما یاد داده‌ام. پس وقتی به سرزمین موعود وارد شده، آن را تسخیر نمودید از این قوانین اطاعت کنید.
6 Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
اگر این دستورها را اجرا کنید به داشتن حکمت و بصیرت مشهور خواهید شد. زمانی که قومهای مجاور، این قوانین را بشنوند خواهند گفت: «این قوم بزرگ از چه حکمت و بصیرتی برخوردار است!»
7 Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
هیچ قومی، هر قدر هم که بزرگ باشد، مثل ما خدایی مانند یهوه خدای ما ندارد که در بین آنها بوده، هر وقت او را بخوانند، فوری جواب دهد.
8 Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
هیچ قومی، هر قدر هم که بزرگ باشد، چنین احکام و قوانین عادلانه‌ای که امروز به شما یاد دادم، ندارد.
9 Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
ولی مواظب باشید و دقت کنید مبادا در طول زندگی‌تان آنچه را که با چشمانتان دیده‌اید فراموش کنید. همهٔ این چیزها را به فرزندان و نوادگانتان تعلیم دهید.
10 Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
به یاد آورید آن روزی را که در کوه حوریب در برابر خداوند ایستاده بودید و او به من گفت: «مردم را به حضور من بخوان و من به ایشان تعلیم خواهم داد تا یاد بگیرند همیشه مرا احترام کنند و دستورهای مرا به فرزندانشان بیاموزند.»
11 Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
شما در دامنهٔ کوه ایستاده بودید. ابرهای سیاه و تاریکی شدید اطراف کوه را فرا گرفته بود و شعله‌های آتش از آن به آسمان زبانه می‌کشید.
12 Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
آنگاه خداوند از میان آتش با شما سخن گفت. شما کلامش را می‌شنیدید، ولی او را نمی‌دیدید.
13 Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
او قوانینی را که شما باید اطاعت کنید یعنی «ده فرمان» را اعلام فرمود و آنها را بر دو لوح سنگی نوشت.
14 Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
آری، در همان وقت بود که خداوند به من دستور داد قوانینی را که باید بعد از رسیدن به سرزمین موعود اجرا کنید به شما یاد دهم.
15 Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
شما در آن روز در کوه حوریب وقتی که خداوند از میان آتش با شما سخن می‌گفت، شکل و صورتی از او ندیدید. پس مواظب باشید
16 kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
مبادا با ساختن مجسمه‌ای از خدا خود را آلوده سازید، یعنی با ساختن بُتی به هر شکل، چه به صورت مرد یا زن،
17 kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
و چه به صورت حیوان یا پرنده،
18 Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
خزنده یا ماهی.
19 Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
همچنین وقتی به آسمان نگاه می‌کنید و تمامی لشکر آسمان یعنی خورشید و ماه و ستارگان را که یهوه خدایتان برای تمام قومهای روی زمین آفریده است می‌بینید، آنها را پرستش نکنید.
20 Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
خداوند شما را از مصر، از آن کورهٔ آتش، بیرون آورد تا قوم خاص او و میراث او باشید، چنانکه امروز هستید.
21 Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
ولی به خاطر شما نسبت به من خشمناک گردید و به تأکید اعلام فرمود که من به آن سوی رود اردن یعنی به سرزمین حاصلخیزی که یهوه خدایتان به شما به میراث داده است نخواهم رفت.
22 Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
من اینجا در این سوی رودخانه خواهم مرد، ولی شما از رودخانه عبور خواهید کرد و آن زمین حاصلخیز را تصرف خواهید نمود.
23 Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
هوشیار باشید مبادا عهدی را که خداوند، خدایتان با شما بسته است بشکنید! اگر دست به ساختن هرگونه بُتی بزنید آن عهد را می‌شکنید، چون خداوند، خدایتان این کار را به کلی منع کرده است.
24 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
زیرا یهوه خدای شما آتشی سوزاننده و خدایی غیور است.
25 Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
حتی اگر سالها در سرزمین موعود ساکن بوده، در آنجا صاحب فرزندان و نوادگان شده باشید، ولی با ساختن بت خود را آلوده کرده با گناهانتان یهوه خدایتان را خشمگین سازید،
26 ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
زمین و آسمان را شاهد می‌آورم که در آن سرزمینی که با گذشتن از رود اردن آن را تصاحب خواهید کرد، نابود خواهید شد. عمرتان در آنجا کوتاه خواهد بود و به کلی نابود خواهید شد.
27 Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
خداوند شما را در میان قومها پراکنده خواهد کرد و تعدادتان بسیار کم خواهد شد.
