< Deuteronomo 4 >
1 Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
Khathesi-ke, Israyeli, zwana izimiso lezahlulelo engilifundisa zona, ukuzenza, ukuze liphile, lingene lidle ilifa lelizwe iNkosi uNkulunkulu waboyihlo elinika lona.
2 Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
Kaliyikwengezelela elizwini engililaya lona, lingaphunguli lutho kulo, ukuze ligcine imilayo yeNkosi uNkulunkulu wenu engililaya yona.
3 Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
Amehlo enu abonile iNkosi eyakwenzayo ngenxa kaBhali-Peyori; ngoba wonke umuntu owalandela uBhali-Peyori, iNkosi uNkulunkulu wenu yambhubhisa phakathi kwenu;
4 Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
kodwa lina elanamathela eNkosini uNkulunkulu wenu liyaphila lonke lamuhla.
5 Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
Bonani, ngilifundisile izimiso lezahlulelo, njengokungilaya kweNkosi uNkulunkulu wami, ukuthi lenze njalo phakathi kwelizwe eliya kulo ukudla ilifa lalo.
6 Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
Ngakho zigcineni, lizenze; ngoba lokhu kuyinhlakanipho yenu lokuqedisisa kwenu emehlweni ezizwe ezizakuzwa zonke lezizimiso zithi: Isibili lesisizwe esikhulu singabantu abahlakaniphileyo labaqedisisayo.
7 Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
Ngoba yisiphi isizwe esikhulu esilabonkulunkulu abaseduze laso njengeNkosi uNkulunkulu ekumbizeni kwethu konke?
8 Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
Futhi yisiphi isizwe esikhulu esilezimiso lezahlulelo ezilungileyo njengalumlayo wonke engiwubeka phambi kwenu lamuhla?
9 Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
Kuphela ziqaphele, ugcine kakhulu umphefumulo wakho, hlezi ukhohlwe izinto amehlo akho azibonileyo, njalo hlezi zisuke enhliziyweni yakho, zonke izinsuku zempilo yakho. Njalo uzazise abantwana bakho labantwana babantwana bakho,
10 Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
ukuthi ngosuku owema ngalo phambi kweNkosi uNkulunkulu wakho eHorebe, lapho iNkosi yathi kimi: Ngibuthanisela abantu ngibe sengibazwisa amazwi ami, ukuze bafunde ukungesaba zonke izinsuku abazaziphila emhlabeni, bafundise njalo abantwana babo.
11 Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
Laselisondela, lema ngaphansi kwentaba, lentaba yayivutha umlilo kwaze kwaba phakathi kwamazulu, lomnyama, amayezi, lomnyama onzima.
12 Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
INkosi yasikhuluma kini iphakathi komlilo; lezwa ilizwi lamazwi, kodwa kalibonanga simo; ilizwi kuphela.
13 Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
Yamemezela kini isivumelwano sayo, eyalilaya ukuthi lisenze, imilayo elitshumi; njalo yayibhala ezibhebheni zamatshe ezimbili.
14 Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
INkosi yasingilaya ngalesosikhathi ukuthi ngilifundise izimiso lezahlulelo, ukuze lizenze elizweni elidlulela kulo ukudla ilifa lalo.
15 Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
Ngakho-ke qaphelani kakhulu ngenxa yemiphefumulo yenu. Ngoba kalibonanga lasimo ngosuku iNkosi ikhuluma kini eHorebe iphakathi komlilo,
16 kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
hlezi lizone, lizenzele isithombe esibaziweyo, isimo saloba yiwuphi umfanekiso, isifanekiso sowesilisa loba sowesifazana,
17 kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
isifanekiso saloba yiyiphi inyamazana esemhlabeni, isifanekiso saloba yiyiphi inyoni elempiko ephapha emazulwini,
18 Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
isifanekiso saloba yikuphi okuhuquzelayo emhlabeni, isifanekiso saloba yiyiphi inhlanzi esemanzini ngaphansi komhlaba.
19 Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
Futhi hlezi uphakamisele amehlo akho emazulwini, lapho ubona ilanga lenyanga lezinkanyezi, ibutho lonke lamazulu, uyengwe, ukukhothamele, ukukhonze, iNkosi uNkulunkulu wakho ekwabele izizwe zonke ngaphansi kwamazulu wonke.
20 Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
Kodwa lina iNkosi yalithatha, yalikhupha esithandweni sensimbi, eGibhithe, ukuze libe kuyo ngabantu belifa, njengalamuhla.
21 Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
Futhi iNkosi yangithukuthelela ngenxa yenu, yafunga ukuthi kangiyikuchapha iJordani, lokuthi kangiyikungena kulelolizwe elihle iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona libe yilifa.
22 Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
Ngoba ngizafela kulelilizwe, ngingachaphi iJordani; kodwa lina lizachapha, lidle ilifa lalelolizwe elihle.
23 Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
Ziqapheleni hlezi likhohlwe isivumelwano seNkosi uNkulunkulu wenu eyasenza lani, lizenzele isithombe esibaziweyo, umfanekiso waloba yikuphi iNkosi uNkulunkulu wakho ekwenqabele khona.
24 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
Ngoba iNkosi uNkulunkulu wakho ingumlilo oqothulayo, uNkulunkulu olobukhwele.