28 Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
در آنجا، بتهایی را که از چوب و سنگ ساخته شده‌اند پرستش خواهید کرد، بتهایی که نه می‌بینند، نه می‌شنوند، نه می‌بویند و نه می‌خورند.
29 Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
ولی اگر شما دوباره شروع به طلبیدن خداوند، خدایتان کنید، زمانی او را خواهید یافت که با تمام دل و جانتان او را طلبیده باشید.
30 Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
وقتی در سختی باشید و تمام این حوادث برای شما رخ دهد، آنگاه سرانجام به خداوند، خدایتان روی آورده، آنچه را که او به شما بگوید اطاعت خواهید کرد.
31 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
یهوه، خدای شما رحیم است، پس او شما را ترک نکرده، نابود نخواهد نمود و عهدی را که با پدران شما بسته است فراموش نخواهد کرد.
32 Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
در تمامی تاریخ، از وقتی که خدا انسان را روی زمین آفرید، از یک گوشهٔ آسمان تا گوشهٔ دیگر جستجو کنید و ببینید آیا می‌توانید چیزی شبیه به این پیدا کنید که
33 Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
قومی صدای خدا را که از میان آتش با آنها سخن گفته است مثل شما شنیده و زنده مانده باشد!
34 Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
و آیا تا به حال خدایی کوشیده است که با فرستادن بلاهای ترسناک و آیات و معجزات و جنگ، و با دست نیرومند و بازوی افراشته و اعمال عظیم و ترسناک، قومی را از بردگی قومی دیگر رها سازد؟ ولی یهوه خدایتان همۀ این کارها را در برابر چشمان شما در مصر برای شما انجام داد.
35 Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
خداوند این کارها را کرد تا شما بدانید که فقط او خداست و کسی دیگر مانند او وجود ندارد.
36 Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
او هنگامی که از آسمان به شما تعلیم می‌داد اجازه داد که شما صدایش را بشنوید؛ او گذاشت که شما ستون بزرگ آتشش را روی زمین ببینید. شما حتی کلامش را از میان آتش شنیدید.
37 Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
چون او پدران شما را دوست داشت و اراده نمود که فرزندانشان را برکت دهد، پس شخص شما را از مصر با نمایش عظیمی از قدرت خود بیرون آورد.
38 kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
او قومهای دیگر را که قویتر و بزرگتر از شما بودند پراکنده نمود و سرزمینشان را به طوری که امروز مشاهده می‌کنید، به شما بخشید.
39 Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
پس امروز به خاطر آرید و فراموش نکنید که خداوند، هم خدای آسمانها و هم خدای زمین است و هیچ خدایی غیر از او وجود ندارد!
40 Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
شما باید قوانینی را که امروز به شما می‌دهم اطاعت کنید تا خود و فرزندانتان کامیاب بوده، تا به ابد در سرزمینی که خداوند، خدایتان به شما می‌بخشد زندگی کنید.
41 Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
آنگاه موسی سه شهر در شرق رود اردن تعیین کرد
42 kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
تا اگر کسی ناخواسته شخصی را بکشد بدون اینکه قبلاً با او دشمنی داشته باشد، برای فرار از خطر به آنجا پناه ببرد.
43 Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
این شهرها عبارت بودند از: باصر واقع در اراضی مسطح بیابان برای قبیلهٔ رئوبین، راموت در جلعاد برای قبیلهٔ جاد، و جولان در باشان برای قبیلهٔ منسی.
44 Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
وقتی قوم اسرائیل از مصر خارج شده و در شرق رود اردن در کنار شهر بیت‌فغور اردو زده بودند، موسی قوانین خدا را به آنها داد. (این همان سرزمینی بود که قبلاً اموری‌ها در زمان سلطنت سیحون پادشاه که پایتختش حشبون بود در آنجا سکونت داشتند و موسی و بنی‌اسرائیل وی را با مردمش نابود کردند.
45 Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
46 Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
47 Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
آنها بر سرزمین او و بر سرزمین عوج، پادشاه باشان که هر دو از پادشاهان اموری‌های شرق رود اردن بودند غلبه یافتند.
48 Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
این سرزمین از عروعیر در کنار رود ارنون تا کوه سریون که همان حرمون باشد، امتداد می‌یافت
49 ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.
و شامل تمام منطقهٔ شرق رود اردن که از جنوب به دریای مرده و از شرق به دامنهٔ کوه پیسگاه منتهی می‌شد، بود.)

< Deuteronomo 4 >