25 Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
Lapho uzala abantwana labantwana babantwana, njalo selihlale elizweni isikhathi eside, uba lisonakala, lenze isithombe esibaziweyo, umfanekiso waloba yikuphi, lenze okubi emehlweni eNkosi uNkulunkulu wakho ukuze liyithukuthelise,
26 ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
ngibiza amazulu lomhlaba lamuhla ukuze kufakaze kumelene lani ukuthi lizabhubha lokubhubha masinyane lisuka elizweni elichapha iJordani ukuya kilo ukuze libe yilifa lenu; kaliyikwelula insuku zenu phezu kwalo, ngoba lizabhujiswa lokubhujiswa.
27 Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
Njalo iNkosi izalichithachitha phakathi kwezizwe, lisale libalutshwana ngenani phakathi kwezizwe, lapho iNkosi ezalixotshela khona.
28 Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
Lapho lizakhonza onkulunkulu, umsebenzi wezandla zabantu, izigodo lamatshe, abangaboniyo, abangezwayo, abangadliyo, labanganukiyo.
29 Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Kodwa lilapho liyidinge iNkosi uNkulunkulu wakho, uzayithola uba uyidinga ngenhliziyo yakho yonke langomphefumulo wakho wonke.
30 Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
Lapho usekuhluphekeni, lezizinto zonke zikwehlela, ekupheleni kwezinsuku, uzaphendukela eNkosini uNkulunkulu wakho, ulalele ilizwi layo;
31 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
ngoba iNkosi uNkulunkulu wakho inguNkulunkulu olomusa, kayiyikukutshiya, kayiyikukubhubhisa, kayiyikukhohlwa isivumelwano saboyihlo, eyasifunga kubo.
32 Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
Ngoba buza-ke ngensuku zamandulo ezazingaphambi kwakho, kusukela osukwini uNkulunkulu adala ngalo umuntu emhlabeni, kusukela komunye umkhawulo wamazulu kuze kube komunye umkhawulo wamazulu, ukuthi kwake kwaba khona yini into enje njengale into enkulu, kumbe kwezwakala enjengayo yini?
33 Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
Abantu bake bezwa yini ilizwi likaNkulunkulu likhuluma livela phakathi komlilo, njengalokhu ulizwile wena, waphila?
34 Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
Futhi uNkulunkulu wake wazama yini ukuyazithathela isizwe phakathi kwesizwe, ngezilingo, ngezibonakaliso, langezimangaliso, langempi, langesandla esilamandla, langengalo eyeluliweyo, langezesabiso ezinkulu, njengakho konke iNkosi uNkulunkulu wenu eyalenzela khona eGibhithe phambi kwamehlo akho?
35 Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
Wena wakutshengiswa, ukuze wazi ukuthi uJehova unguNkulunkulu; kakho omunye ngaphandle kwakhe.
36 Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
Esemazulwini wakuzwisa ilizwi lakhe ukukufundisa; lemhlabeni wakutshengisa umlilo wakhe omkhulu, lamazwi akhe wawezwa evela phakathi komlilo.
37 Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
Njalo ngoba wabathanda oyihlo, wakhetha inzalo yabo emva kwabo, wakukhupha eGibhithe ebusweni bakhe ngamandla akhe amakhulu,
38 kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
ukuxotsha elifeni izizwe ezinkulu lezilamandla kulawe phambi kwakho, ukukungenisa, ukukupha ilizwe lazo, libe yilifa, njengalamuhla.
39 Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
Ngakho yazi lamuhla, ukukhumbule enhliziyweni yakho ukuthi iNkosi inguNkulunkulu emazulwini phezulu, lemhlabeni phansi; kakho omunye.
40 Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
Ngakho uzagcina izimiso zakhe lemilayo yakhe engikulaya yona lamuhla, ukuze kukulungele labantwana bakho emva kwakho, lokuze welule izinsuku phezu kwelizwe iNkosi uNkulunkulu wakho ekunika lona, zonke izinsuku.
41 Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
Khona uMozisi wehlukanisa imizi emithathu nganeno kweJordani ngasempumalanga,
42 kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
ukuthi abalekele kuyo umbulali obulele umakhelwane wakhe kungeyisikho ngabomo, obengamzondi mandulo, ukuze abalekele komunye waleyomizi aphile;
43 Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
iBezeri enkangala elizweni lamagceke, elabakoRubeni; leRamothi eGileyadi, elabakoGadi; leGolani eBashani, elabakoManase.
44 Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
Njalo yilo umlayo uMozisi awubeka phambi kwabantwana bakoIsrayeli.
45 Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
Lobu yibufakazi lezimiso lezahlulelo uMozisi akukhuluma ebantwaneni bakoIsrayeli ekuphumeni kwabo eGibhithe,
46 Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
nganeno kweJordani, esigodini maqondana leBeti-Peyori, elizweni likaSihoni inkosi yamaAmori, owayehlala eHeshiboni, uMozisi labantwana bakoIsrayeli abamtshayayo ekuphumeni kwabo eGibhithe.
47 Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
Basebesidla ilifa lelizwe lakhe lelizwe likaOgi inkosi yeBashani, amakhosi amabili amaAmori, ayenganeno kweJordani ngasempumalanga,
48 Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
kusukela eAroweri esekhunjini lwesifula seArinoni, kuze kufike entabeni yeSiyoni, eyiHermoni,
49 ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.
lamagceke wonke nganeno kweJordani ngasempumalanga, kuze kube selwandle lwamagceke, ngaphansi kweAshidodi-Pisiga.